< Isaïe 66 >

1 Voici ce que dit le Seigneur: Le ciel est mon trône, et la terre l’escabeau de mes pieds; quelle est cette maison que vous me bâtirez? et quel est ce lieu de mon repos?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Toutes ces choses, c’est ma main qui les a faites, et elles ont été faites toutes, dit le Seigneur; mais vers qui porterai-je mes regards, sinon vers le pauvre et celui qui a l’esprit contrit, et qui tremble à mes paroles?
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Celui qui immole un bœuf est comme celui qui tuerait un homme; celui qui sacrifie une bête de menu bétail est comme celui qui ôterait la cervelle à un chien; celui qui fait une oblation est comme celui qui offrirait du sang de porc; celui qui se souvient de brûler de l’encens est comme celui qui adorerait une idole. Ils ont choisi toutes ces choses dans leurs voies; et dans leurs abominations leur âme s’est délectée.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 D’où moi aussi je choisirai pour eux les railleries; et ce qu’ils craignaient, je l’amènerai sur eux; parce que j’ai appelé, et il n’y avait personne qui répondît; j’ai parlé, et ils n’ont pas écouté; ils ont fait le mal à mes yeux; et ce que je n’ai pas voulu, ils font choisi.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Ecoutez la parole du Seigneur, vous qui tremblez à sa parole; vos frères qui vous haïssent, et qui vous rejettent à cause de mon nom, ont dit: Que la gloire du Seigneur se montre; et nous le reconnaîtrons à votre joie; mais eux, ils seront confondus.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Une voix du peuple sort de la cité, une voix s’élève du temple, c’est la voix du Seigneur qui rendra rétribution à ses ennemis.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Avant qu’elle fût en travail, elle a enfanté; avant que vînt le temps de son enfantement, elle a enfanté un enfant mâle.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Qui a jamais ouï une telle chose? et qui a vu rien de semblable à cela? est-ce que la terre engendrera en un seul jour? ou toute une nation sera enfantée en même temps, parce que Sion a été en travail et qu’elle a enfanté ses fils?
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Est-ce que moi, qui fais enfanter les autres, je n’enfanterai pas moi-même, dit le Seigneur? est-ce que moi, qui donne la génération aux autres, je demeurerai stérile, dit le Seigneur ton Dieu?
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Livrez-vous à la joie avec Jérusalem, exultez en elle, vous tous qui l’aimez; réjouissez-vous avec elle, vous tous qui pleurez sur elle;
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Afin que vous suciez, et que vous soyez rassasiés à la mamelle de sa consolation; afin que vous tétiez et que vous regorgiez des délices de sa gloire infinie.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Parce que voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi j’amènerai sur elle comme un fleuve de paix, et comme un torrent qui se déborde, la gloire des nations, laquelle vous sucerez; à la mamelle vous serez portés, et sur les genoux on vous caressera.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 De même qu’une mère qui caresse quelqu’un de ses enfants, de même moi je vous consolerai; et c’est dans Jérusalem que vous serez consolés.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Vous verrez et votre cœur se réjouira, et vos os comme l’herbe germeront; et l’on connaîtra que la main du Seigneur est pour ses serviteurs, et il sera indigné contre ses ennemis.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Parce que voilà que le Seigneur viendra dans le feu, et ses quadriges seront comme la tempête, pour répandre dans son indignation sa fureur, et ses reproches dans une flamme de feu;
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Parce que le Seigneur jugera dans le feu et avec son glaive toute chair; et ils seront bien nombreux, ceux qui seront tués par le Seigneur.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Ceux qui se sanctifiaient et croyaient se rendre purs dans leurs jardins, derrière la porte, en dedans; qui mangeaient de la chair de porc, et des abominations, et des rats seront consumés tous ensemble, dit le Seigneur.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Mais moi je viens afin de recueillir leurs œuvres et leurs pensées, et de les rassembler avec toutes les nations et les langues; ils viendront et ils verront ma gloire.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 Je poserai un étendard parmi eux, et j’enverrai ceux d’entre eux qui auront été sauvés, vers les nations, vers la mer, en Afrique et en Lydie, qui tend la flèche; dans l’Italie et la Grèce, dans les îles au loin, vers ceux qui n’ont pas entendu parler de moi, et n’ont pas vu ma gloire. Et ils annonceront ma gloire aux nations,
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Et ils amèneront tous vos frères de toutes les nations comme un don au Seigneur, sur des chevaux, sur des quadriges et sur des litières, sur des mulets et sur des chariots, à ma montagne sainte, Jérusalem, dit le Seigneur, comme si les fils d’Israël portaient un présent dans un vase pur dans la maison du Seigneur.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Et j’en prendrai d’entre eux pour prêtres et lévites, dit le Seigneur.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Parce que comme les cieux nouveaux et la terre nouvelle, que je fais subsister devant moi, dit le Seigneur, ainsi subsisteront votre race et votre nom.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Et il arrivera que de mois en mois, et de sabbat en sabbat, toute chair viendra afin d’adorer devant ma face, dit le Seigneur.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Et ils sortiront, et ils verront les cadavres des hommes qui ont prévariqué contre moi; leur ver ne mourra pas, et leur feu ne s’éteindra pas, ils seront un objet de regard jusqu’à satiété pour toute chair.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Isaïe 66 >