< Lévitique 22 >

1 Le Seigneur parla aussi à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Parle à Aaron et à ses fils, afin qu’ils s’abstiennent de ce qui a été consacré par les enfants d’Israël, et qu’ils ne souillent pas le nom des choses qui me sont consacrées, qu’ils offrent eux-mêmes. Je suis le Seigneur.
“Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
3 Dis à eux et à leurs descendants: Tout homme de votre race qui s’approchera des choses qui auront été consacrées et que les enfants d’Israël auront offertes au Seigneur, mais dans lequel est une impureté, périra devant le Seigneur. C’est moi qui suis le Seigneur.
“Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
4 Un homme de la race d’Aaron qui sera lépreux ou qui aura la gonorrhée ne mangera point des choses qui m’auront été consacrées, jusqu’à ce qu’il soit guéri. Celui qui touchera un homme impur à cause d’un mort, et à qui arrivera comme il arrive dans l’usage du mariage,
“Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
5 Et qui touchera un reptile et quoi que ce soit d’impur dont le contact souille,
kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
6 Sera impur jusqu’au soir, et ne mangera point des choses qui auront été sanctifiées; mais lorsqu’il aura lavé sa chair dans l’eau,
Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
7 Et que le soleil sera couché, alors purifié, il mangera des choses sanctifiées, parce que c’est sa nourriture.
Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
8 Ils ne mangeront point d’un animal crevé, et d’un animal pris par une bête sauvage, et ils ne seront point souillés par eux. C’est moi qui suis le Seigneur.
Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
9 Qu’ils gardent mes préceptes, afin qu’ils ne soient point soumis au péché, et qu’ils ne lorsqu’ils l’auront souillé. Je suis le Seigneur qui les sanctifie.
“‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
10 Nul étranger ne mangera des choses sanctifiées, celui qui séjourne chez un prêtre et un mercenaire n’en mangeront point.
“‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
11 Mais celui que le prêtre aura acheté, et le serviteur qui sera né dans sa maison, ceux-là en mangeront.
Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
12 Si la fille d’un prêtre épouse un homme du peuple, quel qu’il soit, elle ne mangera point des choses qui auront été sanctifiées, ni des prémices.
Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
13 Mais si, veuve ou répudiée et sans enfants, elle retourne à la maison de son père, elle sera nourrie de la nourriture de son père, comme elle avait accoutumé étant jeune fille. Aucun étranger n’a le droit d’en manger.
Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
14 Celui qui aura mangé des choses sanctifiées par ignorance, ajoutera la cinquième partie à ce qu’il a mangé, et il la donnera au prêtre pour le sanctuaire.
“‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
15 Ils ne profaneront point les choses sanctifiées des enfants d’Israël, que ceux-ci offrent au Seigneur:
Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
16 De peur qu’ils ne portent l’iniquité de leur délit, lorsqu’ils auront mangé les choses sanctifiées. Je suis le Seigneur qui les sanctifie.
ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
17 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Parle à Aaron, à ses fils et à tous les enfants d’Israël, et tu leur diras: Un homme de la maison d’Israël, et d’entre les étrangers qui habitent chez vous qui présente son oblation, ou acquittant des vœux, ou faisant une offrande spontanée, quoi que ce soit qu’il présente pour l’holocauste du Seigneur,
“Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
19 Afin que ce soit présenté par vous, ce sera un mâle sans tache d’entre les bœufs, les brebis et les chèvres.
ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
20 S’il a une tache, vous ne l’offrirez point, et il ne sera point acceptable.
Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
21 Un homme qui offre une victime de sacrifices pacifiques au Seigneur, ou acquittant des vœux, ou faisant une offrande spontanée, tant de bœufs que de brebis, offrira un animal sans tache, afin qu’il soit acceptable: il n’y aura aucune tache en lui.
Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
22 S’il est aveugle, s’il a un membre rompu, ou une cicatrice, ou des pustules, ou la gale, ou le farcin: vous n’offrirez pas ces animaux au Seigneur, et vous n’en brûlerez point sur l’autel du Seigneur.
Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
23 Tu pourras offrir volontairement un bœuf et une brebis, une oreille et la queue ayant été coupées; mais un vœu ne peut être acquitté par leur moyen.
Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
24 Vous n’offrirez au Seigneur aucun animal qui a l’organe générateur ou froissé, ou foulé, ou coupé, ou arraché; et en votre pays ne faites absolument point cela.
Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
25 De la main de l’étranger vous n’offrirez point des pains à votre Dieu, ni toute autre chose qu’il voudra donner, parce que toutes ces choses sont corrompues et souillées: vous ne les recevrez point.
Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
26 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
27 Un bœuf, une brebis et une chèvre, lorsqu’ils seront nés, seront sept jours sous la mamelle de leur mère; mais au huitième jour et après, ils pourront être offerts au Seigneur.
“Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
28 Soit cette vache, soit cette brebis, elles ne seront pas immolées en un seul jour avec leurs petits.
Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
29 Si vous immolez une hostie pour action de grâces au Seigneur, afin qu’il puisse se laisser fléchir,
“Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
30 Vous la mangerez le même jour, il n’en demeurera rien pour le matin du jour suivant. Je suis le Seigneur.
Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
31 Gardez mes commandements et exécutez-les. Je suis le Seigneur.
“Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
32 Ne souillez point mon nom saint, afin que je sois sanctifié au milieu des enfants d’Israël. Je suis le Seigneur qui vous sanctifie,
Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
33 Et qui vous ai retirés de la terre d’Egypte afin que je fusse votre Dieu. Je suis le Seigneur.
ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”

< Lévitique 22 >