< Lévitique 20 >

1 Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tu diras ces choses aux enfants d’Israël: Si quelque homme d’entre les enfants d’Israël, et d’entre les étrangers qui habitent en Israël, donne de ses enfants à l idole de Moloch, qu’il meure de mort: le peuple du pays le lapidera,
“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
3 Et moi, je poserai ma face contre lui, et je le retrancherai du milieu de son peuple, parce qu’il a donné de ses enfants à Moloch, qu’il a souillé mon sanctuaire, et qu’il a profané mon saint nom.
Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
4 Que si le peuple du pays négligeant et estimant peu mon commandement, laisse aller l’homme qui a donné de ses enfants à Moloch, et ne veut point le tuer,
Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
5 Je poserai ma face sur cet homme et sur sa parenté, et je le retrancherai lui et tous ceux qui auront consenti à ce qu’il forniquât avec Moloch, du milieu de son peuple.
Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
6 Un homme qui ira vers les magiciens et les devins et forniquera avec eux, je poserai ma face contre lui, et je l’exterminerai du milieu de son peuple.
“‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
7 Sanctifiez-vous et soyez saints, parce que c’est moi qui suis le Seigneur votre Dieu.
“‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Gardez mes préceptes et exécutez-les. Je suis le Seigneur qui vous sanctifie.
Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
9 Que celui qui maudit son père ou sa mère, meure de mort: c’est son père et sa mère qu’il a maudits, que son sang soit sur lui.
“‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
10 Si quelqu’un abuse de la femme d’un autre, et commet un adultère avec la femme de son prochain, qu’ils meurent de mort, et l’homme adultère et la femme adultère.
“‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
11 Que celui qui dort avec sa belle-mère, et découvre l’ignominie de son père, meure avec elle: que leur sang soit sur eux.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
12 Si quelqu’un dort avec sa belle-fille, que l’un et l’autre meurent, parce que c’est un crime qu’ils ont commis: que leur sang soit sur eux.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
13 Celui qui dort avec un homme comme avec une femme, l’un et l’autre a fait une action horrible; qu’ils meurent de mort: que leur sang soit sur eux.
“‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
14 Celui qui, outre la fille devenue sa femme, a épousé la mère, a commis un crime: il sera brûlé vif avec elles, et une action aussi horrible ne persistera pas au milieu de vous.
“‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
15 Que celui qui s’approchera d’une bête de gros ou de menu bétail, meure de mort: tuez aussi la bête.
“‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
16 Une femme qui ira avec une bête quelle qu’elle soit, sera tuée avec elle: que leur sang soit sur elles.
“‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
17 Si quelqu’un prend sa sœur, fille de son père, ou fille de sa mère et voit sa nudité, et que cette sœur aperçoive l’ignominie de son frère, ils ont fait une chose horrible: ils seront tués en la présence de leur peuple, parce qu’ils ont découvert leur nudité l’un à l’autre, et ils porteront leur iniquité.
“‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
18 Celui qui s’approche d’une femme pendant ses mois et révèle sa nudité, et qu’elle-même se fasse voir en cet état, ils seront exterminés tous les deux du milieu de leur peuple.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
19 Tu ne découvriras point la nudité de ta tante maternelle et de ta tante paternelle: celui qui le fait, met à nu l’ignominie de sa chair; ils porteront tous deux leur iniquité.
“‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
20 Celui qui s’approche de la femme de son oncle paternel ou de son oncle maternel, et révèle l’ignominie de sa parenté, il portera comme elle son péché: ils mourront sans enfants.
“‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
21 Celui qui a épousé la femme de son frère, a fait une chose illicite; il a révélé la honte de son frère: il sera ainsi qu’elle sans enfants.
“‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
22 Gardez mes lois et mes ordonnances, et exécutez-les, afin qu’elle ne vous vomisse point aussi, la terre dans laquelle vous devez entrer, et vous devez habiter.
“‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
23 Ne marchez point dans les lois des nations que je dois chasser moi-même devant vous. Car elles ont fait toutes ces choses, et je les ai eues en abomination.
Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
24 Mais à vous, je dis: Possédez leur terre que je vous donnerai en héritage, terre où coulent du lait et du miel. Je suis votre Dieu, qui vous ai séparés de tous les autres peuples.
Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 Séparez donc, vous aussi, la bête pure de l’impure et l’oiseau pur de l’impur; ne souillez point vos âmes par les bêtes, par les oiseaux et par tout ce qui se meut sur la terre, et que je vous ai montré être impur.
“‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
26 Vous me serez saints, parce que je suis saint, moi le Seigneur, et je vous ai séparés de tous les autres peuples, afin que vous fussiez à moi.
Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
27 Qu’un homme ou une femme, dans lesquels se trouve un esprit de python ou de divination, meurent de mort: on les lapidera; que leur sang soit sur eux.
“‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”

< Lévitique 20 >