< Nombres 32 >
1 Or les enfants de Ruben et de Gad avaient beaucoup de troupeaux, et ils possédaient en bestiaux d’immenses richesses. Lors donc qu’ils eurent vu que les terres de Jazer et de Galaad étaient propres à nourrir des animaux,
Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
2 Ils vinrent vers Moïse et Eléazar, le prêtre, et les princes de la multitude, et dirent:
Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
3 Ataroth, Dibon, Jazer, Nemra, Hésébon, Saban, Nébo et Béon,
“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
4 Terre qu’a frappée le Seigneur en la présence des enfants d’Israël, est une contrée très fertile pour le pâturage des animaux: et nous, tes serviteurs, nous avons des bestiaux en très grand nombre:
dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
5 Nous prions donc, si nous avons trouvé grâce devant toi, pour que tu la donnes à tes serviteurs en possession, et que tu ne nous fasses point passer le Jourdain.
Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
6 Moïse leur répondit: Est-ce que vos frères iront au combat, et vous, vous demeurerez ici?
Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
7 Pourquoi bouleversez-vous les esprits des enfants d’Israël, afin qu’ils n’osent passer dans la terre que doit leur donner le Seigneur?
Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
8 N’est-ce pas ainsi qu’ont agi vos pères, lorsque je les envoyai à Cadesbarné pour explorer cette terre?
Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
9 Car, lorsqu’il furent venus jusqu’à la Vallée de la grappe de raisin, toute la contrée parcourue, ils bouleversèrent le cœur des enfants d’Israël, afin qu’ils n’entrassent point dans le pays que le Seigneur leur donna.
Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
10 Le Seigneur, irrité, jura, disant:
Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
11 Ils ne verront pas, ces hommes qui sont montés de l’Egypte depuis vingt ans et au-dessus, la terre que j’ai promise sous serment à Abraham, Isaac et Jacob, et qui n’ont pas voulu me suivre,
‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
12 Excepté Caleb, fils de Jéphoné, le Cénézéen, et Josué, fils de Nun: ceux-ci ont accompli ma volonté.
Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
13 Et le Seigneur, irrité contre Israël, lui fit faire un détour par le désert pendant quarante ans, jusqu’à ce que fut détruite toute la génération qui avait fait le mal en sa présence.
Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 Et voilà que vous, vous avez surgi à la place de vos pères, rejetons et nourrissons d’hommes pécheurs, pour augmenter la fureur du Seigneur contre d’Israël.
“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
15 Si vous ne voulez point le suivre, il abandonnera le peuple dans le désert, et vous serez la cause de la mort de tous.
Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 Mais eux, s’approchant plus près, dirent: Nous ferons des parcs de brebis et des étables de bestiaux, et aussi pour nos petits enfants des villes fortifiées;
Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
17 Mais nous-mêmes, armés et équipés, nous marcherons au combat devant les enfants d’Israël, jusqu’à ce que nous les introduisions dans leurs terres. Nos petits enfants, et tout ce que nous pouvons avoir seront dans des villes murées, à cause des embûches des habitants.
Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
18 Nous ne retournerons point dans nos maisons, jusqu’à ce que les enfants d’Israël possèdent leur héritage;
Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
19 Et nous ne chercherons rien au-delà du Jourdain, parce que nous avons déjà notre possession au côté oriental de ce fleuve.
Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 Moïse leur répondit: Si vous faites ce que vous promettez, marchez devant le Seigneur, tout prêts au combat;
Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
21 Et que tout guerrier, armé, passe le Jourdain, jusqu’à ce que le Seigneur renverse ses ennemis,
ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
22 Et que toute la terre lui soit soumise: alors vous serez irréprochables devant le Seigneur et devant Israël, et vous obtiendrez les contrées que vous voulez, devant le Seigneur.
dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 Mais si ce que vous dites, vous ne le faites point, il n’y a de doute pour personne que vous ne péchiez contre le Seigneur; et sachez que votre péché s’emparera de vous.
“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
24 Bâtissez donc des villes pour vos petits enfants, des parcs et des étables pour vos brebis et vos bestiaux; et effectuez ce que vous avez promis.
Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 Alors les enfants de Gad et de Ruben dirent à Moïse: Nous •sommes tes serviteurs, nous ferons ce que commande notre maître.
Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
26 Nous laisserons nos petits enfants, nos femmes, nos troupeaux et nos bestiaux dans les villes de Galaad;
Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
27 Mais nous tous, tes serviteurs, nous marcherons à la guerre, tout prêts, comme toi, seigneur, tu le dis.
koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 Moïse ordonna donc à Eléazar, le prêtre, à Josué, fils de Nun, et aux princes des familles, dans les tribus d’Israël, et leur dit:
Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
29 Si les enfants de Gad et les enfants de Ruben passent avec vous le Jourdain, tous armés pour la guerre devant le Seigneur, et que la terre vous soit soumise, donnez-leur Galaad en possession.
Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
30 Mais s’ils ne veulent pas passer armés avec vous dans la terre de Chanaan, qu’ils prennent parmi vous des lieux d’habitation.
Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 Les enfants de Gad et les enfants de Ruben répondirent: Comme le Seigneur a dit à ses serviteurs, ainsi nous ferons.
Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
32 Nous-mêmes, nous marcherons armés devant le Seigneur dans la terre de Chanaan, et nous reconnaissons que nous avons déjà reçu notre possession au-delà du Jourdain.
Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 C’est pourquoi Moïse donna aux enfants de Gad et de Ruben, et à la demi-tribu de Manassé, fils de Joseph, le royaume de Séhon, roi de l’Amorrhéen, et le royaume d’Og, roi de Basan, et leur terre avec leurs villes d’alentour.
Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 Ainsi, les enfants de Gad reconstruisirent Gad, Dibon, Ataroth, Aroër,
Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
35 Etroth, Sophan, Jaser, Jegbaa,
Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
36 Bethnemra, Betharan, villes fortifiées, et des étables pour leurs troupeaux.
Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
37 Mais les enfants de Ruben rebâtirent Hésébon, Eléale, Cariathaïm,
Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
38 Nabo et Baalméon en changeantes noms, et aussi Sabama; donnant des noms aux villes qu’ils avaient construites.
Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 Or, les enfants de Machir, fils de Manassé, marchèrent sur Galaad et la dévastèrent, l’Amorrhéen qui l’habitait ayant été tué.
Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
40 Moïse donna donc la terre de Galaad à Machir, fils de Manassé, qui y habita.
Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
41 Mais Jaïr, fils de Manassé, s’en alla, et occupa ses bourgs, qu’il appela Havoth Jaïr, c’est-à-dire Bourgs de Jaïr,
Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
42 Nobé alla aussi, et prit Chanath avec ses bourgades, et il l’appela de son nom, Nobé.
Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.