< Nombres 16 >
1 Or voilà que Corée, fils d’Isaar, fils de Caath, fils de Lévi, et Dathan et Abiron, les fils d’Eliab, et de plus Hon, fils de Phéleth d’entre les fils de Ruben,
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2 S’élevèrent contre Moïse, ainsi que deux cent cinquante autres hommes des enfants d’Israël, princes de la synagogue, et qui, au temps du conseil, étaient nommément appelés.
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
3 Comme donc ils résistaient à Moïse et à Aaron, ils dirent: Qu’il vous suffise que toute la multitude soit une multitude de saints, et que le Seigneur soit au milieu d’eux. Pourquoi vous élevez-vous au-dessus du peuple du Seigneur?
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
4 Ce qu’ayant entendu Moïse, il tomba incliné sur sa face,
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
5 Et parlant à Coré et à toute la troupe: Demain matin, dit-il, le Seigneur fera connaître ceux qui lui appartiennent, et il attachera à lui les saints; et ceux qu’il aura choisis s’approcheront de lui.
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
6 Faites donc ceci: Que chacun prenne son encensoir, toi, Coré, et tout ton conseil.
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7 Et ayant pris demain du feu, mettez dessus de l’encens devant le Seigneur, et celui qu’il aura choisi, celui-là même sera saint. Vous vous élevez beaucoup, fils de Lévi.
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
8 Il dit encore à Coré: Ecoutez, fils de Lévi;
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9 Est-ce peu pour vous, que le Dieu d’Israël vous ait séparé de tout le peuple, et vous ait attaché à lui, afin que vous le serviez dans le culte du tabernacle, que vous assistiez devant la foule du peuple, et que vous exerciez le ministère pour le Seigneur?
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
10 Est-ce pour cela qu’il t’a fait approcher de lui, toi et tous tes frères, enfants de Lévi, afin que vous vous arrogiez même le sacerdoce,
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
11 Et que toute ta troupe résiste au Seigneur? Qu’est-ce, en effet, qu’Aaron, pour que vous murmuriez contre lui?
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
12 Moïse envoya donc appeler Dathan et Abiron, fils d’Eliab. Ils répondirent: Nous n’irons pas.
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
13 Est-ce peu pour vous, que vous nous ayez retirés d’une terre où coulaient du lait et du miel, pour nous faire mourir dans le désert, si de plus vous ne nous dominez point?
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
14 À la vérité, vous nous avez conduits dans une terre, où coulent des ruisseaux de lait et de miel, et vous nous avez donné des possessions de champs et de vignes; est-ce que vous voulez aussi nous arracher les yeux? Nous n’irons pas.
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
15 Or, Moïse fort irrité, dit au Seigneur: Ne regardez point leurs sacrifices; vous savez que je n’ai jamais reçu d’eux pas même un ânon, et que je n’ai affligé aucun deux.
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
16 Et il dit à Coré: Toi et toute ton assemblée, tenez-vous demain d’un côté devant le Seigneur, et Aaron d’un autre.
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
17 Prenez chacun vos encensoirs, et mettez-y de l’encens, offrant au Seigneur deux cent cinquante encensoirs; qu’Aaron tienne aussi son encensoir.
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
18 Lorsqu’ils eurent fait cela, Moïse et Aaron étant présents,
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 Et qu’ils eurent réuni contre eux toute la multitude à la porte du tabernacle, la gloire du Seigneur apparut à tous.
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
20 Et le Seigneur ayant parlé à Moïse et à Aaron, dit:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
21 Séparez-vous du milieu de cette assemblée, afin que je les détruise soudain.
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
22 Ceux-ci tombèrent inclinés sur leur face et dirent: Dieu très fort des esprits de toute chair, est-ce qu’un seul péchant, votre colère sévira contre tous.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
23 Et le Seigneur repartit à Moïse:
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
24 Ordonne à tout le peuple qu’il se sépare des tentes de Coré, de Dathan et d’Abiron.
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
25 Et Moïse se leva, alla vers Dathan et Abiron, et les anciens d’Israël le suivant,
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
26 Il dit à la multitude: Retirez-vous des tentes de ces hommes impies et ne touchez pas ce qui leur appartient, de peur que vous ne soyez enveloppés dans leurs péchés.
