< Nombres 21 >

1 Lorsque le roi d’Arad Chananéen, qui habitait vers le midi, eut appris cela, c’est-à-dire, qu’Israël était venu par le chemin des espions, il combattit contre lui, et étant vainqueur, il en emporta le butin.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
2 Mais Israël se liant par un vœu au Seigneur, dit: Si vous livrez ce peuple à ma main, je détruirai toutes ses villes.
Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
3 Et le Seigneur exauça les prières d’Israël, et il livra le Chananéen qu’Israël fit périr, ses villes ayant été renversées; et il appela ce lieu du nom de Horma, c’est-à-dire anathème.
Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
4 Or, ils partirent aussi du mont Hor par la voie qui conduit à la mer Rouge, pour aller autour de la terre d’Edom. Et le peuple commença à s’ennuyer du chemin et de la fatigue;
Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
5 Et il parla contre Dieu et contre Moïse, et dit: Pourquoi nous as-tu retirés de l’Egypte, pour que nous mourions dans le désert? Le pain nous manque, il n’y a pas d’eau; notre âme a déjà des nausées à cause de cette nourriture très légère.
ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
6 C’est pourquoi le Seigneur envoya contre le peuple des serpents brûlants: à cause des blessures et de la mort d’un grand nombre.
Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
7 On vint à Moïse et on dit: avons péché, parce que Nous nous avons parlé contre le Seigneur et contre toi: prie pour qu’il éloigne de nous les serpents. Et Moïse pria pour le peuple,
Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
8 Et le Seigneur lui dit: Fais un serpent d’airain, et expose-le comme un signe: celui qui ayant été blessé, le regardera, vivra.
Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
9 Moïse fit donc un serpent d’airain et l’exposa comme un signe: lorsque les blessés le regardaient, ils étaient guéris.
Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
10 Or les enfants d’Israël étant partis, campèrent à Oboth.
Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
11 D’où étant sortis, ils plantèrent leurs tentes à Jéabarim, dans le désert qui regarde Moab, contre le côté oriental.
Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
12 Et partant de là, ils vinrent au torrent de Zared;
Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
13 Le laissant, ils campèrent contre Arnon, qui est dans le désert, et s’avance sur les confins de l’Amorrhéen; puisqu’Arnon est la frontière de Moab, divisant les Moabites et les Amorrhéens.
Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
14 D’où il est dit dans le livre des guerres du Seigneur: Comme il a fait en la mer Rouge, ainsi il fera dans les torrents d’Arnon.
Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
15 Les rochers des torrents se sont inclinés, pour se reposer en Ar, et pour retomber dans les confins des Moabites.
ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
16 Au sortir de ce lieu parut un puits, au sujet duquel le Seigneur dit à Moïse: Assemble le peuple, et je lui donnerai de l’eau.
Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
17 Alors Israël chanta ce cantique: Que le puits monte. Ils chantaient tous ensemble:
Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
18 Le puits qu’ont creusé des princes, et qu’ont préparé les chefs de la multitude avec celui qui a donné la loi, et avec leurs bâtons. Du désert, ils vinrent à Matthana,
chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 De Matthana à Nahaliel, de Nahaliel à Bamoth;
Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
20 Après Bamoth est une vallée dans la contrée de Moab, près du sommet de Phasga, qui regarde contre le désert.
ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
21 Or Israël envoya des messagers à Séhon, roi des Amorréhens, disant:
Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
22 Je demande instamment qu’il me soit permis de passer par ta terre: nous ne nous détournerons point dans les champs et les vignes, nous ne boirons point l’eau des puits; c’est par la voie publique que nous marcherons, jusqu’à ce que nous soyons passés hors de tes frontières.
“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
23 Séhon ne voulut pas accorder qu’Israël passât par ses confins; bien plus, son armée assemblée, il sortit au devant dans le désert et vint à Jasa, et combattit contre lui.
Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
24 Israël le frappa du tranchant du glaive et posséda sa terre depuis Arnon jusqu’à Jeboc et aux enfants d’Ammon, parce que les frontières des Ammonites étaient gardées par une forte garnison.
Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
25 Israël prit donc toutes ses cités et il habita dans les villes de l’Amorrhéen, c’est-à-dire, dans Hésébon et ses bourgades.
Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
26 La ville d’Hésébon était à Séhon, roi des Amorréhens qui combattit contre le roi de Moab et prit toute la terre qui avait été de sa domination jusqu’à Arnon.
Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
27 C’est pourquoi on dit dans le proverbe: Venez à Hésébon; que la ville de Séhon soit bâtie et construite.
Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
28 Un feu est sorti d’Hésébon, une flamme, de la ville de Séhon, et elle a dévoré Ar des Moabites et les habitants des hauteurs d’Arnon.
“Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Malheur à toi, Moab! Tu as péri, peuple de Chamos. Il a mis ses fils en fuite et livré ses filles captives au roi des Amorrhéens, à Séhon.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 Leur joug a été entièrement détruit, depuis Hésébon jusqu’à Dibon; dans leur lassitude ils sont parvenus à Nophé et jusqu’à Médaba.
“Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
31 Israël habita donc dans la terre de l’Amorrhéen.
“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
32 Or, Moïse envoya des gens pour explorer Jazer; ils en prirent les bourgades et s’emparèrent des habitants.
Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
33 Ensuite, ils se détournèrent, et montèrent par le chemin de Basan; mais Og, roi de Basan, vint à leur rencontre pour les combattre à Edraï.
Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
34 Alors le Seigneur dit à Moïse: Ne le crains point, je l’ai livré à ta main, lui, tout son peuple et sa terre; et tu lui feras comme tu as fait à Séhon, roi des Amorrhéens, qui habitait Hésébon.
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
35 Ils le frappèrent donc, et lui avec ses enfants, et tout son peuple, jusqu’à une entière extermination, et ils possédèrent sa terre.
Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

< Nombres 21 >