< Nombres 9 >

1 Le Seigneur parla à Moïse dans le désert de Sinaï, à la seconde année après qu’ils furent sortis de la terre d’Egypte, au premier mois, disant:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
2 Que les enfants d’Israël fassent la Pâque en son temps,
“Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
3 Au quatorzième jour de ce mois, vers le soir, selon toutes ses cérémonies et ses ordonnances.
Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
4 Et Moïse ordonna aux enfants d’Israël qu’ils feraient la Pâque.
Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
5 Ils la firent en son temps, au quatorzième jour du mois, sur la montagne de Sinaï. Les enfants d’Israël firent selon tout ce qu’avait commandé le Seigneur à Moïse.
ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 Or voici que quelques-uns, impurs à cause de l’âme d’un homme, et qui ne pouvaient faire la Pâque en ce jour-là, s’approchant de Moïse et d’Aaron,
Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
7 Leur dirent: Nous sommes impurs à cause de l’âme d’un homme: pourquoi sommes-nous frustrés de pouvoir offrir l’offrande au Seigneur en son temps parmi les enfants d’Israël?
ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
8 Moïse leur répondit: Attendez que je consulte le Seigneur sur ce qu’il ordonnera de vous.
Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
9 Et le Seigneur parla à Moïse, disant:
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
10 Dis aux enfants d’Israël: Qu’un homme dans votre nation qui sera impur à cause d’une âme, ou en voyage au loin, fasse la Pâque du Seigneur
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
11 Au second mois, au quatorzième jour du mois, vers le soir; c’est avec des azymes et des laitues sauvages qu’il la mangera;
Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
12 Il n’en laissera rien jusque au matin et il n’en rompra point les os: il observera tout le rite de la Pâque.
Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
13 Mais si quelqu’un est même pur, et n’est point en voyage, et que cependant il ne fasse point la Pâque, cette âme sera exterminée du milieu de ses peuples; parce qu’il n’a pas offert de sacrifice au Seigneur en son temps: il portera lui-même son péché.
Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
14 Un voyageur aussi et un étranger, s’ils se trouvent chez vous, feront la Pâque du Seigneur selon ses cérémonies et ses ordonnances. Ce sera un précepte parmi vous, tant pour l’étranger que pour l’indigène.
“‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
15 Donc au jour que fut dressé le tabernacle, la nuée le couvrit. Mais depuis le soir, il y eut sur la tente comme une espèce de feu jusqu’au matin.
Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
16 Ainsi arrivait-il toujours: pendant le jour la nuée couvrait le tabernacle, et pendant la nuit, comme une espèce de feu.
Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
17 Et lorsque la nuée qui couvrait le tabernacle était enlevée, les enfants d’Israël partaient; et dans le lieu où elle s’arrêtait, là ils campaient.
Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
18 Au commandement du Seigneur ils partaient, et à son commandement ils dressaient le tabernacle. Pendant tous les jours que la nuée se tenait sur le tabernacle, ils demeuraient dans le même lieu.
Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
19 Et s’il arrivait qu’elle demeurât longtemps sur lui, les enfants d’Israël étaient en observation du Seigneur, et partaient pas,
Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
20 Autant de jours que la nuée était sur le tabernacle. Au commandement du Seigneur, ils dressaient les tentes, et à son commandement, ils les enlevaient.
Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
21 Si la nuée restait depuis le soir jusqu’au matin, et qu’aussitôt le point du jour elle quittât le tabernacle, ils partaient: et si après un jour et une nuit elle se retirait, ils détendaient les tentes.
Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
22 Mais si elle était deux jours, ou un mois ou plus longtemps sur le tabernacle, les enfants d’Israël demeuraient dans le même lieu et ne partaient pas; mais dès qu’elle s’était retirée, ils levaient le camp.
Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
23 C’était sur la parole du Seigneur qu’ils plantaient les tentes, et sur sa parole qu’ils partaient: et ils étaient en observation du Seigneur, selon son commandement par l’entremise de Moïse.
Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

< Nombres 9 >