< Nombres 2 >
1 Le Seigneur parla encore à Moïse et à Aaron, disant:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Les enfants d’Israël, chacun selon ses bandes, ses étendards, ses drapeaux et les maisons de sa parenté, camperont autour du tabernacle d’alliance.
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 Juda plantera ses tentes vers l’orient selon les bandes de son armée, et le prince de ses enfants sera Nahasson, fils d’Aminadab;
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
4 Et le nombre total des combattants de sa race, est de soixante-quatorze mille six cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
5 Près de lui campèrent ceux de la tribu d’Issachar; leur prince fut Nathanael fils de Suar;
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
6 Et le nombre total de ses combattants, de cinquante-quatre mille quatre cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
7 Dans la tribu de Zabulon le prince fut Eliab, fils d’Hélon.
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
8 Toute l’armée des combattants de sa race fut de cinquante-sept mille quatre cents,
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
9 Tous ceux qui ont été dénombrés dans le camp de Juda, furent cent quatre-vingt-six mille quatre cents; et ils sortiront les premiers selon leurs bandes.
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
10 Dans le camp des enfants de Ruben vers le côté méridional, le prince sera Eli sur, fils de Sédéur;
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
11 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, quarante-six mille cinq cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
12 Près de lui campèrent ceux de la tribu de Siméon; leur prince fut Salamiel, fils de Surisaddaï,
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
13 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, cinquante-neuf mille trois cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
14 Dans la tribu de Gad, le prince fut Eliasaph, fils de Duel;
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
15 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, quarante-cinq mille six cent cinquante.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
16 Tous ceux qui ont été recensés dans le camp de Ruben furent cent cinquante-un mille quatre cent cinquante, selon leurs bandes; ils marcheront au second rang.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
17 Alors le tabernacle de témoignage sera enlevé par les soins des Lévites et par leurs bandes: de la manière qu’il sera dressé, il sera aussi enlevé. Chacun marchera en sa place et en son rang.
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
18 Vers le côté occidental sera le camp des enfants d’Ephraïm; leur prince fut Elisama, fils d’Ammiud;
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
19 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, quarante mille cinq cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
20 Et avec eux, la tribu des enfants de Manassé; leur prince fut Gamaliel, fils de Phadassur;
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
21 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, trente-deux mille deux cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
22 Dans la tribu des fils de Benjamin, le prince fut Abidan, fils de Gédéon;
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
23 Et toute l’armée de ses combattants qui ont été recensés, trente-cinq mille quatre cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
24 Tous ceux qui ont été dénombrés dans le camp d’Ephraïm, furent cent huit mille cent, selon leurs bandes; ils marcheront les troisièmes.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
25 Vers la partie de l’aquilon ont campé les fils de Dan; leur prince fut Ahiézer, fils d’Ammisaddaï;
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Toute l’armée de ses combattants qui ont été dénombrés, soixante-deux mille sept cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
27 C’est près de Dan que plantèrent leurs tentes ceux de la tribu d’Aser; leur prince fut Phégiel, fils d’Ochran;
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
28 Toute l’armée de ses combattants qui ont été comptés, quarante-un mille cinq cents,
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
29 Quant à la tribu des enfants de Nephthali, le prince fut Ahira, fils d’Enan;
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
30 Toute l’armée de ses combattants, cinquante-trois mille quatre cents.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
31 Tous ceux qui ont été dénombrés dans le camp de Dan, furent cent cinquante-sept mille six cents; et ils marcheront les derniers.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
32 Ce nombre des enfants d’Israël, selon les maisons de leur parenté et les bandes de leur armée divisée, était de six cent trois mille cinq cent cinquante.
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
33 Mais les Lévites n’ont pas été dénombrés parmi les enfants d’Israël; car ainsi l’avait ordonné le Seigneur à Moïse.
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
34 Et les enfants d’Israël firent selon tout ce qu’avait commandé le Seigneur. Ils campèrent selon leurs bandes, et marchèrent selon les familles et les maisons de leurs pères.
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.