< Jérémie 5 >

1 Parcourez les rues de Jérusalem, et regardez, et considérez, et cherchez dans ses places publiques si vous trouvez un homme faisant la justice et cherchant la vérité, et je lui serai propice.
“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
2 Que s’ils disent aussi: Le Seigneur vit! ils feront même ce serment faussement.
Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
3 Seigneur, vos yeux regardent la bonne foi; vous les avez frappés, et ils n’ont pas éprouvé de douleur; vous les avez brisés, et ils n’ont pas voulu voir la correction; ils ont rendu leurs faces dures au-dessus de la pierre, et ils n’ont pas voulu revenir.
Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
4 Mais moi, j’ai dit: Peut-être sont-ce des pauvres, des insensés, ignorant la voie du Seigneur, et le jugement de leur Dieu.
Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
5 J’irai donc vers les grands, et je leur parlerai; car ils ont connu la voie du Seigneur et le jugement de leur Dieu; et voilà que de plus tous ensemble ont brisé le joug, ils ont rompu les liens.
Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
6 C’est pour cela que le lion de la forêt les a saisis; le loup un soir les a ravagés, le léopard a veillé sur leurs cités; quiconque en sortira sera pris, parce que leurs prévarications se sont multipliées, et que leurs défections se sont fortifiées.
Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
7 En quoi pourrai-je vous être propice? vos fils m’ont abandonné, ils jurent par ceux qui ne sont point des dieux: je les ai rassasiés, et ils ont commis l’adultère, et dans la maison d’une femme de mauvaise vie, ils se livraient à la débauche.
Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
8 Ils sont devenus comme des chevaux ardents, lâchés après des cavales; chacun a henni après la femme de son prochain.
Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
9 Est-ce que je ne visiterai pas ces crimes? dit le Seigneur, et d’une pareille nation mon âme ne se vengera-t-elle pas?
Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
10 Montez sur ses murs, et renversez-les; mais n’achevez pas sa ruine; enlevez ses rejetons, parce qu’ils ne sont point au Seigneur.
“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
11 Car par la prévarication ont prévariqué contre moi la maison d’Israël et la maison de Juda, dit le Seigneur.
Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
12 Ils ont renié le Seigneur, et ils ont dit: Ce n’est pas lui; et il ne viendra pas sur nous de mal; nous ne verrons pas le glaive et la famine.
Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
13 Les prophètes ont parié en l’air, et ils n’ont pas reçu de réponse de Dieu; voici donc ce qui leur arrivera.
Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
14 Voici ce que dit le Seigneur Dieu des armées: Parce que vous avez parlé ainsi, voici que moi, je mets mes paroles dans ta bouche comme un feu, et ce peuple comme du bois, et le feu les dévorera.
Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
15 Voici que moi, ô maison d’Israël, j’amènerai sur vous une nation de loin, dit le Seigneur; une nation forte, une nation ancienne, dont tu ignoreras la langue, et tu ne comprendras pas sa parole.
Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
16 Son carquois est comme un sépulcre ouvert; tous sont vaillants.
Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
17 Et elle mangera tes moissons et ton pain; elle dévorera tes fils et tes filles; elle mangera tes troupeaux de menu et de gros bétail; elle mangera tes vignes et tes figuiers; et elle détruira par le glaive tes villes fortifiées, dans lesquelles tu as confiance.
Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
18 Cependant en ces jours-là, dit le Seigneur, je ne consommerai pas votre ruine
“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
19 Que si vous dites: Pourquoi le Seigneur notre Dieu nous a-t-il fait tous ces maux? tu leur diras: Comme vous m’avez abandonné, et vous avez servi un dieu étranger dans votre terre, ainsi vous servirez des étrangers dans une terre qui n’est pas la vôtre.
Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
20 Annoncez ceci à la maison de Jacob, faites-le entendre dans Juda, disant:
“Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
21 Ecoute, peuple insensé, qui n’as point de cœur; vous qui ayant des yeux, ne voyez point; des oreilles, et n’entendez point.
Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
22 Ne me craindrez-vous donc pas, dit le Seigneur, et devant ma face ne serez-vous pas saisis de douleur? moi qui ai donné le sable pour borne à la mer, précepte éternel, qu’elle ne transgressera pas; ses flots s’agiteront et ils ne prévaudront pas; ils se soulèveront, et ils ne le dépasseront pas;
Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
23 Mais en ce peuple s’est formé un cœur incrédule et rebelle; ils se sont retirés, et s’en sont allés.
Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
24 Et ils n’ont pas dit en leur cœur: Craignons le Seigneur notre Dieu, qui nous donne la pluie de la première et de l’arrière-saison en son temps, et qui nous conserve tous les ans une abondante moisson.
Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
25 Vos iniquités ont détourné cela, et vos péchés ont écarté de vous le bien.
Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
26 Parce qu’il s’est trouvé parmi mon peuple des impies qui dressent des pièges comme des oiseleurs, qui posent des lacs et des rets pour prendre les hommes.
“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
27 Comme un trébuchet rempli d’oiseaux, ainsi leurs maisons seront pleines de tromperie; c’est pour cela qu’ils sont devenus grands et se sont enrichis.
Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
28 Ils ont épaissi et se sont engraissés, et ils ont laissé de côté mes paroles très méchamment. Ils n’ont pas jugé la cause de la veuve, ils n’ont pas dirigé la cause de l’orphelin, et ils n’ont pas rendu justice aux pauvres.
Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
29 Est-ce que je ne visiterai pas ces crimes, dit le Seigneur? ou mon âme ne se vengera-t-elle pas d’une nation semblable?
Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
30 La stupeur et des merveilles ont eu lieu sur la terre;
“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
31 Les prophètes ont prophétisé le mensonge, et les prêtres ont battu des mains; et mon peuple a aimé de pareilles choses; qu’arrivera-t-il donc à son dernier moment?
Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?

< Jérémie 5 >