< Josué 2 >

1 Josué, fils de Nun, envoya donc de Sétim deux hommes comme espions secrets, et il leur dit: Allez et considérez la terre et la ville de Jéricho. Et ceux-ci s’étant mis en chemin, entrèrent dans la maison d’une femme de mauvaise vie, du nom de Rahab, et se reposèrent chez elle.
Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
2 Or, on l’annonça au roi de Jéricho, et on lui dit: Voilà que des hommes d’entre les enfants d’Israël sont entrés ici pendant la nuit pour explorer la terre.
Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
3 Et le roi de Jéricho envoya chez Rahab, disant: Fais sortir les hommes qui sont venus chez toi, et qui sont entrés dans ta maison; car ce sont des espions, et ils sont venus considérer toute cette terre.
Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
4 Mais Rahab, prenant ces hommes, les cacha, et dit: Je l’avoue, ils sont venus chez moi, mais je ne savais pas d’où ils étaient:
Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
5 Et comme on fermait la porte de la ville pendant la nuit, ils sont sortis en même temps; je ne sais où ils sont allés: poursuivez-les promptement et vous les atteindrez.
Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
6 Mais elle, elle fit monter ces hommes sur la terrasse de sa maison, et elle les couvrit avec de la paille de Un, qui était là.
Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
7 Or, ceux qui avaient été envoyés les poursuivirent par la voie qui mène au gué du Jourdain; et, eux sortis, aussitôt la porte fut fermée.
Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
8 Ceux qui étaient cachés ne dormaient pas encore, et voilà que Rahab monta vers eux, et dit:
Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
9 Je sais que le Seigneur vous a livré cette terre; car la terreur de votre nom nous a saisis, et tous les habitants de cette terre sont dans l’abattement.
ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
10 Nous avons appris que le Seigneur a desséché les eaux de la mer rouge, à votre entrée, quand vous êtes sortis de l’Egypte, et ce que vous avez fait aux deux rois des Amorrhéens, qui étaient au-delà du Jourdain, Séhon et Og, que vous avez tués.
Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
11 Et apprenant cela, nous avons craint fortement; notre cœur a défailli, et le courage nous a abandonnés à votre entrée; car le Seigneur votre Dieu est Dieu aussi dans le ciel en haut, et sur la terre en bas.
Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
12 Maintenant donc, jurez-moi par le Seigneur, que, comme je vous ai fait miséricorde, ainsi vous ferez à la maison de mon père, et que vous me donnerez un signe certain,
Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
13 Que vous sauverez mon père et ma mère, mes frères et mes sœurs et tout ce qui est à eux, et que vous arracherez ainsi nos âmes à la mort.
Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
14 Et ils lui répondirent: Que notre âme soit pour vous jusqu’à la mort, si toutefois tu ne nous trahis point; et lorsque le Seigneur nous aura livré cette terre, nous accomplirons envers toi la miséricorde et la fidélité.
Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
15 Elle les fit donc descendre avec une corde par la fenêtre; car sa maison tenait au mur de la ville,
Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
16 Et elle leur dit: Allez vers les montagnes, de peur qu’en revenant, ils ne vous rencontrent; et cachez-vous là trois jours, jusqu’à ce qu’ils reviennent; et alors vous irez par votre chemin.
Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
17 Ils lui répondirent: Nous ne manquerons pas à ce serment par lequel tu nous a adjurés,
Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
18 Si, nous entrant dans cette terre, ce cordon d’écarlate sert de signe, et si tu le lies à la fenêtre par laquelle tu nous a fait descendre, et que tu assembles dans ta maison ton père et ta mère, tes frères et toute ta parenté,
tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
19 Celui qui sortira de la porte de ta maison, son sang sera sur sa tête, et nous, nous y serons étrangers; mais le sang de tous ceux qui seront avec toi dans ta maison retombera sur nous, si quelqu’un les touche.
Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
20 Que si tu veux nous trahir, et publier ces paroles, nous serons libres de ce serment par lequel tu nous as adjurés.
Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
21 Et elle leur répondit: Qu’il soit fait ainsi que vous avez dit. Et les laissant aller, elle suspendit le cordon d’écarlate à la fenêtre.
Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
22 Et eux, cheminant, parvinrent aux montagnes, et demeurèrent là trois jours, jusqu’à ce que revinrent ceux qui les avaient poursuivis; car les cherchant dans tout le chemin, ils ne les trouvèrent pas.
Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
23 Et ceux-ci étant déjà entrés dans la ville, les espions s’en retournèrent, et descendirent de la montagne; puis, le Jourdain passé, ils vinrent vers Josué, fils de Nun, et lui racontèrent tout ce qui leur était arrivé,
Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
24 Et ils dirent: Le Seigneur a livré toute cette terre en nos mains et tous ses habitants sont consternés par la frayeur.
Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

< Josué 2 >