< Jérémie 20 >
1 Et Phassur, le prêtre, fils d’Emmer, qui avait été établi prince dans la maison du Seigneur, entendit Jérémie prophétisant ces choses.
Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 Et Phassur frappa Jérémie, le prophète, et le jeta dans la prison qui était à la porte haute de Benjamin, dans la maison du Seigneur.
Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 Et lorsque le jour eut paru le lendemain, Phassur fit sortir Jérémie de prison, et Jérémie lui dit: Le Seigneur n’appelle plus ton nom, Phassur, mais l’épouvante de toutes parts.
Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 Parce que voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi, je te livrerai à l’épouvante, toi et tous tes amis; et ils tomberont sous le glaive de leurs ennemis, et tes yeux le verront; et tout Juda, je le livrerai à la main du roi de Babylone; et il les transportera à Babylone, et il les frappera par le glaive.
Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 Et je livrerai toutes les richesses de cette cité; et tout son travail, et tout ce qu’elle a de précieux, et tous les trésors des rois de Juda, je les livrerai à la main de leurs ennemis; et ceux-ci les arracheront, les enlèveront, et les conduiront à Babylone.
Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 Mais toi, Phassur, et tous les habitants de ta maison, vous irez en captivité; et tu viendras à Babylone, et là tu mourras, et là tu seras enseveli, toi et tous tes amis à qui tu as prophétisé le mensonge.
Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
7 Vous m’avez séduit. Seigneur, et j’ai été séduit; vous avez été plus fort, et vous avez prévalu; je suis devenu un objet de dérision durant tout le jour; et tous me raillent.
Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
8 Parce que déjà depuis longtemps je parle, criant contre l’iniquité, et annonçant à grand bruit une désolation, et la parole du Seigneur est devenue pour moi un sujet d’opprobre et de dérision durant tout le jour.
Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
9 Et j’ai dit: Je ne ferai pas mention de lui, et je ne parlerai plus en son nom; et alors il s’est allumé dans mon cœur comme un feu ardent, et renfermé dans mes os; et j’ai défailli, ne pouvant le soutenir.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
10 Car j’ai entendu les outrages d’un grand nombre et la terreur tout autour de moi. Poursuivez-le, et nous le poursuivrons; j’ai entendu aussi de tous les hommes qui vivaient en paix avec moi, et qui se tenaient à mes côtés: Si en quelque manière il était trompé, et que nous prévalions contre lui, et que nous tirions vengeance de lui.
Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
11 Mais le Seigneur est avec moi comme un guerrier vaillant; c’est pour cela que ceux qui me persécutent tomberont et seront sans force; ils seront confondus grandement, parce qu’ils n’ont pas compris un opprobre éternel qui ne s’effacera jamais.
Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 Et vous. Seigneur des armées, vous qui éprouvez le juste, et qui voyez les reins et les cœurs; que je voie, je vous prie, la vengeance que vous tirerez d’eux, car à vous j’ai révélé ma cause.
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
13 Chantez le Seigneur, louez le Seigneur, parce qu’il a délivré l’âme d’un pauvre de la main des méchants.
Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
14 Maudit le jour auquel je suis né! que le jour auquel m’a enfanté ma mère ne soit pas béni!
Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 Maudit l’homme qui Va annoncé à mon père, disant: Un enfant mâle t’est né, et qui l’a comme rempli de joie!
Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 Que cet homme soit comme sont les cités qu’a détruites le Seigneur, sans qu’il s’en soit repenti; qu’il entende des clameurs le matin, et des hurlements à l’heure de midi;
Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
17 Lui qui ne m’a pas tué avant ma naissance; en sorte que ma mère devînt mon sépulcre, et que sa grossesse fût éternelle,
Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Pourquoi suis-je sorti du sein de ma mère pour voir le travail et la douleur, et pour que mes jours fussent consumés dans la confusion?
Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?