< Jonas 3 >

1 Et la parole du Seigneur fut adressée une seconde fois à Jonas, disant:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
2 Lève-toi, et va dans Ninive la grande cité, et prêches-y ce que moi je te dis de prêcher.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
3 Et Jonas se leva, et alla à Ninive selon la parole du Seigneur; or Ninive était une grande cité de trois jours de chemin.
Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
4 Jonas commença à entrer dans la cité, à faire le chemin d’un jour; et il cria, et il dit: Encore quarante jours et Ninive sera renversée.
Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
5 Les hommes de Ninive crurent en Dieu, et ils publièrent un jeûne, et se revêtirent de cilices, depuis le plus grand jusqu’au plus petit.
Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
6 Et le bruit en parvint au roi de Ninive; et il se leva de son trône, et quitta son vêtement, et se revêtit d’un sac, et s’assit sur la cendre.
Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
7 Et il cria et dit dans Ninive par la bouche du roi et de ses princes, disant: Que les hommes et les animaux, et les bœufs et les troupeaux de menu bétail ne goûtent rien; et qu’ils ne paissent point, et ne boivent point d’eau.
Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
8 Et que les hommes se couvrent de sacs ainsi que les animaux, et qu’ils crient au Seigneur avec force, et que chacun se convertisse de sa voie mauvaise, et de l’iniquité qui est en leurs mains.
Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
9 Qui sait si Dieu ne reviendra pas et ne pardonnera pas; et s’il ne se détournera pas de la fureur de sa colère, et nous ne périrons pas?
Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
10 Et Dieu vit leurs œuvres, il vit qu’ils étaient convertis de leur voie mauvaise; et Dieu eut pitié d’eux, touchant le mal qu’il avait dit qu’il leur ferait, et il ne le fit pas.
Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.

< Jonas 3 >