< Jérémie 22 >
1 Voici ce que dit le Seigneur: Descends dans la maison du roi de Juda, et tu prononceras là cette parole,
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
2 Et tu diras: Ecoute la parole du Seigneur, roi de Juda, toi qui es assis sur le trône de David; toi, et tes serviteurs, et ton peuple, qui entrez par ces portes.
‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
3 Voici ce que dit le Seigneur: Rendez le jugement et la justice; délivrez celui qui est opprimé par la violence de la main de l’oppresseur; ne contristez pas l’étranger, l’orphelin, et la veuve, et ne les opprimez pas injustement, et le sang innocent, ne le répandez pas dans ce lieu.
Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
4 Si observant vous observez ces paroles, des rois de la race de David entreront par les portes de cette maison; ils seront assis sur son trône, et montés sur des chars et sur des chevaux, leurs serviteurs et leur peuple.
Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
5 Que si vous n’écoutez point ces paroles, j’ai juré par moi-même, dit le Seigneur, que cette maison deviendra une solitude.
Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
6 Parce que voici ce que dit le Seigneur sur la maison du roi de Juda: Tu es pour moi, Galaad, la tête du Liban; néanmoins je te rendrai toi, une solitude, et tes villes inhabitables.
Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
7 Et je consacrerai contre toi un homme qui tuera, et ses armes; et ils abattront tes cèdres choisis, et ils les jetteront dans le feu.
Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
8 Et des nations nombreuses passeront par cette cité, et chacun dira à son voisin: Pourquoi le Seigneur a-t-il fait ainsi à cette cité considérable?
“Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
9 Et on répondra: Parce qu’ils ont abandonné l’alliance du Seigneur leur Dieu, et qu’ils ont adoré des dieux étrangers, et qu’ils les ont servis.
Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
10 Ne pleurez pas un mort, ne faites pas de deuil pour lui par votre pleur; désolez-vous au sujet de celui qui sort, parce qu’il ne reviendra plus, et qu’il ne verra plus la terre de sa naissance.
Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
11 Parce que voici ce que dit le Seigneur, contre Sellum, fils de Josias, et roi de Juda, qui a régné pour Josias, son père, et qui est sorti de ce lieu: Il ne reviendra plus ici;
Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
12 Mais dans le lieu où je l’ai transporté, là il mourra, et il ne verra plus cette terre.
Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
13 Malheur à celui qui bâtit sa maison dans l’injustice, et ses cénacles dans l’iniquité; il opprimera son ami sans sujet, et il ne lui payera pas son salaire;
“Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
14 Qui dit: Je me bâtirai une maison vaste et des cénacles spacieux; qui s’ouvre des fenêtres, fait des lambris de cèdre, et il les peint avec de la terre de Sinope.
Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
15 Est-ce que tu régneras, parce que tu te compares au cèdre? ton père n’a-t-il pas mangé et bu, et rendu le jugement et la justice, alors que tout allait bien pour lui?
“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
16 Et il a jugé la cause du pauvre et de l’indigent pour son propre bonheur; n’est-ce pas parce qu’il m’a connu, dit le Seigneur?
Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
17 Mais tes yeux et ton cœur sont portés seulement à l’avarice, à répandre le sang innocent, à la calomnie, et à courir après les mauvaises œuvres.
“Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
18 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur à Joakim, fils de Josias et roi de Juda: On ne se désolera pas à son sujet, en disant: Malheur, frère! Malheur, sœur! on ne fera pas retentir pour lui: Malheur, maître! Malheur, illustre!
Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
19 De la sépulture d’un âne il sera enseveli; pourri, il sera jeté hors des portes de Jérusalem.
Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
20 Monte sur le Liban, et crie; et en Basan élève ta voix, et crie aux passants qu’ils ont été brisés, tous ceux qui t’aimaient.
“Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
21 Je t’ai parlé dans le temps de ton abondance, et tu as dit: Je n’écouterai pas; ça a été ta voie dès ta jeunesse, que de ne pas écouter ma parole.
Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
22 Le vent paîtra tous tes pasteurs, et tes amants iront en captivité; et alors tu seras confondue, et tu rougiras de toute ta malice.
Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
23 Toi qui es assise sur le Liban, et qui as fait ton nid dans les cèdres, comment as-tu gémi profondément, lorsque te sont venues des douleurs, comme celles d’une femme en travail?
Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
24 Je vis, moi, dit le Seigneur; quand Jéchonias, fils de Joakim, roi de Juda, serait un anneau à ma main droite, je l’en arracherai.
“Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
25 Et je te livrerai à la main de ceux qui cherchent ton âme, et à la main de ceux dont tu redoutes la face, et à la main de Nabuchodonosor, roi de Babylone, et à la main des Chaldéens.
Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
26 Je t’enverrai, toi et ta mère qui t’a enfantée, dans une terre étrangère dans laquelle vous n’êtes pas nés, et vous y mourrez.
Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
27 Et quant à la terre vers laquelle eux-mêmes élèvent leur âme pour y retourner, ils n’y retourneront pas.
Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
28 N’est-ce pas un vase d’argile, et un vase brisé, que cet homme, Jéchonias? n’est-ce pas un vase sans aucun agrément? pourquoi ont-ils été rejetés, lui et sa race, et jetés dans une terre qu’ils ne connaissaient pas?
Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
29 Terre, terre, terre, écoute la parole du Seigneur.
Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
30 Voici ce que dit le Seigneur: Inscris cet homme comme stérile, comme un homme qui durant ses jours ne prospérera pas, car il n’y aura pas d’homme de sa race qui s’assiéra sur le trône de David, et qui aura à; l’avenir le pouvoir dans Juda.
Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”