< Jérémie 42 >

1 Et s’approchèrent tous les princes des hommes de guerre, Johanan, fils de Carée, et Jézonias, fils d’Osaïas, et tout le reste du peuple, depuis le petit jusqu’au grand;
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 Et ils dirent à Jérémie, le prophète: Que notre prière tombe en ta présence; et prie pour nous le Seigneur ton Dieu pour tous ces restes, parce que nous avons été laissés un petit nombre d’un bien plus grand, comme les yeux nous voient;
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 Et que le Seigneur ton Dieu nous annonce la voie par laquelle nous devons marcher, et la parole que nous devons accomplir.
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 Or Jérémie, le prophète, leur dit: J’ai entendu; voici que moi je prie le Seigneur votre Dieu, selon vos paroles; toute parole quelconque qu’il me répondra, je vous la ferai connaître, et je ne vous cacherai rien.
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 Et ceux-ci dirent à Jérémie: Que le Seigneur soit entre nous témoin de la vérité et de notre bonne foi, si nous n’agissons pas conformément à toute parole avec laquelle le Seigneur ton Dieu t’aura envoyé vers nous.
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
6 Soit bonne, soit défavorable, nous obéirons à la voix du Seigneur notre Dieu, vers qui nous t’envoyons, afin que bien nous soit, lorsque nous aurons écouté la voix du Seigneur notre Dieu.
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 Or, lorsque dix jours eurent été accomplis, la parole du Seigneur fut adressée à Jérémie.
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 Et il appela Johanan, fils de Carée, tous les princes des Sommes de guerre qui étaient avec lui et tout le peuple, depuis le plus petit jusqu’au grand.
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 Et il leur dit: Voici ce que di t le Seigneur, Dieu d’Israël, vers qui vous m’avez envoyé afin de répandre vos prières en sa présence:
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 Si vous demeurez en repos dans cette terre, je vous édifierai, et je ne détruirai pas; je planterai, et je n’arracherai pas; car je suis apaisé par le mal que je vous ai fait.
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 Ne craignez pas la face du roi de Babylone, que tremblants d’effroi vous redoutez; ne le craignez pas, dit le Seigneur, parce que moi je suis avec vous, afin de vous sauver, et de vous tirer de sa main.
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 Et je vous donnerai mes miséricordes et j’aurai pitié de vous, et je vous ferai habiter dans votre terre.
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 Mais si vous dites: Nous n’habiterons pas dans cette terre, et nous n’écouterons pas la voix du Seigneur notre Dieu,
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
14 Disant: En aucune manière; mais nous irons dans la terre d’Egypte, où nous ne verrons pas la guerre, où nous n’entendrons pas le bruit de la trompette, où nous ne souffrirons pas la faim, et nous y habiterons:
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
15 À cause de cela, écoutez maintenant la parole du Seigneur, restes de Juda. Voici ce que dit le Seigneur des armées, Dieu d’Israël: Si vous tournez votre face afin d’entrer en Egypte, et que vous y entriez pour y habiter,
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 Le glaive, que vous redoutez, vous atteindra là, dans la terre d’Egypte; et la famine, au sujet de laquelle vous êtes inquiets, s’attachera à vous en Egypte, et vous y mourrez.
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 Et tous les hommes qui ont tourné leurs faces afin d’entrer en Egypte et d’y habiter seront détruits par le glaive, et par la famine, et par la peste; et nul d’entre eux ne demeurera, et n’échappera à la face du mal que moi j’amènerai sur eux.
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 Parce que voici ce que dit le Seigneur des armées, Dieu d’Israël: Comme ma colère et ma fureur se sont allumées contre les habitants de Jérusalem, ainsi s’allumera contre vous mon indignation, lorsque vous serez entrés en Egypte; et vous serez en exécration, en stupeur, en malédiction et en opprobre; et jamais plus vous ne verrez ce lieu.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 Voici la parole du Seigneur sur vous, restes de Juda: N’entrez pas en Egypte; sachant, vous saurez que je vous ai protesté aujourd’hui,
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 Que vous avez trompé vos âmes; car c’est vous qui m’avez envoyé vers le Seigneur notre Dieu, disant: Prie pour nous le Seigneur notre Dieu; et tout ce que t’aura dit le Seigneur notre Dieu, annonce-nous-le, et nous le ferons.
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 Et je vous l’ai annoncé aujourd’hui, et vous n’avez pas écouté la voix du Seigneur votre Dieu, dans toutes les choses pour lesquelles il m’a envoyé vers vous.
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 Maintenant donc, sachant, vous saurez que c’est par le glaive, et par la famine, et par la peste que vous mourrez dans le lieu dans lequel vous avez voulu entrer afin d’y habiter.
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

< Jérémie 42 >