< Nombres 20 >
1 Or, les enfants d’Israël et toute la multitude vinrent dans le désert de Sin, au premier mois; et le peuple demeura à Cadès. Et Marie mourut là, et elle fut ensevelie au même lieu.
Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
2 Et comme le peuple manquait d’eau, ils s’assemblèrent contre Moïse et Aaron,
Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
3 Et tournant à la sédition, ils dirent: Plût à Dieu que nous eussions péri au milieu de nos frères devant le Seigneur!
Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
4 Pourquoi avez-vous amené l’assemblée du Seigneur dans cette solitude, pour que nous et nos bêtes nous mourions?
Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
5 Pourquoi nous avez-vous fait monter de l’Egypte, et nous avez-vous amenés dans ce lieu détestable, qui ne peut être semé, qui ne produit ni figuier, ni vignes, ni grenadiers, où, de plus, il n’y a pas même d’eau pour boire?
Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
6 Alors Moïse et Aaron, la multitude congédiée, entrèrent dans le tabernacle, tombèrent inclinés vers la terre, crièrent au Seigneur, et dirent: Seigneur Dieu, écoutez le cri de ce peuple, et ouvrez-leur votre trésor, une fontaine d’eau vive, afin qu’étant rassasiés, leur murmure cesse. Alors apparut la gloire du Seigneur sur eux.
Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
7 Et le Seigneur parla à Moïse, disant:
Yehova anati kwa Mose,
8 Prends ta verge et assemble le peuple, toi et Aaron ton frère, et parlez à la pierre devant eux; et elle donnera de l’eau. Et lorsque tu auras fait sortir de l’eau de la pierre, toute la multitude boira et ses bêtes.
“Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
9 Moïse prit donc la verge qui était en la présence du Seigneur, comme il lui avait ordonné,
Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
10 La multitude étant assemblée devant la pierre, et il leur dit: Ecoutez, rebelles et incrédules: Pourrons-nous vous faire jaillir de l’eau de cette pierre?
Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
11 Et lorsque Moïse eut élevé la main, frappant de la verge deux fois la pierre, il en sortit de l’eau très abondante; en sorte que le peuple buvait et les bêtes.
Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
12 Et le Seigneur dit à Moïse et à Aaron: Parce que vous ne m’avez pas cru, et que vous ne m’avez pas sanctifié devant les enfants d’Israël, vous n’introduirez point ces peuples dans la terre que je leur donnerai.
Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
13 C’est là l’eau de contradiction, où les enfants d’Israël excitèrent une querelle contre le Seigneur, et il fut sanctifié au milieu d’eux.
Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
14 Cependant Moïse envoya de Cadès des messagers au roi d’Edom, pour lui dire: Voici ce que te mande ton frère Israël: Tu sais tout le labeur qui nous a saisis;
Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
15 Comment nos pères sont descendus en Egypte, comment nous y avons habité longtemps, comment les Egyptiens nous ont affligés, nous et nos pères,
Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
16 Et comment, nous ayant crié au Seigneur, il nous a exaucés, et a envoyé un ange qui nous a retirés de l’Egypte. Voici qu’arrêtés dans la ville de Cadès, qui est à tes derniers confins,
koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
17 Nous demandons instamment qu’il nous soit permis de passer par ta terre. Nous n’irons pas à travers les champs, ni à travers les vignes, nous ne boirons point l’eau de tes puits; mais nous marcherons par la voie publique, ne nous détournant ni à droite, ni à gauche, jusqu’à ce que nous soyons passés hors de tes frontières.
Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
18 Edom lui répondit: Tu ne passeras point par chez moi; autrement j’irai armé au-devant de toi.
Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
19 Et les enfants d’Israël dirent: C’est par la voie battue que nous marcherons; et si nous buvons ton eau, nous et nos troupeaux, nous donnerons ce qui est juste: il n’y aura pour le prix aucune difficulté; seulement que nous puissions passer rapidement.
Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
20 Mais Edom répondit: Tu ne passeras point. Et aussitôt il sortit au-devant d’eux avec une multitude infinie et une forte armée,
Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
21 Et il ne voulut pas écouler celui qui le priait d’accorder le passage par son territoire; c’est pourquoi Israël s’en détourna.
Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
22 Or, lorsqu’ils eurent décampé de Cadès ils vinrent à la montagne de Hor, qui est sur les confins de la terre d’Edom,
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
23 Où le Seigneur parla à Moïse:
Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
24 Qu’Aaron, dit-il, aille vers ses peuples; car il n’entrera pas dans la terre que j’ai donnée aux enfants d’Israël, parce qu’il a été incrédule à ma parole, aux Eaux de contradiction.
“Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
25 Prends Aaron et son fils avec lui, et tu les conduiras sur la montagne de Hor.
Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
26 Et, lorsque tu auras dépouillé le père de son vêtement, tu en revêtiras Eléazar son fils: Aaron sera réuni à ses pères, et il mourra là.
Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
27 Moïse fit comme avait ordonné le Seigneur: et ils montèrent sur la montagne de Hor devant toute la multitude.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
28 Et lorsqu’il eut dépouillé Aaron de ses vêtements il en revêtit Eléazar son fils. Aaron mort sur le sommet de la montagne, Moïse descendit avec Eléazar.
Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
29 Or toute la multitude voyant qu’Aaron était mort, pleura sur lui pendant trente jours dans toutes ses familles.
ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.