< Matthieu 26 >
1 Or il arriva que lorsque Jésus eut achevé tous ces discours, il dit à ses disciples:
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
2 Vous savez que la pâque se fera dans deux jours, et que le Fils de l’homme sera livré pour être crucifié.
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
3 Alors les princes des prêtres et les anciens du peuple s’assemblèrent dans la salle du grand prêtre appelé Caïphe,
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
4 Et tinrent conseil pour se saisir de Jésus par ruse, et le faire mourir.
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
5 Mais ils disaient: Non pas un jour de la fête, de peur qu’il ne s’élevât du tumulte parmi le peuple.
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
6 Or, comme Jésus était à Béthanie, dans la maison de Simon le lépreux,
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
7 Vint auprès de lui une femme ayant un vase d’albâtre plein d’un parfum de grand prix, et elle le répandit sur sa tête, lorsqu’il était à table.
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
8 Ce que voyant, ses disciples s’indignèrent, disant: Pourquoi cette perte?
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
9 Il pouvait, en effet, ce parfum, se vendre très cher et être donné aux pauvres.
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
10 Mais Jésus le sachant, leur dit: Pourquoi faites-vous de la peine à cette femme? c’est une bonne œuvre qu’elle a faite envers moi.
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
11 Car vous avez toujours les pauvres avec vous; mais moi, vous ne m’avez pas toujours.
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
12 Cette femme, en répandant ce parfum sur mon corps, l’a fait pour m’ensevelir.
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
13 En vérité, je vous le dis, partout où sera prêché cet évangile, dans le monde entier, on dira même, en mémoire d’elle, ce qu’elle vient de faire.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
14 Alors un des douze, appelé Judas Iscariote, alla vers les princes des prêtres,
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
15 Et leur dit: Que voulez-vous me donner, et je vous le livrerai? Et ceux-ci lui assurèrent trente pièces d’argent.
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
16 Et de ce moment il cherchait une occasion favorable pour le leur livrer.
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
17 Or, le premier jour des azymes, les disciples s’approchèrent de Jésus, disant: Où voulez-vous que nous vous préparions ce qu’il faut pour manger la pâque?
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
18 Jésus répondit: Allez dans la ville, chez un tel, et dites-lui: Le maître dit: Mon temps est proche, je veux faire chez toi la pâque avec mes disciples.
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
19 Et les disciples firent comme Jésus leur commanda, et ils préparèrent la pâque.
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
20 Le soir donc étant venu, il était à table avec ses douze disciples.
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
21 Et pendant qu’ils mangeaient, il dit: En vérité, je vous dis qu’un de vous doit me trahir.
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
22 Alors, grandement contristés, ils commencèrent à lui demander chacun en particulier: Est-ce moi, Seigneur?
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
23 Mais Jésus répondant, dit: Celui qui met avec moi la main dans le plat, celui-là me trahira.
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
24 Pour ce qui est du Fils de l’homme, il s’en va, selon ce qui a été écrit de lui; mais malheur à l’homme par qui le Fils de l’homme sera trahi; il vaudrait mieux pour cet homme qu’il ne fût pas né.
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
25 Mais prenant la parole. Judas qui le trahit, dit: Est-ce moi, maître? Il lui répondit: Tu l’as dit.
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
26 Or, pendant qu’ils soupeaient, Jésus prit le pain, le bénit, le rompit, et le donna à ses disciples, et dit: Prenez et mangez; ceci est mon corps.
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
27 Et, prenant le calice, il rendit grâces, et le leur donna, disant: Buvez-en tous.
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
28 Car ceci est mon sang, le sang du nouveau testament, qui sera répandu pour un grand nombre en rémission des péchés.
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
29 Or, je vous le dis, je ne boirai plus désormais de ce fruit de la vigne, jusqu’au jour où je le boirai nouveau avec vous dans le royaume de mon Père.
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
30 Et l’hymne dit, ils s’en allèrent à la montagne des Oliviers.
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
31 Alors Jésus leur dit: Vous tous vous prendrez du scandale à mon sujet pendant cette nuit; car il est écrit: Je frapperai le pasteur, et les brebis du troupeau seront dispersées.
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
32 Mais, après que je serai ressuscité, je vous précéderai en Galilée.
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
33 Or, Pierre répondant, lui dit: Quand tous se scandaliseraient de vous, pour moi jamais je ne me scandaliserai.
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
34 Jésus lui répondit: En vérité, je te dis que cette nuit même, avant qu’un coq chante, tu me renieras trois fois.
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
35 Pierre lui dit: Quand il me faudrait mourir avec vous, je ne vous renierai point. Et tous les disciples dirent aussi de même.
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
36 Alors Jésus vint avec eux à une maison de campagne qui est appelée Gethsémani, et il dit à ses disciples: Asseyez-vous ici, pendant que j’irai là et que je prierai.
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
37 Et ayant pris avec lui Pierre et les deux fils de Zébédée, il commença à s’attrister et à être affligé.
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
38 Alors il leur dit: Mon âme est triste jusqu’à la mort; demeurez ici, et veillez avec moi.
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
39 Et, s’étant un peu avancé, il tomba sur sa face, priant et disant: Mon Père, s’il est possible, que ce calice passe loin de moi; toutefois, non ma volonté, mais la vôtre.
