< Job 5 >

1 Appelle donc, s’il y a quelqu’un qui te réponde, et tourne-toi vers quelqu’un des saints.
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Certes, le courroux tue l’insensé, et l’envie fait mourir le jeune enfant.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Moi, j’ai vu l’insensé avec une forte racine, et j’ai maudit sa beauté aussitôt.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Ses fils se trouveront loin du salut, et ils seront brisés à la porte, et il n’y aura personne qui les délivre.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Le famélique mangera sa moisson: l’homme armé le ravira lui-même, et ceux qui ont soif boiront ses richesses.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Rien sur la terre ne se fait sans cause, et ce n’est pas du sol que provient la douleur.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 L’homme naît pour le travail, et l’oiseau pour voler.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 C’est pourquoi je prierai le Seigneur, et c’est à Dieu que j’adresserai ma parole,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Lui qui fait des choses grandes, impénétrables et admirables, sans nombre;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Qui donne de la pluie sur la face de la terre, et arrose d’eaux tous les lieux;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Qui élève les humbles, ranime ceux qui sont abattus en les protégeant;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Qui dissipe les pensées des méchants, afin que leurs mains ne puissent accomplir ce qu’elles avaient commencé;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Qui surprend les sages dans leur finesse, et dissipe le conseil des pervers.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Dans le jour ils rencontreront des ténèbres, et comme dans la nuit, ainsi ils tâtonneront à midi.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Mais Dieu sauvera l’indigent du glaive de leur bouche, et le pauvre de la main du violent.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Et il y aura de l’espérance pour l’indigent, mais l’iniquité contractera sa bouche.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Heureux l’homme qui est corrigé par Dieu! ne repousse donc pas le châtiment du Seigneur,
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Parce que lui-même blesse, et il donne le remède; il frappe, et ses mains guériront.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Dans six tribulations il te délivrera, et, à la septième, le mal ne te touchera pas.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Dans la famine, il te sauvera de la mort, et à la guerre, de la main du glaive.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Tu seras mis à couvert du fouet de la langue, et tu ne craindras pas la calamité lorsqu’elle viendra.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Dans la désolation et la faim tu riras, et tu ne redouteras pas les bêtes de la terre.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Il y aura même un accord entre toi et les pierres des champs; et les bêtes de la terre seront pacifiques pour loi.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Et tu verras que ton tabernacle aura la paix; et, visitant ta beauté, tu ne pécheras pas.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Tu verras aussi que ta race se multipliera, et ta postérité croîtra comme l’herbe de la terre.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Tu entreras dans l’abondance au sépulcre, comme un monceau de blé qui est rentré en son temps.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Vois, ceci est comme nous l’avons observé: ce que tu as entendu, repasse-le en ton esprit.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >