< Jérémie 51 >
1 Voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi je susciterai sur Babylone et sur ses habitants, qui ont élevé leur cœur contre moi, comme un vent pestilentiel.
Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
2 Et j’enverrai contre Babylone des gens le van à la main; et ils la vanneront, et ils ruineront sa terre. De tous côtés ils sont venus sur elle au jour de son affliction.
Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
3 Que celui qui tend son arc ne le tende pas, et que nul ne monte cuirassé; n’épargnez point ses jeunes hommes; tuez toute sa milice.
Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
4 Et les tués tomberont dans la terre des Chaldéens, et les blessés dans ses provinces.
Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
5 Parce qu’Israël et Juda ne sont pas veufs de leur Dieu, le Seigneur des armées; mais leur terre a été remplie de crimes contre le saint d’Israël.
Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
6 Fuyez du milieu de Babylone, et que chacun sauve son âme; ne vous taisez point sur son iniquité; car c’est le temps de la vengeance du Seigneur; lui-même la rétribuera.
“Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
7 Babylone a été une coupe d’or dans la main du Seigneur; elle a enivré toute la terre; les nations ont bu de son vin, c’est pour cela qu’elles ont chancelé.
Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
8 Babylone est tombée subitement, et elle a été brisée; poussez des hurlements sur elle; prenez de la résine pour sa douleur, afin de voir si elle guérira.
Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
9 Nous avons soigné Babylone, et elle n’a pas été guérie; abandonnons-la et allons chacun en notre terre, parce que jusqu’aux cieux est parvenu son jugement, et qu’il s’est élevé jusqu’aux nues.
Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
10 Le Seigneur a fait ressortir notre justice; venez, et racontons dans Sion l’ouvrage du Seigneur, notre Dieu.
“‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
11 Aiguisez les flèches, remplissez les carquois; le Seigneur a suscité l’esprit des rois des Mèdes, et sa pensée est contre Babylone afin de la perdre; parce que c’est la vengeance du Seigneur, la vengeance de son temple.
“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
12 Sur les murs de Babylone levez l’étendard, augmentez la garde, posez des sentinelles, préparez les embuscades, parce que le Seigneur a résolu et il a accompli tout ce qu’il a dit contre les habitants de Babylone.
Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
13 Toi qui habites sur de grandes eaux, riche en trésors, ta fin est venue, c’est le fondement de ta destruction.
Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
14 Le Seigneur des armées a juré par son âme, disant: Je te remplirai d’hommes comme de bruchus, et on entonnera sur toi un chant de joie.
Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
15 C’est lui qui a fait la terre par sa puissance, préparé l’univers par sa sagesse, et par sa prudence étendu les cieux.
“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
16 Lorsqu’il fait entendre sa voix, les eaux s’amassent dans le ciel; c’est lui qui fait monter les nuées des extrémités de la terre; il a converti les éclairs en pluie, et il a tiré les vents de ses trésors.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
17 Tout homme est devenu insensé par sa propre science; tout fondeur a été confondu par son image taillée au ciseau, parce que c’est une chose mensongère qu’il a fondue, et que la vie n’y est pas.
“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
18 Vaines sont leurs œuvres et dignes de risée; au temps de leur visite elles périront.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
19 Il n’en est pas ainsi de la part de Jacob, parce que celui qui a fait toutes ces choses est lui-même son partage; et Israël est le sceptre de son héritage; le Seigneur des armées est son nom.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
20 Tu brises pour moi des instruments de guerre, et je briserai par toi des nations, et je perdrai entièrement par toi des royaumes;
“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
21 Et je briserai par toi le cheval et celui qui le monte; et je briserai par toi le char et celui qui le monte;
ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
22 Et je briserai par toi l’homme et la femme; et je briserai par toi le vieillard et l’enfant; et je briserai par toi le jeune homme et la vierge;
Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
23 Et je briserai par toi le pasteur et son troupeau; et je briserai par toi le laboureur et ses bœufs attachés au joug; et je briserai par toi les chefs et les magistrats.
Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
24 Et je rendrai à Babylone et à tous les habitants de la Chaldée tout leur mal, qu’ils ont fait dans Sion, à vos yeux, dit le Seigneur.
“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 Et voilà que je viens à toi, montagne pernicieuse, dit le Seigneur, qui corromps toute la terre; et j’étendrai ma main sur toi, et je t’arracherai d’entre les rochers, et je ferai de toi une montagne en combustion.
“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
26 Et on ne tirera pas de toi une pierre pour un angle, ni une pierre pour des fondements; mais tu seras éternellement détruite, dit le Seigneur.
Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
27 Levez l’étendard sur la terre; sonnez la trompette parmi des nations; consacrez contre elle des nations; annoncez aux rois d’Ararat, de Menni et d’Ascenez de marcher contre elle; dénombrez contre elle les soldats du Taphsar; amenez contre elle le cheval, comme le bruchus armé d’un aiguillon.
“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
28 Consacrez contre elle des nations, les rois de Médie, ses chefs et tous ses magistrats, et toute la terre soumise à sa puissance.
Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
29 Et la terre sera agitée et troublée; parce que contre Babylone s’éveillera la pensée du Seigneur, afin de rendre la terre de Babylone déserte et inhabitable.
Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
30 Les forts de Babylone ont cessé le combat; ils sont demeurés dans les citadelles: leur force a été dévorée, et ils sont devenus comme des femmes; leurs tabernacles ont été brûlés, leurs verrous ont été brisés.
Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31 Un coureur viendra au-devant d’un coureur, et un messager à la rencontre d’un messager, afin d’annoncer au roi de Babylone que sa ville a été prise d’un bout à l’autre;
Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
32 Et que les gués sont occupés, et que le feu a été mis aux marais, et que les hommes de guerre ont été bouleversés.
Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
33 Parce que voici ce que dit le Seigneur des armées, Dieu d’Israël: La fille de Babylone est comme une aire: c’est le temps de son battage; encore un peu et viendra le temps de sa moisson.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
34 Il m’a mangée; il m’a dévorée, Nabuchodonosor, roi de Babylone, il m’a rendue comme un vase vide, il m’a engloutie comme un dragon, il a rempli son ventre de ce que j’avais de plus délicieux, et il m’a rejetée.
A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
35 L’iniquité commise contre moi et ma chair est retombée sur Babylone, dit l’habitation de Sion, et mon sang sur les habitants de la Chaldée, dit Jérusalem.
Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
36 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi je jugerai ta cause, et j’exercerai ta vengeance: je sécherai sa mer, et je tarirai sa source.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
37 Et Babylone sera un monceau de pierres, une demeure de dragons, un objet de stupeur et de sifflement, parce qu’il n’y a point d’habitant.
Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
38 Tous ensemble ils rugiront comme des lions, ils secoueront leur crinière comme de petits bons.
Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
39 Dans leur chaleur je leur donnerai leurs boissons, et je les enivrerai, afin qu’ils s’assoupissent, et qu’ils dorment un sommeil éternel, et qu’ils ne se relèvent point, dit le Seigneur.
Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
40 Je les conduirai comme des agneaux pour servir de victimes, comme des béliers avec des chevreaux.
“Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
41 Comment a été prise Sésach? et comment a été emportée la ville illustre dans toute la terre? comment Babylone est-elle devenue un objet de stupeur parmi les nations?
“Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
42 La mer est montée sur Babylone; par la multitude de ses efforts elle a été couverte.
Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
43 Ses cités sont devenues un objet de stupeur, une terre inhabitable et déserte, une terre dans laquelle nul n’habite, et où ne passe pas le fils d’un homme.
Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
44 Et je visiterai Bel à Babylone, et je ferai sortir de sa bouche ce qu’il avait absorbé; et les nations n’afflueront plus vers lui, puisque le mur même de Babylone croulera.
Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
45 Sortez d’au milieu d’elle, mon peuple, afin que chacun sauve son âme de la colère du Seigneur;
“Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
46 Et pour que votre cœur ne mollisse pas, et que vous ne craigniez pas le bruit qui s’entendra sur la terre; car dans une année viendra une nouvelle; et après cette année, une autre nouvelle; et l’iniquité sur la terre, et dominateur sur dominateur.
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
47 À cause de cela, voilà que des jours viennent, et je visiterai les images taillées au ciseau de Babylone; et toute sa terre sera couverte de confusion, et tous ses tués tomberont au milieu d’elle.
Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
48 Et les cieux et la terre et tout ce qui est en eux loueront le Seigneur au sujet de Babylone; parce que ses spoliateurs viendront de l’aquilon, dit le Seigneur.
Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
49 Et comme Babylone a fait que des tués sont tombés en Israël, ainsi de Babylone tomberont des tués dans toute la terre.
“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
50 Vous qui avez fui le glaive, venez, ne vous arrêtez point; souvenez-vous de loin du Seigneur, et que Jérusalem monte dans votre cœur.
Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
51 Nous avons été confondus, parce que nous avons entendu l’opprobre; l’ignominie a couvert nos faces, parce que sont venus des étrangers contre le sanctuaire de la maison du Seigneur.
Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
52 À cause de cela, voilà que des jours viennent, dit le Seigneur, et je visiterai ses images taillées au ciseau; et dans toute sa terre mugiront des blessés.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
53 Quand Babylone serait montée jusqu’au ciel, et qu’elle aurait affermi en haut sa force, de moi lui viendront ses dévastateurs, dit le Seigneur.
Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
54 Voix de clameur qui s’élève de Babylone, et grande destruction de la terre des Chaldéens;
“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
55 Parce que le Seigneur a ravagé Babylone, et détruit en elle une grande voix; et leurs flots retentiront comme de grandes eaux; leur voix a eu un retentissement;
Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
56 Parce qu’il est venu sur elle, c’est-à-dire sur Babylone, un spoliateur, et que ses braves ont été pris, et que leur arc a perdu sa force; parce que le Seigneur, puissant vengeur, la rétribuera très certainement.
Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
57 Et j’enivrerai ses princes, et ses sages, et ses chefs, et ses magistrats, et ses braves; et ils dormiront un sommeil éternel; et ils ne se réveilleront pas, dit le roi; le Seigneur des armées est son nom.
Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
58 Voici ce que dit le Seigneur des armées: Ce mur très large de Babylone sera sapé entièrement; et ses portes élevées seront brûlées par le feu; les travaux des peuples seront réduits au néant, et ceux des nations seront livrés au feu et périront entièrement.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
59 Ordre que donna Jérémie, le prophète, à Saraïas, fils de Nérias, lorsqu’il allait avec le roi Sédécias, à Babylone, la quatrième année de son règne; or Saraïas était prince de la prophétie.
Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 Et Jérémie écrivit tout le mal qui devait venir sur Babylone dans son livre, toutes ces paroles qui ont été écrites contre Babylone.
Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 Et Jérémie dit à Saraïas: Lorsque tu seras venu à Babylone, et que tu auras vu, et que tu auras lu toutes ces paroles,
Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 Tu diras: Seigneur, c’est vous qui avez parlé contre ce lieu-ci, afin de le perdre entièrement, pour qu’il n’y ait personne qui l’habite depuis l’homme jusqu’à la bête, et afin qu’il soit une éternelle solitude.
Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 Et lorsque tu auras achevé de lire ce livre, tu y attacheras une pierre et tu le jetteras au milieu de l’Euphrate;
Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 Et tu diras: Ainsi sera submergée Babylone, et elle ne se relèvera pas, à cause de l’affliction que moi j’amène sur elle; et elle sera détruite. Jusqu’ici ce sont les paroles de Jérémie.
Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.