< Matthieu 28 >

1 Or la nuit du sabbat, le premier jour de la semaine commençant à luire, Marie-Madeleine et l’autre Marie vinrent pour voir le sépulcre.
Litapita tsiku la Sabata, mmawa wa tsiku loyamba la Sabata, Mariya wa ku Magadala ndi Mariya wina anapita kukaona manda.
2 Et voilà qu’il se fit un grand tremblement de terre; car un ange du Seigneur descendit du ciel, et s’approchant, il renversa la pierre et s’assit dessus:
Kunachitika chivomerezi chachikulu, pakuti mngelo wa Ambuye anabwera kuchokera kumwamba ndipo anapita ku manda, nakagubuduza mwala nawukhalira.
3 Son visage était comme un éclair, et son vêtement comme la neige.
Maonekedwe ake anali ngati mphenzi ndipo zovala zake zinali mbuu ngati matalala.
4 Par la crainte qu’il leur inspira, les gardes furent épouvantés, et devinrent comme morts.
Alondawo anachita naye mantha kwambiri kotero kuti ananjenjemera ndi kuwuma ngati akufa.
5 Mais l’ange prenant la parole, dit aux femmes: Ne craignez point, vous; car je sais que vous cherchez Jésus, qui a été crucifié:
Mngelo anati kwa amayiwo, “Musachite mantha popeza ndikudziwa kuti mukufuna Yesu amene anapachikidwa.
6 Il n’est point ici; car il est ressuscité, comme il l’a dit; venez, et voyez le lieu où le Seigneur était déposé:
Iye muno mulibe, wauka monga mmene ananenera. Bwerani, dzaoneni malo amene anagona.
7 Et allant promptement, dites à ses disciples qu’il est ressuscité: et voici qu’il va devant vous en Galilée; c’est là que vous le verrez. Ainsi je vous l’ai dit d’avance.
Ndipo pitani msanga kawuzeni ophunzira ake kuti, ‘Wauka kwa akufa ndipo watsogola kupita ku Galileya. Mukamuona Iye kumeneko.’ Taonani ndakuwuzani.”
8 Elles sortirent aussitôt du sépulcre avec crainte et avec une grande joie, courant porter ces nouvelles à ses disciples.
Pamenepo amayiwo anachoka mofulumira ku mandako ali ndi mantha komabe atadzaza ndi chimwemwe, ndipo anathamanga kukawuza ophunzira ake.
9 Et voilà que Jésus se présenta à elles, disant: Je vous salue. Et elles, s’approchant, embrassèrent ses pieds et l’adorèrent.
Mwadzidzidzi Yesu anakumana nawo nati, “Moni.” Iwo anabwera kwa Iye, nagwira mapazi ake namulambira.
10 Alors Jésus leur dit: Ne craignez point; allez, annoncez à mes frères qu’ils aillent en Galilée; c’est là qu’ils me verront.
Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Musachite mantha, pitani kawuzeni abale anga kuti apite ku Galileya ndipo kumeneko akandiona Ine.”
11 Lorsqu’elles s’en furent allées, voilà que quelques-uns des gardes vinrent à la ville, et rapportèrent aux princes des prêtres tout ce qui s’était passé.
Amayi aja akupita, ena mwa alonda aja anapita ku mzinda nafotokozera akulu a ansembe zonse zimene zinachitika.
12 Et ceux-ci, s’étant assemblés avec les anciens, et ayant tenu conseil, donnèrent une grosse somme d’argent aux soldats,
Akulu a ansembe atakumana ndi akuluakulu anapangana zochita. Anapatsa alonda aja ndalama zambiri,
13 Disant: Dites: Ses disciples sont venus de nuit et l’ont enlevé, pendant que nous dormions.
nawawuza kuti, “Muzinena kuti, ‘Ophunzira ake anabwera usiku ndipo amuba ife tili mtulo.’
14 Et si le gouverneur l’apprend, nous le persuaderons, nous vous mettions en sûreté.
Ngati nkhani iyi imupeze bwanamkubwa, ife tidzamukhazika mtima pansi ndipo simudzakhala mʼmavuto.”
15 Ainsi les soldats, l’argent reçu, firent comme on leur avait appris; et ce bruit s’est répandu parmi les Juifs jusqu’à ce jour.
Pamenepo alondawo anatenga ndalamazo nachita monga mmene anawuzidwira. Ndipo mbiri iyi inawanda pakati pa Ayuda mpaka lero lino.
16 Cependant les onze disciples s’en allèrent en Galilée, sur la montagne que Jésus leur avait déterminée.
Ndipo ophunzira khumi ndi mmodzi aja anapita ku Galileya, ku phiri limene Yesu anawawuza kuti apite.
17 Et le voyant, ils l’adorèrent; quelques-uns néanmoins doutèrent.
Atamuona Iye, anamulambira; koma ena anakayika.
18 Alors s’approchant, Jésus leur parla, disant: Toute puissance m’a été donnée dans le ciel et sur la terre.
Kenaka Yesu anabwera kwa iwo nati, “Ulamuliro wonse kumwamba ndi dziko lapansi wapatsidwa kwa Ine.
19 Allez donc, enseignez toutes les nations, les baptisant au nom du Père, et du Fils, et du Saint-Esprit;
Chifukwa chake, pitani kaphunzitseni anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza mʼdzina la Atate ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera,
20 Leur apprenant à garder tout ce que je vous ai commandé: et voici que je suis avec vous tous les jours, jusqu’à la consommation du siècle. (aiōn g165)
ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.” (aiōn g165)

< Matthieu 28 >