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
40 Ensuite il vint à ses disciples, et il les trouva endormis, et Il dit à Pierre: Ainsi, vous n’avez pu veiller une heure avec moi.
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
41 Veillez et priez, afin que vous n’entriez point en tentation; à la vérité, l’esprit est prompt, mais la chair est faible.
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
42 Il s’en alla encore une seconde fois, et pria, disant: Mon Père, si ce calice ne peut passer sans que je le boive, que votre volonté se fasse.
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
43 Il vint de nouveau, et les trouva dormant, car leurs yeux étaient appesantis.
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
44 Et les ayant laissés, il s’en alla encore, et pria une troisième fois, disant les mêmes paroles.
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
45 Alors il revint à ses disciples, et leur dit: Dormez maintenant, et reposez-vous: voici que l’heure approche, et le Fils de l’homme sera livré aux mains des pécheurs.
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
46 Levez-vous, allons; voici qu’approche celui qui me livrera.
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
47 Jésus parlant encore, voici que Judas, l’un des douze, vint, et, avec lui, une troupe nombreuse armée d’épées et de bâtons, envoyée par les princes des prêtres et par les anciens du peuple.
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
48 Or celui qui le livra, leur donna un signe, disant: Celui que je baiserai, c’est lui-même, saisissez-le.
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
49 Et aussitôt, s’approchant de Jésus, il dit: Je vous salue, maître. Et il le baisa.
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
50 Et Jésus lui répondit: Mon ami, dans quel dessein es-tu venu? Alors ils s’avancèrent, mirent la main sur Jésus et se saisirent de lui.
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
51 Et voilà qu’un de ceux qui étaient avec Jésus, étendant la main, tira son épée, et, frappant le serviteur du prince des prêtres, lui coupa l’oreille.
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 Alors Jésus lui dit: Remets ton épée en son lieu; car tous ceux qui se serviront de l’épée périront par l’épée.
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
53 Penses-tu que je ne puisse pas prier mon Père, et qu’il ne m’enverra pas à l’heure même plus de douze légions d’anges?
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
54 Comment donc s’accompliront les Ecritures, disant qu’il doit en être ainsi?
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
55 En cette heure-là, Jésus dit à la troupe: Vous êtes sortis comme contre un voleur avec des épées et des bâtons afin de me prendre; j’étais tous les jours assis parmi vous, enseignant dans le temple, et vous ne m’avez point pris.
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
56 Or tout cela s’est fait, pour que s’accomplissent les Ecritures des prophètes. Alors tous les disciples l’abandonnant, s’enfuirent.
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
57 Mais les autres, se saisissant de Jésus, l’emmenèrent chez Caïphe, prince des prêtres, où s’étaient assemblés les scribes et les anciens du peuple.
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
58 Or Pierre le suivit de loin, jusque dans la cour du prince des prêtres; et y étant entré, il s’assit avec les serviteurs, pour voir la fin.
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
59 Cependant les princes des prêtres et tout le conseil cherchaient un faux témoignage contre Jésus, pour le livrer à la mort.
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
60 Et ils n’en trouvèrent point, quoique beaucoup de faux témoins se fussent présentés. En dernier lieu, vinrent deux faux témoins,
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
61 Et ils dirent: Celui-ci a dit: Je puis détruire le temple de Dieu, et, après trois jours, le rebâtir.
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
62 Alors le prince des prêtres se levant, lui dit: Tu ne réponds rien à ce que ceux-ci témoignent contre toi?
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
63 Mais Jésus se taisait. Et le prince des prêtres lui dit: Je t’adjure par le Dieu vivant de nous dire si tu es le Christ, le Fils de Dieu.
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
64 Jésus lui répondit: Tu l’as dit. De plus, je vous le déclare, vous verrez un jour le Fils de l’homme assis à la droite de la majesté de Dieu, et venant dans les nuées du ciel.
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
65 Aussitôt le prince des prêtres déchira ses vêtements, disant: Il a blasphémé; qu’avons-nous encore besoin de témoins? voilà que maintenant vous avez entendu le blasphème.
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
66 Que vous en semble? Et eux répondant, dirent: Il mérite la mort.
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
67 Alors ils lui crachèrent au visage, et le déchirèrent à coups de poing; et d’autres lui donnèrent des soufflets,
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
68 Disant: Christ, prophétise-nous, qui est celui qui t’a frappé?
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
69 Cependant Pierre était assis dehors dans la cour; et une servante s’approcha de lui, disant: Et toi aussi tu étais avec Jésus le Galiléen?
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
70 Mais il nia devant tous, disant: Je ne sais ce que tu veux dire.
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
71 Et comme il sortait hors de la porte, une autre servante l’aperçut et dit à ceux qui se trouvaient là: Celui-ci était aussi avec Jésus de Nazareth.
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
72 Et il le nia de nouveau avec serment, disant: Je ne connais point cet homme.
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
73 Peu après, ceux qui se trouvaient là s’approchèrent et dirent à Pierre: Certainement, toi aussi tu es de ces gens-là; ton langage te décèle.
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
74 Alors il se mit à faire des imprécations et à jurer qu’il ne connaissait point cet homme. Et aussitôt un coq chanta.
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
75 Et Pierre se souvint de cette parole que Jésus lui avait dite: Avant qu’un coq chante, tu me renieras trois fois. Et étant sorti, il pleura amèrement.
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.