< Josué 10 >
1 Lorsque Adonisédec, roi de Jérusalem, eut appris ces choses, savoir, que Josué avait pris Haï et qu’il l’avait détruite (car comme il avait fait à Jéricho et à son roi, ainsi fit-il à Haï et à son roi), et que les Gabaonites avaient passés aux Israélites, et qu’ils étaient leurs alliés,
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 Il en eut une grande crainte; car Gabaon était une grande ville et une des cités royales, et plus grande que la ville de Haï et tous ses guerriers étaient très vaillants.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 Adonisédec, roi de Jérusalem, envoya donc vers Oham, roi d’Hébron, vers Pharam, roi de Jérimoth, vers Japhia aussi, roi de Lachis, et vers Dabir, roi d’Eglon, disant:
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Montez vers moi, et me portez secours, afin que nous réduisions Gabaon, parce qu’elle a passé à Josué et aux enfants d’Israël.
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 S’étant donc assemblés, les cinq rois des Amorrhéens, le roi de Jérusalem, le roi d’Hébron, le roi de Jérimoth, le roi de Lachis, le roi d’Eglon, montèrent ensemble avec leurs armées, ils campèrent près de Gabaon et l’assiégèrent.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 Mais les habitants de Gabaon, la ville assiégée, envoyèrent à Josué, qui alors était au camp près de Galgala, et lui dirent: Ne retire pas tes mains auxiliaires de tes serviteurs: monte aussitôt, délivre-nous, et porte-nous secours; car tous les rois des Amorrhéens qui habitent dans les montagnes se sont réunis contre nous.
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 Et Josué monta de Galgala, et avec lui toute l’armée des combattants, hommes très vaillants.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 Et le Seigneur dit à Josué: Ne les crains point; car je les ai livrés en tes mains: nul d’entre eux ne pourra te résister.
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 C’est pourquoi Josué montant de Galgala pendant toute la nuit, fondit soudainement sur eux;
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 Et le Seigneur les mit en déroute à la face d’Israël; il en fit un grand carnage à Gabaon, il les poursuivit par la voie de la montée de Béthoron, et les tailla en pièces jusqu’à Azéca et à Macéda.
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 Et lorsqu’ils fuyaient les enfants d’Israël, et qu’ils étaient dans la descente de Béthoron, le Seigneur lança du ciel sur eux de grosses pierres jusqu’à Azéca: et il en mourut beaucoup plus par les pierres de grêle, que les enfants d’Israël n’en avaient tués par le glaive.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 Alors Josué parla au Seigneur, dans le jour qu’il livra l’Amorrhéen en présence des enfants d’Israël, et il dit devant eux: Soleil, ne te meus point contre Gabaon, ni toi, lune, contre la vallée d’Aïalon.
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 Et le soleil et la lune s’arrêtèrent, jusqu’à ce qu’une nation se fut vengée de ses ennemis. Cela n’est-ii pas écrit dans le livre des Justes? C’est pourquoi le soleil s’arrêta au milieu du ciel, et ne se hâta point de se coucher durant l’espace d’un jour.
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 Il n’y eut point avant ni après un aussi long jour, le Seigneur obéissant à la voix d’un homme et combattant pour israël.
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 Et Josué retourna avec tout Israël au camp de Galgala.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 Car les cinq rois s’étaient enfuis et s’étaient cachés dans la caverne de la ville de Macéda.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 Et l’on annonça à Josué que les cinq rois avaient été trouvés cachés dans la caverne de la ville de Macéda.
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 Et Josué ordonna à ceux qui l’accompagnaient, et dit: Roulez de grandes pierres à l’ouverture de la caverne, et placez des hommes intelligents qui gardent ceux qui y sont enfermés.
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 Pour vous, ne vous arrêtez point, mais poursuivez les ennemis, et taillez en pièces tous les derniers des fuyards; et ne les laissez point entrer dans les forteresses de leurs villes, eux que le Seigneur votre Dieu a livrés en vos mains.
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Les ennemis donc ayant été taillés en pièces dans un grand carnage, et presque détruits jusqu’à une entière extermination, ceux qui purent échapper à Israël entrèrent dans les villes fortifiées.
