< Marc 3 >

1 Jésus entra une autre fois dans la synagogue; or il s’y trouvait un homme qui avait une main desséchée.
Nthawi inanso analowa mʼsunagoge, ndipo munthu wa dzanja lolumala anali momwemo.
2 Et on l’observait pour voir s’il le guérirait un jour de sabbat, afin de l’accuser.
Ena a iwo anafunafuna chifukwa chakuti akamuneneze Yesu, potero anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angamuchiritse tsiku la Sabata.
3 Et il dit à l’homme qui avait la main desséchée: Lève-toi, là, au milieu.
Yesu anati kwa munthu wolumala dzanjayo, “Imirira, bwera kuno kutsogolo.”
4 Puis il demanda aux autres: Est-il permis, un jour de sabbat, de faire du bien ou du mal, de sauver une âme ou de la perdre? Mais eux gardaient le silence.
Ndipo Yesu anawafunsa kuti, “Kodi chololedwa ndi chiyani pa tsiku la Sabata: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kupha?” Koma iwo anakhala chete.
5 Alors les regardant avec colère, et contristé de l’aveuglement de leur cœur, il dit à cet homme: Etends ta main. Il l’étendit, et sa main devint saine.
Yesu anawayangʼana ndi mkwiyo ndipo powawidwa mtima chifukwa cha mitima yawo yowuma anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola, ndipo dzanja lake linachira.
6 Or les pharisiens étant sortis, tinrent aussitôt conseil contre lui avec les hérodiens, comment ils le perdraient.
Kenaka Afarisi anatuluka nayamba kukonza chiwembu ndi Aherode mmene angamuphere Yesu.
7 Mais Jésus se retira avec ses disciples vers la mer, et une troupe nombreuse le suivit de la Galilée et de la Judée,
Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata.
8 De Jérusalem, de l’Idumée, et d’au-delà du Jourdain; et une grande multitude des environs de Tyr et de Sidon, apprenant ce qu’il faisait, vint à lui.
Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni.
9 Il dit alors à ses disciples de lui amener une barque, à cause de la foule, de peur qu’il n’en fût accablé
Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize.
10 Car il en guérissait beaucoup, de sorte que tous ceux qui avaient quelque mal se jetaient sur lui pour le toucher.
Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze.
11 Les esprits impurs eux-mêmes, lorsqu’ils le voyaient, se prosternaient devant lui et criaient, disant;
Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!”
12 Vous êtes le Fils de Dieu. Mais il leur défendait avec de grandes menaces de le révéler.
Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.
13 Etant monté sur la montagne, il appela à lui ceux que lui-même voulut; et ils vinrent à lui.
Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye.
14 Il en établit douze pour être avec lui et pour les envoyer prêcher,
Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira
15 Et il leur donna le pouvoir de guérir les maladies et de chasser les démons:
ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda.
16 D’abord Simon à qui il donna le nom de Pierre;
Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro);
17 Puis Jacques, fils de Zébédée, et Jean son frère, auxquels il donna le nom de Boanergès, c’est-à-dire fils du tonnerre;
Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu);
18 André, Philippe, Barthélemi, Matthieu, Thomas, Jacques fils d’Alphée, Thaddée, Simon le Cananéen,
Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote,
19 Et Judas Iscariote, celui-là même qui le trahit.
ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
20 Ils vinrent dans une maison, et la foule s’y assembla de nouveau, en sorte qu’ils ne pouvaient pas même manger du pain.
Pambuyo pake Yesu analowa mʼnyumba, ndipo gulu la anthu linasonkhananso, kotero kuti Iye pamodzi ndi ophunzira ake sanapeze mpata kuti adye.
21 Ce qu’ayant appris, les siens vinrent pour se saisir de lui, car ils disaient: Il a perdu l’esprit.
Anthu a ku banja lake atamva zimenezi, anapita kuti akamutenga, pakuti ankanena kuti, “Wazungulira mutu.”
22 Et les scribes, qui étaient venus de Jérusalem, disaient: Il est possédé de Béelzébub, et c’est par le prince des démons qu’il chasse les démons.
Ndipo aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anati, “Iye wagwidwa ndi Belezebabu! Ndi ulamuliro wa mkulu wa ziwanda akutulutsa ziwanda.”
23 Mais Jésus les ayant appelés, leur disait en paraboles: Comment Satan peut-il chasser Satan?
Pamenepo Yesu anawayitana nawayankhula mʼmafanizo nati: “Kodi Satana angatulutse bwanji Satana?
24 Si un royaume est divisé contre lui-même, ce royaume ne peut subsister.
Ngati ufumu ugawanikana mwa iwo okha, ufumu umenewo sungakhalitse.
25 Et si une maison est divisée contre elle-même, cette maison ne peut subsister.
Ngati nyumba igawanikana mwa iyo yokha, nyumba imeneyo singathe kuyima.
26 Si donc Satan s’est élevé contre lui-même, il est divisé, et il ne pourra subsister; mais il touche à sa fin.
Ndipo ngati Satana adzitsutsa yekha sangathe kuyima; ulamuliro wake watha.
27 Nul ne peut entrer dans la maison du fort et ravir ce qu’il possède, s’il ne l’a lié auparavant; c’est alors qu’il pillera sa maison.
Kunena zoona, palibe munthu angalowe mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kutenga katundu wake pokhapokha atayamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Pamenepo akhoza kumubera.
28 En vérité je vous le dis, tous les péchés seront remis aux enfants des hommes, même les blasphèmes par lesquels ils auront blasphémé.
Ndikukuwuzani zoona kuti machimo onse ndi zamwano zonse za anthu zidzakhululukidwa,
29 Mais celui qui aura blasphémé contre l’Esprit-Saint n’en aura jamais la rémission; mais il sera coupable d’un péché éternel. (aiōn g165, aiōnios g166)
koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
30 Parce qu’ils disaient: II est possédé d’un esprit impur.
Ananena izi chifukwa anati, “Ali ndi mzimu woyipa.”
31 Cependant sa mère et ses frères vinrent; et, se tenant dehors, ils l’envoyèrent appeler.
Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye.
32 Or la foule était assise autour de lui, et on lui dit: Voilà dehors votre mère et vos frères qui vous cherchent.
Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, “Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani.”
33 Et leur répondant, il dit: Qui est ma mère, et qui sont mes frères?
Iye anafunsa kuti, “Amayi ndi abale anga ndi ndani?”
34 Et, regardant ceux qui étaient assis autour de lui: Voici, dit-il, ma mère et mes frères,
Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, “Awa ndi amayi anga ndi abale anga!
35 Car quiconque fait la volonté de Dieu, celui-là est mon frère, et ma sœur, et ma mère.
Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga.”

< Marc 3 >