< Juges 9 >

1 Or, Abimélech, fils de Jérobaal, s’en alla à Sichem vers les frères de sa mère, et il leur parla, ainsi qu’à toute la parenté de la maison du père de sa mère, disant:
Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
2 Dites à tous les habitants de Sichem: Lequel est le meilleur pour vous, que soixante-dix hommes, tous fils de Jérobaal, vous commandent, ou qu’un seul homme vous commande? et considérez en même temps que je suis votre os et votre chair.
“Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
3 Et les frères de sa mère rapportèrent à son sujet toutes ces paroles aux hommes de Sichem, et ils firent pencher leur cœur pour Abimélech, disant: C’est notre frère.
Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
4 Et ils lui donnèrent soixante-dix sicles pesant d’argent du temple de Baalberith. Abimélech réunit à lui avec cet argent des hommes misérables et vagabonds; et ils le suivirent.
Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
5 Alors il vint dans la maison de son père à Ephra, et il tua ses frères, fils de Jérobaal, soixante-dix hommes, sur une seule pierre: mais il resta Joatham, le fils de Jérobaal le plus petit, et il fut caché.
Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
6 Or, tous les hommes de Sichem s’étant assemblés, et toutes les familles de la ville de Mello, ils allèrent, et établirent roi Abimélech près du chêne qui était à Sichem.
Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
7 Lorsque cela fut annoncé à Joatham, il alla, et se tint au sommet de la montagne de Garizim, et, la voix élevée, il cria et dit: Écoutez-moi, hommes de Sichem, et qu’ainsi Dieu vous entende.
Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
8 Les arbres allèrent pour oindre et établir sur eux un roi, et ils dirent à l’olivier: Commande-nous.
Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
9 L’olivier leur répondit: Est-ce que je peux abandonner mon huile dont les dieux et les hommes se servent, et venir pour être promu, parmi les arbres?
“Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
10 Les arbres dirent ensuite au figuier: Viens, et règne sur nous.
Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
11 Le figuier leur répondit: Est-ce que je puis abandonner ma douceur et mes fruits très suaves, et aller pour être promu parmi tous les autres arbres?
Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
12 Alors les arbres dirent à la vigne: Viens, et commande-nous.
Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
13 La vigne leur répondit: Est-ce que je puis abandonner mon vin, qui réjouit Dieu et les hommes, et être promu parmi tous les autres arbres?
Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
14 Et tous les arbres dirent au buisson: Viens, et règne sur nous.
Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
15 Le buisson leur répondit: Si vraiment vous me constituez votre roi, venez et reposez-vous sous mon ombre; mais si vous ne voulez pas, qu’un feu sorte du buisson, et qu’il dévore les cèdres du Liban.
Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
16 Maintenant donc, est-ce justement et sans péché que vous avez constitué sur vous Abimélech roi? avez-vous bien agi envers Jérobaal et envers sa maison? et avez-vous payé de retour les bienfaits de celui qui a combattu pour vous,
Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
17 Qui a livré son âme aux périls, pour vous délivrer de la main de Madian,
Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
18 Vous qui maintenant venez de vous élever contre la maison de mon père, qui avez tué ses fils, soixante-dix hommes sur une seule pierre, et constitué roi sur les habitants de Sichem, Abimélech, fils de sa servante, parce qu’il est votre frère?
Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
19 Si donc, c’est justement et sans péché, que vous avez agi envers Jérobaal et sa maison, réjouissez-vous aujourd’hui en Abimélech, et que lui se réjouisse en vous.
Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
20 Mais si c’est méchamment, qu’un feu sorte de lui, qu’il consume les habitants de Sichem et la ville de Mello; qu’un feu sorte des hommes de Sichem et de la ville de Mello, et qu’il dévore Abimélech.
Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
21 Lorsqu’il eut dit ces choses, il s’enfuit et s’en alla à Béra; et il habita là par la crainte d’Abimélech son frère.
Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
22 C’est pourquoi Abimélech régna sur Israël pendant trois ans.
Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
23 Mais le Seigneur envoya un esprit très mauvais entre Abimélech et les habitants de Sichem, qui commencèrent à le délester,
Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
24 Et à rejeter le crime du meurtre des soixante-dix fils de Jérobaal, et l’effusion de leur sang sur Abimélech leur frère et sur tous les autres princes de Sichem, qui l’avaient aidé.
Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
25 Ils lui dressèrent donc des embûches au sommet des montagnes; et pendant qu’ils attendaient son arrivée, ils exerçaient des brigandages, faisant du butin sur les passants. Et on l’annonça à Abimélech.
Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
26 Cependant Gaal. fils d’Obed, vint avec ses frères et passa à Sichem. À son arrivée, les habitants de Sichem rassurés,
Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
27 Sortirent dans les champs, ravageant les vignes, et foulant aux pieds les raisins; puis, des chœurs de chantants formés, ils entrèrent dans le temple de leur dieu, et, au milieu des mets et des coupes, ils maudissaient Abimélech,
Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
28 Gaal, fils d’Obed, criant: Qui est Abimélech, et quelle est Sichem, pour que nous le servions? N’est-il pas le fils de Jérobaal, et n’a-t-il pas constitué Zébul, son serviteur, prince sur les hommes d’Hémor, père de Sichem? Pourquoi donc le servirions-nous?
Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
29 Plût à Dieu que quelqu’un mît ce peuple sous ma main, pour que j’enlevasse du monde Abimélech! Et on dit à Abimélech: Assemble une multitude de troupes, et viens.
Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
30 Car Zébul prince de la ville, ayant entendu les discours de Gaal, fils d’Obed, fut très irrité,
Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
31 Et il envoya en cachette vers Abimélech, disant: Voilà, Gaal, fils d’Obed, est venu à Sichem avec ses frères, et ils attaquent la ville contre toi.
Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
32 C’est pourquoi lève-toi pendant la nuit avec le peuple qui est avec toi, et cache-toi dans la campagne;
Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
33 Et de grand matin, le soleil se levant, fonds sur la ville; or, lorsqu’il sortira avec son peuple contre toi, fais-lui ce que tu pourras.
Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
34 C’est pourquoi Abimélech se leva avec toute son armée pendant la nuit, et tendit des embûches près de Sichem, en quatre endroits.
Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
35 Or, Gaal, fils d’Obed, sortit, et se tint à l’entrée de la porte de la ville. Mais Abimélech se leva, et toute son armée avec lui, du lieu de l’embuscade.
Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
36 Et lorsque Gaal eut vu ce peuple, il dit à Zébul: Voici une multitude qui descend des montagnes. Zébul lui répondit: Tu vois les ombres des montagnes comme des têtes d’hommes, et tu es trompé par cette illusion.
Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
37 Et de nouveau Gaal dit: Voici un peuple qui descend des hauteurs de la terre, et un seul bataillon vient par la voie qui regarde le chêne.
Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
38 Zébul lui répondit: Où est maintenant ta bouche avec laquelle tu disais: Qui est Abimélech, pour que nous le servions? N’est-ce pas ce peuple que tu méprisais? Sors et combats contre lui.
Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
39 Gaal s’en alla donc, le peuple de Sichem le regardant, et il combattit contre Abimélech,
Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
40 Qui le poursuivit pendant qu’il fuyait et le chassa dans la ville; et nombre des siens succombèrent jusqu’à la porte de la ville.
Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
41 Et Abimélech s’arrêta à Ruma; mais Zébul chassa Gaal et ses gens de la ville, il ne souffrit pas qu’ils y demeurassent.
Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
42 Or le jour suivant le peuple sortit dans la campagne. Lorsqu’on l’eut annoncé à Abimélech
Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
43 Il prit son armée et la divisa en trois corps, tendant des embûches dans les champs. Et voyant que le peuple sortait de la ville, il se leva et fondit sur eux
Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
44 Avec son bataillon, attaquant et assiégeant la ville; mais les deux autres bataillons poursuivaient les ennemis fuyant ça et là dans la plaine.
Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
45 Or, pendant tout ce jour-là, Abimélech attaquait la ville qu’il prit, tuant ses habitants et détruisant la ville elle-même, de manière à y semer du sel.
Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
46 Ce qu’ayant appris ceux qui habitaient dans la tour de Sichem, ils entrèrent dans le temple de leur dieu Berith, où ils avaient fait alliance avec lui; et C’est de cette alliance qu’avait reçu son nom le lieu qui était très fortifié.
Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
47 Abimélech aussi, apprenant que les hommes de la tour de Sichem s’étaient réunis ensemble,
Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
48 Monta sur la montagne de Selmon avec tout son peuple, et saisissant la hache il coupa une branche d’arbre, et la mettant sur son épaule il dit aux siens: Ce que vous me voyez faire, faites-le vite.
Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
49 Coupant donc à l’envi des branches d’arbres, ils suivaient leur chef; et environnant la forteresse, ils l’incendièrent; et de cette manière il arriva que par la fumée et par le feu il périt mille personnes, tant hommes que femmes, qui demeuraient dans la tour de Sichem.
Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
50 Ensuite Abimélech, partant de là, vint à la ville de Thébès, qu’investissant, il assiégeait avec son armée.
Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
51 Or, il y avait au milieu de la ville une tour élevée, dans laquelle s’étaient réfugiés ensemble les hommes et les femmes et tous les princes de la ville, la porte étant bien fermée, et ils se tenaient sur le toit de la tour, derrière les parapets.
Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
52 Et Abimélech, s’avançant près de la tour, combattait vaillamment; et, s’approchant de la porte, il s’efforçait d’y mettre le feu.
Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
53 Et voilà qu’une femme, jetant d’en haut un morceau de meule, frappa la tête d’Abimélech et brisa son crâne.
Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
54 Il appela aussitôt son écuyer, et il lui dit: Tire ton glaive, et frappe-moi, de peur qu’on ne dise que c’est par une femme que j’ai été tué. L’écuyer, exécutant ses ordres, le tua.
Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
55 Abimélech mort, tous ceux d’Israël qui étaient avec lui retournèrent en leurs demeures.
Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
56 Ainsi Dieu rendit le mal qu’Abimélech avait commis contre son père, ayant tué ses soixante-dix frères.
Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
57 Aux Sichémites aussi, ce qu’ils avaient fait fut rendu, et la malédiction de Joatham, fils de Jérobaal, vint sur eux.
Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.

< Juges 9 >