< Jean 13 >

1 Avant la fête de la pâque, Jésus sachant que son heure était venue de passer de ce monde à son Père, comme il avait aimé les siens, qui étaient dans le monde, il les aima jusqu’à la fin.
Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.
2 Et le souper fini, lorsque déjà le diable avait mis dans le cœur de Judas fils de Simon Iscariote de le trahir;
Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu.
3 Sachant que son Père lui avait remis toutes choses entre les mains, et qu’il était sorti de Dieu et retournait à Dieu,
Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo;
4 Il se leva de table, posa ses vêtements, et ayant pris un linge, il s’en ceignit.
anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake.
5 Ensuite il versa de l’eau dans un bassin, et commença à laver les pieds de ses disciples, et à les essuyer avec le linge dont il était ceint;
Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.
6 Il vint à Simon Pierre, et Pierre lui dit: Vous, Seigneur, vous me lavez les pieds?
Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”
7 Jésus répondit et lui dit: Tu ne sais pas maintenant ce que je fais; mais tu le sauras plus tard.
Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”
8 Pierre lui dit: Jamais vous ne me laverez les pieds. Jésus lui répondit: Si je ne te lave, tu n’auras point de part avec moi, (aiōn g165)
Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn g165)
9 Simon Pierre lui dit: Seigneur, non seulement les pieds, mais encore les mains et la tête.
Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”
10 Jésus lui dit: Celui qui a été lavé n’a besoin que de laver ses pieds, et il est entièrement pur. Vous aussi, vous êtes purs, mais non pas tous.
Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.”
11 Car il savait celui qui le trahirait; c’est pourquoi il dit: Vous n’êtes pas tous purs.
Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.
12 Après donc qu’il leur eut lavé les pieds, et qu’il eut repris ses vêtements, s’étant remis à table, il leur dit: Savez-vous ce que je viens de vous faire?
Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu?
13 Vous m’appelez vous-mêmes Maître et Seigneur; et vous dites bien, car je le suis.
Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili.
14 Si donc je vous ai lavé les pieds, moi votre Maître et votre Seigneur, vous devez, vous aussi, vous laver les pieds les uns aux autres.
Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu.
15 Car je vous ai donné l’exemple, afin que, comme je vous ai fait, vous fassiez aussi vous-mêmes.
Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira.
16 En vérité, en vérité, je vous le dis, le serviteur n’est pas plus grand que son maître, ni l’apôtre plus grand que celui qui l’a envoyé.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma.
17 Si vous savez ces choses, vous serez heureux, pourvu que vous les pratiquiez.
Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.
18 Je ne dis pas ceci de vous tous; je sais bien ceux que j’ai choisis; mais c’est pour que s’accomplisse l’Ecriture: Celui qui mange le pain avec moi, lèvera contre moi son pied.
“Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’
19 Je vous le dis à présent, avant que cela arrive, afin que lorsque ce sera arrivé, vous me croyiez ce que je suis.
“Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine.
20 En vérité, en vérité, je vous le dis: Qui reçoit celui que j’aurai envoyé, me reçoit; et qui me reçoit, reçoit celui qui m’a envoyé.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”
21 Lorsqu’il eut dit ces choses, Jésus fut troublé en son esprit; puis il parla ouvertement et dit: En vérité, en vérité, je vous le dis, un de vous me trahira.
Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”
22 Les disciples donc se regardaient l’un l’autre, incertains de qui il parlait.
Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani.
23 Or un des disciples de Jésus, que Jésus aimait, reposait sur son sein.
Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake.
24 Simon Pierre lui fit donc signe et lui dit: Qui est celui dont il parle?
Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”
25 C’est pourquoi ce disciple s’étant penché sur le sein de Jésus, lui dit: Seigneur, qui est-ce?
Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”
26 Jésus répondit: C’est celui à qui je présenterai du pain trempé. Et ayant trempé du pain, il le donna à Judas Iscariote, fils de Simon.
Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni.
27 Or après une bouchée, Satan entra en lui, et Jésus lui dit: Ce que tu fais, fais-le vite.
Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye. Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.”
28 Mais aucun de ceux qui étaient à table ne sut pourquoi il lui dit cela.
Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye.
29 Car quelques-uns pensaient que comme Judas avait la bourse, Jésus lui avait dit: Achète ce dont nous avons besoin pour la fête, ou donne quelque chose aux pauvres.
Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka.
30 Judas ayant donc pris cette bouchée sortit aussitôt. Or il était nuit.
Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.
31 Lorsqu’il fut sorti, Jésus dit: Maintenant le Fils de l’homme a été glorifié, et Dieu a été glorifié en lui.
Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso.
32 Si Dieu a été glorifié en lui, Dieu aussi le glorifiera en lui-même, et c’est bientôt qu’il le glorifiera.
Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.
33 Mes petits enfants, je ne suis que pour peu de temps encore avec vous. Vous me chercherez, et comme j’ai dit aux Juifs: Où je vais, vous ne pouvez venir; je vous le dis aussi à vous maintenant.
“Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.
34 Je vous donne un commandement nouveau: C’est que vous vous aimiez les uns les autres; mais que vous vous aimiez les uns les autres comme je vous ai aimés.
“Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake.
35 C’est en cela que tous connaîtront que vous êtes mes disciples, si vous avez de l’amour les uns pour les autres.
Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”
36 Simon Pierre lui dit: Seigneur, où allez-vous? Jésus répondit: Où je vais, tu ne peux me suivre à présent; mais tu me suivras ensuite.
Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”
37 Pierre lui dit: Pourquoi ne puis-je vous suivre à présent? Je donnerai mon âme pour vous.
Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”
38 Jésus lui répondit: Tu donneras ton âme pour moi? En vérité, en vérité, je te le dis, un coq ne chantera pas que tu ne m’aies renié trois fois.
Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”

< Jean 13 >