< Nombres 4 >

1 Le Seigneur parla encore à Moïse et à Aaron, disant:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Fais le dénombrement des fils de Caath d’entre les Lévites, selon leurs familles et leurs maisons,
“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
3 Depuis trente ans et au dessus, jusqu’à cinquante ans, de tous ceux qui entrent, pour se tenir et servir dans le tabernacle d’alliance.
Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
4 Voici la fonction des fils de Caath: C’est dans le tabernacle et le Saint des saints
“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
5 Qu’entreront Aaron et ses fils, quand le camp devra être levé, et ils ôteront le voile qui est suspendu devant la porte, et ils en envelopperont l’arche du témoignage,
Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
6 Et ils le couvriront encore d’une couverture de peaux violettes, et ils étendront par-dessus un drap tout d’hyacinthe, et ils introduiront les leviers.
Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
7 Ils envelopperont aussi la table de proposition d’un drap d’hyacinthe, et ils mettront avec elle les encensoirs, les petits mortiers, les tasses et les coupes pour faire les libations; et les pains seront toujours sur elle;
“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
8 Et ils étendront par-dessus un drap d’écarlate qu’ils couvriront encore d’une couverture de peaux violettes, et ils y introduiront les leviers.
Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
9 Ils prendront de plus un drap d’hyacinthe dont ils couvriront le chandelier avec ses lampes, ses pincettes, ses mouchettes et tous les vases d’huile qui sont nécessaires pour entretenir les lampes.
“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
10 Et sur toutes ces choses ils poseront une couverture de peaux violettes, et ils introduiront les leviers.
Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
11 Et l’autel d’or aussi, ils l’envelopperont d’un drap d’hyacinthe, et ils étendront par-dessus une couverture de peaux violettes, et ils y introduiront les leviers.
“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
12 Tous les vases avec lesquels se fait le service dans le sanctuaire, ils les envelopperont dans un drap d’hyacinthe, et ils étendront par-dessus une couverture de peaux violettes, et ils introduiront les leviers.
“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
13 Mais ils nettoieront aussi l’autel de ses cendres, et ils l’envelopperont dans un drap de pourpre,
“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
14 Et ils y mettront avec lui tous les vases dont ils se servent pour son ministère, c’est-à-dire les brasiers, les fourchettes, les tridents, les crocs et les pelles. Ils couvriront ensemble tous les vases de l’autel d’une couverture de peaux violettes, et ils introduiront les leviers.
Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
15 Or, lorsque Aaron et ses fils auront enveloppé le sanctuaire et tous ses vases, au lever du camp, les fils de Caath entreront pour les porter ainsi enveloppés; mais ils ne toucheront point les vases du sanctuaire, de peur qu’ils ne meurent. Telles sont dans le tabernacle d’alliance les charges des fils de Caath,
“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
16 Au-dessus desquels sera Eléazar, fils d’Aaron, le prêtre, au soin de qui appartient l’huile pour entretenir les lampes, le parfum de composition, le sacrifice perpétuel, l’huile de l’onction et tout ce qui appartient au service du tabernacle et de tous les vases qui sont dans le tabernacle.
“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
17 Le Seigneur parla encore à Moïse et à Aaron, disant:
Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
18 Ne détruisez point le peuple de Caath du milieu des Lévites;
“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
19 Mais faites ceci pour eux, afin qu’ils vivent et qu’ils ne meurent point, s’ils touchent le Saint des saints. Aaron et ses fils entreront, et ils disposeront eux-mêmes les ouvrages de tous séparément, et ils partageront ce que chacun doit porter.
Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
20 Que les autres ne voient nullement avec curiosité ce qui est dans le sanctuaire, avant qu’il soit enveloppé, autrement ils mourront.
Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
21 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
22 Fais aussi le dénombrement des enfants de Gerson, selon leurs maisons, leurs familles et leur parenté,
“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
23 Depuis trente ans et au-dessus jusqu’à cinquante ans. Dénombre tous ceux qui entrent et qui servent dans le tabernacle d’alliance.
Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
24 L’office de la famille des Gersonites est,
“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
25 Qu’ils portent les rideaux du tabernacle et le toit d’alliance, l’autre couverture, puis la couverture violette qui est par-dessus tout, et le voile qui est suspendu à l’entrée du tabernacle d’alliance;
Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 Les rideaux du parvis et le voile de l’entrée, qui est devant le tabernacle. Tout ce qui appartient à l’autel, les cordages et les vases de service,
makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
27 Au commandement d’Aaron et de ses fils, les fils de Gerson le porteront, et chacun saura à quelle charge il doit être soumis.
Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
28 Tel est l’emploi de la famille des Gersonites dans le tabernacle d’alliance; et ils seront sous la main d’Ithamar, fils d’Aaron le prêtre.
Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
29 Tu recenseras aussi les fils de Mérari selon leurs maisons et les familles de leurs pères,
“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
30 Depuis trente ans et au-dessus jusqu’à cinquante ans, tous ceux qui entrent pour l’office de leur ministère, et le service de l’alliance de témoignage.
Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
31 Voici leurs charges: ils porteront les ais du tabernacle, ses leviers, ses colonnes et leurs soubassements,
Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
32 Et aussi les colonnes autour du parvis avec leurs soubassements, leurs pieux et leurs cordages. Ils prendront le compte de tous les vases et des autres objets, et c’est ainsi qu’ils les porteront.
ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
33 Tel est l’office des familles des Mérarites et leur ministère dans le tabernacle d’alliance; et ils sont sous la main d’Ithamar, fils d’Aaron, le prêtre.
Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
34 Moïse donc, Aaron et les princes de la synagogue recensèrent les fils de Caath, selon leur parenté et les maisons de leurs pères,
Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
35 Depuis trente ans et au-dessus jusqu’à cinquante ans, tous ceux qui entrent au service du tabernacle d’alliance;
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
36 Et il s’en trouva deux mille sept cent cinquante.
atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
37 C’est là le nombre du peuple de Caath qui entrent dans le tabernacle d’alliance: Moïse et Aaron les dénombrèrent, selon la parole du Seigneur, par l’entremise de Moïse.
Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
38 Les fils de Gerson aussi furent dénombrés selon leur parenté et les maisons de leurs pères,
Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
39 Depuis trente ans et au-dessus, jusqu’à cinquante ans, tous ceux qui entrent pour servir dans le tabernacle d’alliance;
Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
40 Et il s’en trouva deux mille six cent trente.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
41 C’est là le peuple des Gersonites, que dénombrèrent Moïse et Aaron, selon la parole du Seigneur.
Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
42 Ensuite furent dénombrés les fils de Mérari selon leur parenté et les maisons de leurs pères,
Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
43 Depuis trente ans et au-dessus, jusqu’à cinquante ans, tous ceux qui entrent pour accomplir les rites du tabernacle d’alliance;
Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
44 Et il s’en trouva trois mille deux cents.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
45 Tel est le nombre des fils de Mérari que recensèrent Moïse et Aaron, selon l’ordre du Seigneur, par l’entremise de Moïse.
Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
46 Tous ceux qui furent recensés d’entre les Lévites, et que firent recenser par leurs noms, Moïse, Aaron et les princes d’Israël, selon leur parenté et les maisons de leurs pères,
Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
47 Depuis trente ans et au-dessus, jusqu’à cinquante ans, entrant pour le service du tabernacle et pour porter les fardeaux,
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
48 Furent en tout huit mille cinq cent quatre-vingts.
analipo 8,580.
49 C’est selon la parole du Seigneur que Moïse les recensa, chacun selon son office et ses charges, comme lui avait ordonné le Seigneur.
Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.

< Nombres 4 >