< Isaïe 8 >

1 Et le Seigneur me dit: Prends un grand livre et écris-y en style d’homme: Enlève promptement les dépouilles, prends vite le butin.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Et je pris des témoins fidèles, Urie le prêtre et Zacharie fils de Barachie;
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 Et je m’approchai de la prophétesse, et elle conçut et enfanta un fils. Et le Seigneur me dit: Appelle son nom: Hâte-toi d’enlever les dépouilles: Empresse-toi de prendre le butin.
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 Parce qu’avant que l’enfant sache nommer son père et sa mère, la puissance de Damas sera enlevée, ainsi que les dépouilles de Samarie devant le roi des Assyriens.
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 Et le Seigneur me parla encore, disant:
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 Parce que ce peuple a rejeté les eaux de Siloë, qui coulent en silence, et qu’il a pris plutôt Rasin, et le fils de Romélie;
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 À cause de cela, voici que le Seigneur fera venir sur eux les eaux violentes et abondantes du fleuve, le roi des Assyriens et toute sa gloire; et il s’élèvera au-dessus de toutes ses rives, et il coulera par dessus tous ses bords;
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 Et il ira à travers Juda, l’inondant et le traversant jusqu’au cou. Et il étendra ses ailes, remplissant l’étendue de ta terre, ô Emmanuel.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Rassemblez-vous, peuples, et soyez vaincus; et écoutez, vous toutes, terres lointaines, fortifiez-vous et soyez vaincues, ceignez-vous pour le combat, soyez vaincues;
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Formez des desseins, et ils seront dissipés; dites une parole, et elle ne sera pas exécutée, parce qu’avec nous est Dieu.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 Car voici ce que m’a dit le Seigneur, quand, me tenant par une main puissante, il m’a instruit, afin que je n’allasse point dans la voie de ce peuple disant:
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 Ne dites pas: Conjuration; car tout ce que dit ce peuple est conjuration; ne craignez pas ce qu’il craint et ne vous effrayez point.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Sanctifiez le Seigneur des armées; qu’il soit lui-même votre frayeur, et lui-même votre terreur.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 Et il vous sera en sanctification. Mais il sera en pierre d’achoppement et en pierre de scandale aux deux maisons d’Israël; en lacs et en ruine aux habitants de Jérusalem.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Et le plus grand nombre d’entre eux se heurteront, et tomberont, et seront brisés, et ils s’embarrasseront dans des filets et ils seront pris.
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Lie le témoignage, scelle la loi pour mes disciples,
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 Et j’attendrai le Seigneur qui cache sa face à la maison de Jacob, et je l’attendrai.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Me voici, moi et les enfants que le Seigneur m’a donnés pour être un signe et un présage dans Israël, par l’ordre du Seigneur des armées qui habite sur la montagne de Sion.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 Et lorsqu’on vous dira: Consultez les pythoniens et les devins qui bruissent dans leurs enchantements, répondez: Est-ce qu’un peuple ne consultera pas son Dieu? Consulte-t-on les morts pour les vivants?
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Recourez plutôt à la loi, et au témoignage. Que s’ils ne parlent pas conformément à cette parole, la lumière du matin ne sera pas pour eux.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 Et ils passeront au milieu d’elle, et ils tomberont, et ils souffriront la faim; et lorsqu’ils souffriront la faim, ils se mettront en colère, et ils maudiront leur roi et leur Dieu, et ils regarderont en haut.
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 Et ils porteront leurs regards vers la terre, et voilà la tribulation et les ténèbres, l’abattement et l’angoisse, une nuit sombre qui les poursuivra, et ils ne pourront échapper à leur angoisse.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Isaïe 8 >