< Job 19 >
1 Or, répondant, Job dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jusques a quand affligerez-vous mon âme, et me briserez-vous par vos discours?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Voilà déjà dix fois que vous cherchez à me confondre, et que vous ne rougissez pas de m’accabler.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Car si je suis dans l’ignorance, c’est sur moi que mon ignorance retombera.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Mais vous, vous vous élevez contre moi, et vous m’accusez à cause de mes opprobres.
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Comprenez au moins maintenant que ce n’est pas par un jugement de justice, que Dieu m’a affligé et qu’il m’a environné de ses châtiments.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Voici que je crierai, en souffrant violence, et nul ne m’écoutera; je pousserai des cris perçants, et il n’y aura personne qui me fasse justice.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Il a posé une haie tout autour de mon sentier, et je ne puis passer; et dans mon chemin, il a mis des ténèbres.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Il m’a dépouillé de ma gloire, et il a enlevé la couronne de ma tête, de moi.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Il m’a détruit de tous côtés, et je péris, et il m’a ôté l’espérance comme à un arbre arraché.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Sa fureur s’est irritée contre moi; il m’a traité comme son ennemi.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ses soldats sont venus tous ensemble; ils se sont fait un chemin au travers de moi, et ils ont assiégé mon tabernacle tout autour.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Il a éloigné mes frères de moi, et mes amis, comme des étrangers, se sont retirés de moi.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Mes proches m’ont abandonné, et ceux qui me connaissaient m’ont oublié.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Ceux qui demeuraient dans ma maison, et mes servantes m’ont regardé comme un étranger, et j’ai été comme un hôte passager à leurs yeux.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 J’ai appelé mon serviteur, et il ne m’a pas répondu; cependant je le priais de ma propre bouche.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Ma femme a eu horreur de mon haleine, et j’usais de prière envers les enfants qui sont sortis de moi.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Des insensés même me méprisaient, et lorsque je les avais quittés, ils médisaient de moi.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Mes conseillers d’autrefois m’ont en abomination, et celui que j’aimais le plus s’est tourné contre moi.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 À ma peau, après que ma chair a été consumée, se sont collés mes os, et il n’est resté seulement que les lèvres autour de mes dents.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Ayez pitié de moi, ayez pitié de moi, vous du moins, mes amis, parce que la main du Seigneur m’a touché.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Pourquoi me persécutez-vous comme Dieu, et vous rassasiez-vous de ma chair?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Qui m’accordera que mes paroles soient écrites? Qui me donnera qu’elles soient tracées dans un livre,
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Avec un style de fer et sur une lame de plomb, ou qu’elles soient gravées au burin sur la pierre?
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Car je sais que mon Rédempteur est vivant, et qu’au dernier jour je ressusciterai de la terre;
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Et que de nouveau je serai environné de ma peau, et que dans ma chair je verrai mon Dieu.
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Je dois le voir moi-même, et non un autre, et mes yeux doivent le contempler: c’est là mon espérance; elle repose dans mon sein.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Pourquoi donc maintenant dites-vous: Poursuivons-le, et trouvons une parole fondamentale contre lui?
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Fuyez donc à la face du glaive, parce qu’il y a un glaive vengeur des iniquités; et sachez qu’il y a un jugement.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”