< Lamentations 5 >
1 Souvenez-vous, Seigneur, de ce qui nous est arrivé; considérez et regardez notre opprobre.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Notre héritage est passé à des ennemis, nos maisons à des étrangers.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Nous sommes devenus comme des orphelins sans pères, et nos mères comme des veuves.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Nous avons bu notre eau à prix d’argent, nous avons acheté chèrement notre bois.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Nous étions conduits par des chaînes attachées à nos cous, à ceux qui étaient fatigués on ne donnait pas de repos.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Nous avons donné la main à l’Egypte et aux Assyriens, afin de nous rassasier de pain.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Nos pères ont péché, et ils ne sont plus; et nous, nous avons porté leurs iniquités.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Des esclaves nous ont dominés; il n’y a eu personne qui nous arrachât de leur main.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Au péril de nos âmes, nous allions nous chercher du pain à la face du glaive du désert.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Notre peau, comme un four, a été brûlée par les ardeurs de la faim.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Ils ont humilié des femmes dans Sion, et des vierges dans les cités de Juda,
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Des princes ont été pendus par la main; on n’a pas révéré la face des vieillards.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Ils ont indignement abusé des jeunes hommes; et des enfants ont succombé sous le bois.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Des vieillards ont abandonné les portes, et de jeunes hommes, le chœur des joueurs de psaltérion.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 La joie de notre âme a fait défaut; notre chœur a été changé en deuil.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Elle est tombée, la couronne de notre tête; malheur à nous, parce que nous avons péché!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 À cause de cela, notre cœur est devenu triste; pour cela, nos yeux se sont couverts de ténèbres.
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 À cause de la montagne de Sion, qui a été détruite, les renards s’y sont promenés.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Mais vous, Seigneur, vous demeurerez éternellement; votre trône subsistera dans toutes les générations.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Pourquoi nous oublierez-vous à jamais? Pourquoi nous abandonnerez-vous dans la longueur des jours?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Convertissez-nous à vous, et nous serons convertis; Seigneur, renouvelez nos jours comme au commencement.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Mais nous rejetant, vous nous avez repoussés; vous êtes extrêmement irrité contre nous.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.