< Jérémie 6 >

1 Fortifiez-vous, fils de Benjamin, au milieu de Jérusalem, et dans Thécua sonnez de la trompette, et sur Bethacarem levez l’étendard; parce qu’un mal a été vu du côté de l’aquilon, ainsi qu’une grande destruction.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 À une femme belle et délicate j’ai comparé la fille de Sion.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Vers elle viendront les pasteurs et leurs troupeaux; ils ont dressé leurs tentes à l’entour; chacun d’eux fera paître ceux qui sont sous sa main.
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 Consacrez contre elle une guerre; levez-vous, et montons au milieu du jour; malheur à nous, parce que le jour décline, parce que les ombres du soir sont allongées.
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Levez-vous et montons pendant la nuit, et renversons ses maisons.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Parce que voici ce que dit le Seigneur des armées: Coupez ses arbres, et faites autour de Jérusalem un rempart; c’est la cité de la Visitation; toute sorte de violence est au milieu d’elle.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Comme la citerne rend froide son eau, ainsi cette cité a commis froidement ses méchancetés; iniquité et ravage, c’est ce qui sera ouï en elle; devant moi elle est toujours infirmité et plaie.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Instruis-toi, Jérusalem, de peur que mon âme ne se retire de toi, et que je ne fasse de toi un désert, une terre inhabitable.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Voici ce que dit le Seigneur des armées: On rassemblera les restes d’Israël comme dans une vigne jusqu’à la dernière grappe; reporte ta main comme le vendangeur dans la corbeille.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 À qui parlerai-je? et qui prendrai-je à témoin pour qu’il entende? voici que leurs oreilles sont incirconcises, et qu’ils ne peuvent entendre. Voici que la parole du Seigneur leur est devenue un opprobre; et ils ne la recevront pas.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 C’est pour cela que je suis plein de la fureur du Seigneur et que j’ai peine à la supporter; répandez-la sur le petit enfant au dehors, et sur le conseil des jeunes gens assemblés; car l’homme sera pris avec la femme, le vieillard avec celui qui est plein de jours.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Et leurs maisons passeront à des étrangers, leurs champs, et leurs femmes également, parce que j’étendrai ma main sur ceux qui habitent la terre, dit le Seigneur.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 Depuis le plus petit jusqu’au plus grand, tous se livrent à l’avarice; et depuis le prophète jusqu’au prêtre, tous agissent avec tromperie.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 Et ils guérissaient la plaie de la fille de mon peuple avec ignominie, disant: Paix, paix; et il n’y avait point de paix.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Ils ont été confus, parce qu’ils ont fait des abominations; et encore ne l’ont-ils pas été entièrement, et n’ont-ils pas su rougir; à cause de cela ils tomberont parmi ceux qui sont renversés; au temps de leur Visitation, ils seront renversés tous ensemble, dit le Seigneur.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Voici ce que dit le Seigneur: Tenez-vous sur les voies et voyez; demandez, touchant les sentiers anciens, quelle est la bonne voie, et marchez-y; et vous trouverez un rafraîchissement pour vos âmes. Et ils ont dit: Nous n’y marcherons pas.
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Et j’ai établi sur vous des sentinelles. Ecoutez la voix de la trompette. Et ils ont dit: Nous ne l’écouterons pas.
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 C’est pourquoi, écoutez, nations, et apprenez, assemblée des peuples, les grandes choses que je ferai contre eux.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Ecoute, terre: Voilà que moi j’amènerai sur ce peuple des maux, fruit de ses pensées, parce qu’ils n’ont point écouté mes paroles et qu’ils ont rejeté ma loi.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 Pourquoi m’apportez-vous de l’encens de Saba, et la canne à l’odeur suave d’une terre éloignée? Vos holocaustes ne me sont pas agréables, et vos victimes ne m’ont pas plu.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Voilà que je ferai fondre sur ce peuple des ruines; les pères y tomberont et les fils en même temps; les voisins et les proches y périront.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Voici ce que dit le Seigneur: Voilà qu’un peuple vient de la terre de l’aquilon, et une grande nation s’élèvera des confins de la terre.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Elle saisira la flèche et le bouclier; elle est cruelle et elle n’aura pas de pitié; sa voix comme la mer retentira; et ils monteront sur leurs chevaux, et préparés comme un homme qui va au combat, ils marcheront contre toi, fille de Sion.
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 Nous avons ouï la nouvelle de son dessein, nos mains ont défailli; la tribulation nous a saisis, et les douleurs comme la femme en travail.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Ne sortez point dans les champs, et dans la voie ne marchez point, parce que le glaive de l’ennemi et l’épouvante sont à l’entour.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Fille de mon peuple, ceins-toi d’un cilice, couvre-toi de cendre; sois en deuil comme d’un fils unique, pousse des plaintes amères, parce que tout d’un coup viendra le dévastateur sur nous.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Je t’ai établi au milieu de mon peuple comme un fondeur robuste; tu sauras, et tu éprouveras leur voie.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Tous ses princes ont dévié, marchant frauduleusement; c’est de l’airain et du fer; tous se sont corrompus.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Le soufflet a manqué, dans le feu s’est consumé le plomb; en vain le fondeur les a mis dans le fourneau; car leurs méchancetés n’ont pas été consumées.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Appelez-les un argent réprouvé, parce que le Seigneur les a rejetés.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jérémie 6 >