< Luc 23 >
1 Et toute l’assemblée se levant, ils le menèrent à Pilate.
Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
2 Et ils commencèrent à l’accuser, disant: Nous avons trouvé celui-ci pervertissant notre nation, défendant de payer le tribut à César, et disant qu’il est Christ roi.
Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
3 Or Pilate l’interrogea, disant: Es-tu le roi des Juifs? Jésus répondant, dit: Tu le dis.
Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
4 Alors Pilate dit aux princes des prêtres et à la multitude: Je ne trouve aucune cause de mort en cet homme.
Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
5 Mais eux insistaient, disant: Il soulève le peuple, enseignant par toute la Judée, commençant par la Galilée jusqu’ici.
Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
6 Pilate entendant nommer la Galilée, demanda si cet homme était Galiléen.
Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
7 Et dès qu’il sut qu’il était de la juridiction d’Hérode, il le renvoya à Hérode, qui était lui-même à Jérusalem en ces jours-là.
Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
8 Hérode, voyant Jésus, s’en réjouit beaucoup; car il désirait depuis longtemps de le voir, parce qu’il avait entendu dire beaucoup de choses de lui, et qu’il espérait lui voir faire quelque miracle.
Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
9 Il lui faisait donc beaucoup de questions; mais Jésus ne lui répondait rien.
Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
10 Cependant se trouvaient là les princes des prêtres et les scribes, l’accusant sans relâche.
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
11 Mais Hérode avec sa cour le méprisa; il se joua de lui après l’avoir revêtu d’une robe blanche, et il le renvoya à Pilate.
Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
12 Et Hérode et Pilate devinrent amis ce jour-là même; auparavant ils étaient ennemis l’un de l’autre.
Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
13 Or Pilate ayant convoqué les princes des prêtres, les magistrats et le peuple,
Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
14 Leur dit: Vous m’avez présenté cet homme comme soulevant le peuple; et voilà que, l’interrogeant devant vous, je n’ai rien trouvé en lui de ce dont vous l’accusez,
ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
15 Ni Hérode non plus; car je vous ai envoyés à lui, et on ne l’a convaincu de rien qui mérite la mort.
Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
16 Je le renverrai donc après l’avoir fait châtier.
Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
17 Car il était obligé de leur remettre un prisonnier pendant la fête.
(Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
18 Mais la foule tout entière cria: Otez celui-ci du monde, et délivrez-nous Barabbas.
Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
19 (Lequel, à cause d’une sédition qui s’était faite dans la ville, et d’un meurtre, avait été mis en prison.)
(Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
20 Pilate leur parla de nouveau, désirant renvoyer Jésus.
Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
21 Mais eux redoublaient leurs clameurs, disant: Crucifiez-le, crucifiez-le!
Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
22 Et Pilate, pour la troisième fois, leur dit: Mais quel mal a fait celui-ci? Je ne trouve aucune cause de mort en lui; je le châtierai donc et le renverrai.
Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
23 Mais ils insistaient avec de grands cris, demandant qu’on le crucifiât; et leurs cris devenaient de plus en plus forts.
Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
24 Et Pilate ordonna que ce qu’ils demandaient fût exécuté.
Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
25 Ainsi il leur délivra celui qui avait été mis en prison pour cause de sédition et de meurtre, et qu’ils demandaient, et il abandonna Jésus à leur volonté.
Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
26 Or comme ils l’emmenaient, ils prirent un certain Simon de Cyrène, qui revenait des champs, et le chargèrent de porter la croix derrière Jésus.
Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
27 Or une grande foule de peuple et de femmes le suivaient, se frappant la poitrine et se lamentant sur lui.
Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
28 Mais Jésus, se tournant vers elles, dit: Filles de Jérusalem, ne pleurez pas sur moi, mais pleurez sur vous-mêmes et sur vos enfants;
Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
29 Car voici que viendront des jours où l’on dira: Heureuses les stériles, et les entrailles qui n’ont pas engendré, et les mamelles qui n’ont point allaité!
Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
30 Alors ils commenceront à dire aux montagnes: Tombez sur nous: et aux collines: Couvrez-nous.
Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
31 Car si l’on fait ainsi au bois vert, que sera-t-il fait au bois sec?
Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
32 On conduisait aussi avec lui deux autres hommes qui étaient des malfaiteurs, pour les mettre à mort.
Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
33 Et lorsqu’ils furent arrivés au lieu qui est appelé Calvaire, ils le crucifièrent, et les voleurs aussi, l’un à sa droite, et l’autre à sa gauche.
Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
34 Mais Jésus disait: Mon Père, pardonnez-leur, car ils ne savent ce qu’ils font. Partageant ensuite ses vêtements, ils y jetèrent le sort.
Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
35 Et le peuple était là, regardant, et les chefs le raillaient avec le peuple, disant: Il a sauvé les autres; qu’il se sauve, s’il est le Christ, l’élu de Dieu.
Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
36 Les soldats mêmes, s’approchant, l’insultaient, lui présentant du vinaigre,
Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
37 Et disant: Si tu es le roi des Juifs, sauve-toi.
ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
38 Il y avait aussi au-dessus de lui une inscription où était écrit en caractères grecs, latins et hébreux: CELUI-CI EST LE ROI DES JUIFS.
Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
39 Or l’un des voleurs qui étaient suspendus en croix le blasphémait, disant: Si tu es le Christ, sauve-toi toi-même, et nous aussi.
Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
40 Mais l’autre, répondant, le reprenait, disant: Ne crains-tu point Dieu, quand tu subis la même condamnation?
Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
41 Encore pour nous, c’est avec justice; car nous recevons ce que nos actions méritent; mais celui-ci n’a rien fait de mal.
Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
42 Et il disait à Jésus: Seigneur, souvenez-vous de moi quand vous serez arrivé dans votre royaume.
Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
43 Et Jésus lui dit: En vérité, je te le dis, aujourd’hui tu seras avec moi dans le paradis.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
44 Il était environ la sixième heure, et les ténèbres couvrirent toute la terre jusqu’à la neuvième heure.
Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
45 Et le soleil s’obscurcit, et le voile du temple se déchira par le milieu.
pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
46 Alors, criant d’une voix forte, Jésus dit: Mon Père, je remets mon esprit entre vos mains. Et disant cela, il expira.
Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
47 Or le centurion voyant ce qui était arrivé, glorifia Dieu, disant: Vraiment cet homme était juste.
Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
48 Et toute la multitude de ceux qui assistaient à ce spectacle, et qui voyaient ce qui se passait, s’en retournaient, frappant leur poitrine.
Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
49 Tous ceux de la connaissance de Jésus, et les femmes qui l’avaient suivi de Galilée, se tenaient à l’écart, considérant toutes ces choses.
Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
50 Mais voilà qu’un décurion nommé Joseph, homme bon et juste,
Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
51 Qui n’avait consenti ni au dessein, ni aux actes des autres, et qui était d’Arimathie, ville de Galilée, et attendait lui-même le royaume de Dieu,
Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
52 Vint vers Pilate, et lui demanda le corps de Jésus
Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
53 Et l’ayant détaché de la croix, il l’enveloppa d’un linceul, et le mit dans un sépulcre taillé dans le roc, où personne n’avait encore été mis.
Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
54 Or c’était le jour de la préparation, et le sabbat allait commencer.
Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
55 Les femmes qui étaient venues de la Galilée avec Jésus ayant suivi Joseph, virent le sépulcre, et comment le corps de Jésus y avait été mis.
Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
56 Et s’en retournant, elles préparèrent des aromates et des parfums; et pendant le sabbat, elles demeurèrent en repos, selon la loi.
Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.