< Néhémie 1 >
1 Paroles de Néhémias, fils de Helchias. Et il arriva au mois de Casleu, en l’année vingtième, que j’étais dans le château de Suse.
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 Et Hanani, un de mes frères, vint, lui et des hommes de Juda; et je les interrogeai sur ceux des Juifs, qui étaient restés de la captivité, et qui vivaient encore, et sur Jérusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 Et ils me répondirent: Ceux qui sont restés et qui ont été laissés de la captivité là dans la province, sont dans une grande affliction et dans l’opprobre; et le mur de Jérusalem est tombé, et ses portes ont été brûlées au feu.
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 Lorsque j’eus ouï de telles paroles, je m’assis, je pleurai, et je gémis durant plusieurs jours; je jeûnais, et je priais devant la face du Dieu du ciel.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 Et je dis: Je vous prie. Seigneur, Dieu du ciel, fort, grand et terrible, qui gardez l’alliance et la miséricorde avec ceux qui vous aiment et qui gardent vos commandements,
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 Que vos oreilles deviennent attentives et vos yeux, ouverts pour en cendre la prière de votre serviteur, que je fais aujourd’hui devant vous, nuit et jour, pour les enfants d’Israël, vos serviteurs; et je confesse les péchés des enfants d’Israël, par lesquels ils ont péché contre vous: moi et la maison de mon père, nous avons péché.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 Nous avons été séduits par la vanité, et nous n’avons pas gardé votre commandement, vos cérémonies, et les ordonnances que vous avez prescrites à Moïse, votre serviteur.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Souvenez-vous de la parole que vous avez confiée à Moïse, votre serviteur, disant: Lorsque vous aurez transgressé, moi je vous disperserai parmi les peuples:
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 Et si vous revenez à moi, et que vous gardiez mes préceptes, et que vous les accomplissiez, quand même vous auriez été emmenés jusqu’aux extrémités du ciel, je vous rassemblerai de là, et je vous ramènerai au lieu que j’ai choisi pour que mon nom y habite.
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 Et ceux-ci sont vos serviteurs et votre peuple, que vous avez rachetés par votre grande force et par votre main puissante.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 Je vous conjure, Seigneur, que votre oreille soit attentive à la prière de votre serviteur, et à la prière de vos serviteurs, qui veulent craindre votre nom; et dirigez votre serviteur aujourd’hui, et donnez-lui miséricorde devant cet homme: car moi j’étais l’échanson du roi.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.