< Josué 13 >

1 Josué était vieux et d’un âge fort avancé, et le Seigneur lui dit: Tu es vieux, et même très avancé en âge, et une terre très étendue est restée, qui n’a pas été encore divisée par le sort:
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 Savoir, toute la Galilée, la terre des Philistins et toute celle de Gessuri,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 Depuis le fleuve fangeux qui arrose l’Egypte jusqu’aux confins d’Accaron, contre l’aquilon; la terre de Chanaan qui est partagée entre les cinq princes des Philistins, celui de Gaza, celui d’Azot, celui d’Ascalon, celui de Geth et celui d’Accaron.
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 Mais au midi sont les Hévéens, toute la terre de Chanaan, Maara des Sidoniens, jusqu’à Aphéca et jusqu’aux frontières des Amorrhéens,
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 Et jusqu’aux pays qui leur sont voisins; de plus, la contrée du Liban contre l’orient, depuis Baalgad, au-dessous de la montagne d’Hermon, jusqu’à ce qu’on entre à Emath;
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 La contrée de tous ceux qui habitent sur la montagne, depuis le Liban jusqu’aux eaux de Maséréphoth, et tous les Sidoniens. Je suis celui qui les exterminerai de la face des enfants d’Israël. Que cela entre donc dans la part de l’héritage d’Israël, comme je t’ai ordonné.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Et maintenant partage la terre en possession aux neuf tribus, et à la demi-tribu de Manassé,
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Avec laquelle Ruben et Gad possédèrent déjà la terre que leur a livrée Moïse, serviteur du Seigneur, au-delà des courants du Jourdain, du côté oriental,
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 Depuis Aroer, qui est située sur la rive du torrent d’Arnon, et au milieu de la vallée; de plus, toute la campagne de Médaba, jusqu’à Dibon;
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 Et toutes les villes de Séhon, roi de l’Amorrhéen, lequel a régné à Hésébon, jusqu’aux frontières des enfants d’Ammon:
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 Galaad, les confins de Gessuri et de Machati; toute la montagne d’Hermon, et tout le Basan, jusqu’à Salécha,
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 Tout le royaume d’Og en Basan, lequel a régné à Astaroth et à Edraï, et qui était des restes des Raphaïm; et Moïse les battit et les détruisit.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 Cependant les enfants d’Israël ne voulurent pas exterminer ceux de Gessuri et de Machati; aussi ont-ils habité au milieu d’Israël jusqu’au présent jour.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Mais à la tribu de Lévi. Moïse ne donna point de possession, parce que les sacrifices et les victimes du Seigneur Dieu d’Israël sont son héritage, comme lui a dit le Seigneur.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Moïse donna donc des possessions à la tribu des enfants de Ruben, selon sa parenté.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Et sa limite fut depuis Aroer, qui est située sur la rive du torrent d’Arnon, et au milieu de la vallée du même torrent, toute la plaine qui conduit à Médaba,
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hésébon, et tous leurs villages qui sont dans la campagne; Dibon aussi, Bamothbaal, la ville de Baalméon,
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 Jassa, Cédimoth, Méphaath,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 Cariathaïm, Sabama, Sarathasar sur la montagne de la vallée,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 Bethphogor et Asédoth, Phasga et Bethiésimoth,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 Et toutes les villes de la plaine, tous les royaumes de Séhon, roi de l’Amorrhéen, qui régna à Hésébon, que Moïse battit avec les princes de Madian, Hévi, Résem, Sur, Hur et Rébé, chefs de Séhon, habitants de cette terre.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 Et les enfants d’Israël firent mourir par le glaive Balaam le devin, fils de Béor, avec tous les autres qui furent tués,
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Et le Jourdain devint la limite des enfants de Ruben. C’est là la possession des villes et des villages des Rubénites, selon leur parenté.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Moïse donna aussi à la tribu de Gad et a ses enfants, selon leur parenté, une possession dont voici la division:
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Sa limite fut Jaser, toutes les villes de Galaad, et la moitié de la terre des enfants d’Ammon, jusqu’à Aroer, qui est contre Rabba,
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 Depuis Hésébon jusqu’à Ramoth, Masphé et Betonim, et depuis Manaïm jusqu’aux confins de Dabir;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 De plus, dans la vallée de Betharan, de Bethnemra, de Socoth et de Saphon, reste du royaume de Séhon, roi d’Hésébon; sa limite est aussi le Jourdain jusqu’à l’extrémité de la mer de Généreth, au-delà du Jourdain, du côté oriental.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Voilà la possession des enfants de Gad, selon leurs familles, voilà les villes et les villages de ces familles.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Moïse donna aussi à la demi-tribu de Manassé et à ses enfants, selon leur parenté, une possession,
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Dont voici le commencement: Depuis Manaïm, tout Basan, tous les royaumes d’Og, roi de Bazan, tous les bourgs de Jaïr qui sont en Basan, soixante villes;
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 Et la moitié de Galaad, Astaroth et Edraï, villes du royaume d’Og, en Basan, aux enfants de Machir, fils de Manassé, c’est-à-dire à la moitié des enfants de Machir, selon leur parenté.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Moïse partagea cette possession dans la plaine de Moab, au-delà du Jourdain, contre Jéricho, du côté oriental.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Mais à la tribu de Lévi, il ne donna pas de possession, parce que le Seigneur Dieu d’Israël est lui-même sa possession, comme il lui a dit.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Josué 13 >