< Jérémie 16 >

1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
2 Tu ne prendras point de femme, et tu n’auras point de fils et de filles en ce lieu.
“Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
3 Parce que voici ce que dit le Seigneur sur les fils et les filles qui sont enfantés en ce lieu, et sur les mères qui les ont enfantés, et sur leurs pères de la souche desquels ils sont nés en cette terre:
pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
4 De différentes morts de maladies ils mourront; ils ne seront pas pleures et ils ne seront pas ensevelis; comme un fumier, ils seront sur la face de la terre; par le glaive et par la famine ils seront consumés, et leur cadavre sera en pâture aux volatiles du ciel et aux bêtes de la terre.
adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 Car voici ce que dit le Seigneur: N’entre point dans une maison de festin; et ne va pas pour pleurer, et ne les console point; parce que j’ai retiré ma paix à ce peuple, dit le Seigneur, ma miséricorde et mes bontés.
Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
6 Et ils mourront, grands et petits, sur cette terre, et ils ne seront pas ensevelis, ni pleures, et on ne se fera pas d’incision, et on ne se rasera pas la tête pour eux.
Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
7 Et on ne rompra pas parmi eux de pain pour consoler celui qui pleure un mort, et on ne leur donnera pas le calice à boire pour le consoler de la perte de son père et de sa mère.
Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 Et tu n’entreras pas dans une maison d’un festin, afin de l’asseoir et de manger et de boire;
“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
9 Parce que voici ce que dit le Seigneur des armées, Dieu d’Israël: Voilà que moi j’ôterai de ce lieu, à vos yeux et en vos jours, la voix de la joie et la voix de l’allégresse, la voix de l’époux et la voix de l’épouse.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 Et lorsque tu annonceras à ce peuple toutes ces paroles, et qu’ils le diront: Pourquoi le Seigneur a-t-il prononcé sur nous tous ces grands maux? quelle est notre iniquité? et quel péché avons-nous commis contre le Seigneur notre Dieu?
“Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
11 Tu leur diras: C’est parce que vos pères m’ont abandonné, dit le Seigneur, qu’ils ont couru après des dieux étrangers, qu’ils les ont servis, qu’ils les ont adorés; et qu’ils m’ont abandonné, et qu’ils n’ont point gardé ma loi.
Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
12 Mais vous-même, vous avez fait pis que vos pères; car voilà que chacun marche à la suite de la dépravation de son cœur mauvais, afin de ne pas m’écouter.
Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
13 Et je vous jetterai de cette terre dans une terre que vous ignorez comme vos pères; et vous servirez là des dieux étrangers, le jour et la nuit, qui ne vous donneront pas de repos.
Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
14 À cause de cela, voilà que des jours viennent, dit le Seigneur, et l’on ne dira plus: Le Seigneur vit! qui a retiré les fils d’Israël de la terre d’Egypte,
Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
15 Mais: Vive le Seigneur qui a tiré les fils d’Israël de la terre de l’aquilon, et de toutes les terres où je les ai jetés; et je les ramènerai dans leur terre que j’ai donnée à leurs pères.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Voilà que moi j’enverrai des pêcheurs nombreux, dit le Seigneur, et ils pécheront; et après cela je leur enverrai beaucoup de chasseurs, qui leur feront la chasse sur toute montagne, sur toute colline et dans toutes les cavernes des rochers;
Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
17 Parce que mes yeux sont sur toutes les voies; elles ne sont pas cachées à ma face, et leur iniquité n’est pas voilée à mes yeux.
Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
18 Et je leur rendrai d’abord au double leurs iniquités et leurs péchés, parce qu’ils ont souillé ma terre de morts pour leurs idoles, et que de leurs abominations ils ont rempli mon héritage.
Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 Seigneur, mon courage, ma force et mon refuge au jour de la tribulation, vers vous viendront des nations des extrémités de la terre, et elles diront: Il est vrai que nos pères ont possédé le mensonge et la vanité, qui ne leur a pas été utile.
Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Est-ce qu’un homme se fera des dieux, lesquels même ne sont pas des dieux?
Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 C’est pourquoi voici que moi je leur montrerai cette fois, je leur montrerai ma main et ma force, et ils sauront que mon nom est le Seigneur.
“Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.

< Jérémie 16 >