< Josué 24 >

1 Et Josué assembla toutes les tribus d’Israël à Sichem, et il appela les anciens, les princes, les juges et les magistrats; et ils se tinrent en la présence du Seigneur;
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 Et il parla ainsi au peuple: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d’Israël: C’est au-delà du fleuve qu’ont habité vos pères dès le commencement, Tharé, père d’Abraham et de Nachor, et ils ont servi des dieux étrangers.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 Je pris donc votre père Abraham du pays de la Mésopotamie, et je l’amenai dans la terre de Chanaan, et je multipliai sa race.
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 Et je lui donnai Isaac, et à Isaac ensuite Jacob et Esaü. Quant à ceux-ci, je donnai à Esaü la montagne de Séir, pour la posséder; mais Jacob et ses fils descendirent en Egypte.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 Et j’envoyai Moïse et Aaron, et je frappai l’Egypte d’un grand nombre de signes et de prodiges.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 Et je vous retirai, vous et vos pères de l’Egypte, et vous vîntes à la mer. Alors les Egyptiens poursuivirent vos pères avec des chars et de la cavalerie jusqu’à la mer Rouge.
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 Mais les enfants d’Israël crièrent au Seigneur, qui mit des ténèbres entre vous et les Egyptiens, et amena sur eux la mer, et les couvrit. Vos yeux ont vu tout ce que j’ai fait en Egypte, et vous avez habité dans le désert pendant longtemps;
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 Après cela, je vous ai introduits dans la terre de l’Amorrhéen, qui habitait au-delà du Jourdain. Et lorsqu’ils combattaient contre vous, je les livrai en vos mains; et vous avez possédé leur terre, et vous les avez tués.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 Cependant se leva Balac, fils de Séphor, roi de Moab, et il combattit contre Israël. Il envoya et appela Balaam, fils de Béor, pour vous maudire;
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 Et moi, je ne voulus point l’écouter; mais au contraire je vous bénis par lui, et je vous délivrai de sa main.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 Vous passâtes le Jourdain et vous vîntes à Jéricho. Alors combattirent contre vous les hommes de cette ville, l’Amorrhéen, le Phérézéen, le Chananéen, l’Héthéen, le Gergéséen, l’Hévéen et le Jébuséen, et je les livrai en vos mains.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 De plus, j’envoyai devant vous des frelons, et je les chassai de leur pays, les deux rois des Amorrhéens, non par ton épée, ni par ton arc.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 Je vous donnai une terre dans laquelle vous n’avez pas travaillé, et des villes que vous n’avez pas bâties, pour que vous y habitiez; des vignes, et des lieux couverts d’oliviers que vous n’avez pas plantés.
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 Maintenant donc craignez le Seigneur, et servez-le avec un cœur parfait et très sincère; enlevez les dieux qu’ont servis vos pères dans la Mésopotamie et dans l’Egypte, et servez le Seigneur.
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 Si, au contraire, c’est un mal à vos yeux que de servir le Seigneur, l’option vous est donnée. Choisissez aujourd’hui ce qui vous plaît, et voyez qui vous devez servir plutôt, ou les dieux qu’ont servi vos pères dans la Mésopotamie, ou les dieux des Amorrhéens, dans la terre desquels vous habitez; pour moi et ma maison, nous servirons le Seigneur.
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 Et le peuple répondit, et dit: Loin de nous que nous abandonnions le Seigneur, et que nous servions des dieux étrangers.
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 Le Seigneur notre Dieu lui-même nous a retirés, nous et nos pères, de la terre d’Egypte, de la maison de servitude; il a fait, nous le voyant, de grands prodiges, et il nous a gardés dans tout le chemin par où nous avons marché, et parmi tous les peuples chez lesquels nous avons passé.
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 Et il a chassé toutes les nations, l’Amorrhéen habitant de la terre dans laquelle nous, nous sommes entrés. Nous servirons donc le Seigneur, parce que c’est lui qui est notre Dieu.
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 Et Josué dit au peuple: Vous ne pourrez pas servir le Seigneur; car c’est un Dieu saint et fort jaloux, et il ne pardonnera pas vos crimes et vos péchés.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 Si vous abandonnez le Seigneur et servez des dieux étrangers, il se tournera, vous affligera et vous renversera, après qu’il vous aura donné des biens.
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 Le peuple répliqua à Josué: Il n’en sera nullement comme tu dis; mais nous servirons le Seigneur.
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 Et Josué au peuple: Vous êtes témoins, repartit-il, que vous choisissez vous-mêmes le Seigneur pour le servir. Ils répondirent: Témoins.
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 Maintenant donc, reprit-il, ôtez les dieux étrangers d’au milieu de vous, et inclinez vos cœurs devant le Seigneur Dieu d’Israël.
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 Et le peuple répondit à Josué: C’est le Seigneur notre Dieu que nous servirons, et nous obéirons à ses préceptes.
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 Josué fit donc alliance en ce jour-là, et il proposa au peuple des préceptes et des ordonnances à Sichem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 Il écrivit aussi toutes ces paroles dans le livre de la loi du Seigneur, et il prit une très grande pierre, et il la plaça sous le chêne qui était dans le sanctuaire du Seigneur,
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 Et il dit à tout le peuple: Voici que cette pierre vous sera en témoignage, qu’elle a entendu toutes les paroles que le Seigneur vous a dites, de peur que dans la suite vous ne vouliez le nier, et mentir au Seigneur votre Dieu.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 Et il renvoya le peuple chacun en sa possession.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 Et après cela mourut Josué, fils de Nun, à l’âge de cent dix ans;
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 Et on l’ensevelit dans les limites de sa possession, à Tamnathsaré, qui est située sur la montagne d’Ephraïm, vers la partie septentrionale de la montagne de Gaas.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 Ainsi, Israël servit le Seigneur durant tous les jours de Josué et des anciens qui vécurent longtemps après Josué, et qui connaissaient toutes les œuvres du Seigneur qu’il avait faites en Israël.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 Les os de Joseph aussi, que les enfants d’Israël avaient emportés de l’Égypte, on les ensevelit à Sichem, dans la partie du champ que Jacob avait achetée des fils d’Hémor, père de Sichem, pour cent jeunes brebis, et qui devint la propriété des enfants de Joseph.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 Eléazar, fils d’Aaron, mourut aussi, et on l’ensevelit à Gabaath, ville de Phinéès, son fils, qui lui fut donnée en la montagne d’Ephraïm.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.

< Josué 24 >