< Jean 17 >
1 Jésus parla ainsi; puis, levant les yeux au ciel, il dit: Mon Père, elle est venue l’heure; glorifiez votre Fils, afin que votre Fils vous glorifie;
Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
2 Puisque vous lui avez donné puissance sur toute chair, afin que, quant à tous ceux que vous lui avez donnés, il leur donne la vie éternelle. (aiōnios )
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios )
3 Or la vie éternelle, c’est qu’ils vous connaissent, vous seul vrai Dieu, et celui que vous avez envoyé, Jésus-Christ. (aiōnios )
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios )
4 Moi, je vous ai glorifié sur la terre; j’ai consommé l’œuvre que vous m’avez donnée à faire;
Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
5 Et maintenant vous, mon Père, glorifiez-moi en vous-même de la gloire que j’ai eue en vous avant que le monde fût.
Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
6 J’ai manifesté votre nom aux hommes que vous m’avez donnés; ils étaient à vous, vous me les avez donnés, et ils ont gardé votre parole.
“Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
7 Maintenant ils ont connu que tout ce que vous m’avez donné vient de vous;
Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
8 Parce que je leur ai donné les paroles que vous m’avez données; et ils les ont reçues, et ils ont connu véritablement que c’est de vous que je suis sorti, et ils ont cru que c’est vous qui m’avez envoyé.
Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
9 Moi, je prie pour eux; je ne prie point pour le monde, mais pour ceux que vous m’avez donnés, parce qu’ils sont à vous;
Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
10 Car tout ce qui est à moi est à vous, et tout ce qui est à vous est à moi; et j’ai été glorifié en eux.
Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
11 Et déjà je ne suis plus dans le monde, et eux sont dans le monde, et moi je viens à vous. Père saint, conservez en votre nom ceux que vous m’avez donnés, afin qu’ils soient une seule chose, comme nous.
Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
12 Quand j’étais avec eux, je les conservais en votre nom. Ceux que vous m’avez donnés, je les ai gardés, et pas un d’eux n’a péri, hors le fils de la perdition, afin que l’Ecriture fût accomplie.
Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
13 Mais maintenant je viens à vous; et je dis ces choses dans le monde, pour qu’ils aient en eux ma joie complète.
“Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
14 Moi, je leur ai donné votre parole, et le monde les a eus en haine, parce qu’ils ne sont point du monde, comme moi-même je ne suis pas du monde.
Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
15 Je ne demande point que vous les ôtiez du monde, mais que vous les gardiez du mal.
Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
16 Ils ne sont point du monde, comme moi-même je ne suis pas du monde.
Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
17 Sanctifiez-les dans la vérité. Votre parole est vérité.
Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
18 Comme vous m’avez envoyé dans le monde, moi aussi, je les ai envoyés dans le monde.
Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
19 Et pour eux je me sanctifie moi-même, afin qu’eux aussi soient sanctifiés en vérité.
Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
20 Je ne prie pas pour eux seulement, mais encore pour ceux qui, par leur parole, croiront en moi;
“Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
21 Afin qu’ils soient tous une seule chose, comme vous, mon Père, êtes en moi, et moi en vous; qu’ils soient de même une seule chose en nous, et qu’ainsi le monde croie que c’est vous qui m’avez envoyé.
Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
22 Pour moi, je leur ai donné la gloire que vous m’avez donnée, afin qu’ils soient une seule chose, comme nous sommes une seule chose.
Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
23 Je suis en eux et vous en moi, afin qu’ils soient consommés dans l’unité, et que le monde connaisse que c’est vous qui m’avez envoyé, et que vous les avez aimés comme vous m’avez aimé.
Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
24 Mon Père, je veux que là où je suis, ceux que vous m’avez donnés soient aussi avec moi; afin qu’ils voient la gloire que vous m’avez donnée; parce que vous m’avez aimé avant la fondation du monde.
“Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
25 Père juste, le monde ne vous a point connu; mais moi je vous ai connu, et ceux-ci ont connu que c’est vous qui m’avez envoyé.
“Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
26 Je leur ai fait connaître votre nom, et je le leur ferai connaître encore, afin que l’amour dont vous m’avez aimé soit en eux, et moi en eux.
Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”