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
27 Or lorsqu’ils se furent retirés de leurs tentes tout autour, Dathan et Abiron, sortis se tenaient à l’entrée de leurs pavillons avec leurs femmes, leurs enfants, et tous les leurs.
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
28 Alors Moïse dit: En ceci vous connaîtrez que le Seigneur m’a envoyé pour faire tout ce que vous voyez, et que je n’ai rien produit de mon propre esprit:
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
29 S’ils meurent d’une mort ordinaire aux hommes, et s’ils sont visités de la plaie dont tous les autres ont coutume d’être visités, le Seigneur ne ma pas envoyé;
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
30 Mais si le Seigneur fait une chose nouvelle: si la terre ouvrant sa bouche les engloutit, eux et tout ce qui leur appartient, et qu’ils descendent vivants dans l’enfer, vous saurez qu’ils ont blasphémé le Seigneur. (Sheol )
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol )
31 Aussitôt qu’il cessa de parler, la terre se fendit sous leurs pieds;
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
32 Et ouvrant sa bouche, elle les dévora avec leurs tentes et tout leur avoir;
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
33 Et ils descendirent vivants dans l’enfer, recouverts par la terre, et ils périrent du milieu de la multitude. (Sheol )
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol )
34 Cependant tout Israël qui se tenait là autour, s’enfuit au cri de ceux qui périssaient, disant: C’est de peur que la terre ne nous engloutisse aussi.
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
35 En même temps un feu sorti du Seigneur tua les deux cent cinquante hommes qui offraient de l’encens.
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
36 Et le Seigneur parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
37 Ordonne à Éléazar, fils d’Aaron, le prêtre, qu’il prenne les encensoirs, qui sont par terre au milieu de l’embrasement, et qu’il disperse le feu çà et là, parce qu’ils ont été sanctifiés
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38 Par la mort des pécheurs; qu’il les réduise en lames, et qu’il les attache à l’autel, parce qu’on y a offert de l’encens au Seigneur, et qu’ils ont été sanctifiés, afin que les enfants d’Israël les voient comme un signe et un monument.
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
39 Eléazar, le prêtre, prit donc les encensoirs d’airain dans lesquels avaient offert de l’encens ceux que l’embrasement dévora, et il les réduisit en lames, les attachant à l’autel,
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
40 Afin que les enfants d’Israël eussent dans la suite de quoi les avertir, que quelqu’un d’étranger et qui n’était pas de la race d’Aaron, ne devait pas offrir de l’encens au Seigneur, de peur qu’il ne lui arrivât ce qui arriva à Coré et à toute sa troupe, lorsque le Seigneur parla à Moïse.
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
41 Or toute la multitude des enfants d’Israël murmura le jour suivant contre Moïse et Aaron, disant: C’est vous qui avez tué le peuple du Seigneur.
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
42 Et comme la sédition s’élevait et que le tumulte croissait,
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
43 Moïse et Aaron s’enfuirent au tabernacle d’alliance. Lorsqu’ils furent entrés, la nuée se couvrit, et la gloire du Seigneur apparut,
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44 Et le Seigneur dit à Moïse:
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
45 Retirez-vous du milieu de cette multitude, maintenant même je les détruirai. Et comme ils étaient couchés sur la terre,
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
46 Moïse dit à Aaron: Prends l’encensoir, et ayant pris, du feu de l’autel, mets de l’encens par dessus, et va aussitôt vers le peuple, afin que tu pries pour lui; car déjà la colère est sortie du Seigneur, et la plaie sévit avec violence,
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
47 Aaron l’ayant fait, et ayant couru au milieu de la multitude que déjà ravageait l’embrasement, offrit de l’encens.
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
48 Et se tenant entre les morts et les vivants, il pria pour le peuple, et la plaie cessa.
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
49 Or il y eut de ceux qui furent frappés, quatorze mille et sept cents hommes, outre ceux qui avaient péri dans la sédition de Coré.
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
50 Et Aaron retourna vers Moïse à la porte du tabernacle d’alliance, après que la mort se fut arrêté.
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.