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 Et toute l’armée retourna vers Josué à Macéda, où alors était le camp, saine et sauve, et en nombre complet: et nul n’osa murmurer contre les enfants d’Israël.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 Et Josué ordonna disant: Ouvrez l’entrée de la caverne, et amenez-moi les cinq rois qui y sont cachés.
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 Et les serviteurs firent comme il leur avait été commandé; et ils lui amenèrent de la caverne les cinq rois, le roi de Jérusalem, le roi d’Hébron, le roi de Jérimoth, le roi de Lachis, le roi d’Eglon.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 Et lorsqu’ils eurent été amenés, il appela tous les hommes d’Israël, et il dit aux princes de l’armée, qui étaient avec lui: Allez, et mettez les pieds sur les cous de ces rois. Lorsque ceux-ci furent allés, et pendant qu’ils foulaient leurs cous aux pieds, après les avoir terrassés,
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 Il leur dit de nouveau: Ne craignez point, et ne vous épouvantez pas, prenez courage et soyez forts; car ainsi fera le Seigneur à tous vos ennemis contre lesquels vous combattrez.
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Et Josué les frappa et les tua, et les suspendit à cinq poteaux; et ils furent suspendus jusqu’au soir.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 Et lorsque le soleil se couchait il ordonna à ceux qui l’accompagnaient de les descendre des poteaux. Ceux-ci les ayant descendus, les jetèrent dans la caverne, dans laquelle ils s’étaient cachés, et mirent à l’entrée de grandes pierres, qui sont demeurées jusqu’à présent.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 En ce même jour aussi Josué prit Macéda et la frappa du tranchant du glaive; et il tua son roi et tous ses habitants, et il n’y laissa pas même les moindres restes. Ainsi, il fit au roi de Macéda comme il avait fait au roi de Jéricho.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 Or, il passa avec tout Israël de Macéda à Lebna, et il combattait contre elle.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 Et le Seigneur la livra avec son roi aux mains d’Israël; ils frappèrent du tranchant du glaive la ville et tous ses habitants; ils n’y laissèrent aucun reste. Ainsi, ils firent au roi de Lebna, comme ils avaient fait au roi de Jéricho.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 De Lebna il passa à Lachis avec tout Israël; et, son armée étant rangée tout autour, il l’attaquait.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 Et le Seigneur livra Lachis aux mains d’Israël, et il la prit le second jour, et il frappa du tranchant du glaive, toute âme qui avait été en elle, comme il avait fait à Lebna.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 En ce temps-là monta Horam, roi de Gazer, pour secourir Lachis. Josué le battit avec son armée jusqu’à une dernière extermination.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 Et il passa de Lachis à Eglon et l’assiégea;
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 Et il la prit d’assaut le même jour; et il frappa du tranchant du glaive toutes les âmes qui étaient en elle, selon tout ce qu’il avait fait à Lachis.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 Il monta aussi avec tout Israël d’Eglon à Hébron, et combattit contre elle.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 Il la prit et la frappa du tranchant du glaive, ainsi que son roi et toutes les autres villes de cette contrée, et toutes les âmes qui y étaient demeurées; il n’y laissa aucuns restes: comme il avait fait à Eglon, ainsi fit-il à Hébron, faisant passer par le glaive tout ce qu’il trouva.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 Il la prit et la ravagea; il frappa aussi du tranchant du glaive son roi et toutes les villes d’alentour: il n’y laissa aucuns restes: comme il avait fait à Hébron et à Lebna et à leurs rois, ainsi fit-il à Dabir et à son roi.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 C’est pourquoi Josué frappa toute la terre des montagnes, du midi et de la plaine, et Asédoth avec ses rois: il n’y laissa aucuns restes; mais tout ce qui pouvait respirer, il le tua, comme lui avait ordonné le Seigneur Dieu d’Israël,
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 Depuis Cadesbarné jusqu’à Gaza. Toute la terre de Gosen jusqu’à Gabaon,
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 Et tous leurs rois et leurs contrées, il les prit et les ravagea d’une seule attaque; car le Seigneur Dieu d’Israël combattit pour lui.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 Et il retourna avec tout Israël au lieu du camp, à Galgala.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.