< Isaïe 55 >
1 Vous tous qui avez soif, venez vers les eaux; et vous qui n’avez pas d’argent, hâtez-vous, achetez et mangez; venez, achetez sans argent et sans aucun échange du vin et du lait.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Pourquoi dépensez-vous de l’argent à ce qui n’est pas du pain, et votre travail à ce qui ne peut vous rassasier? Ecoutez-moi avec une grande attention, et mangez une bonne nourriture, et votre âme se délectera en s’en engraissant.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Inclinez votre oreille, et venez à moi; écoutez, et votre âme vivra, et je ferai avec vous un pacte éternel qui montrera véritables les miséricordes promises à David.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Voilà que je l’ai donné pour témoin aux peuples, pour chef et pour maître aux nations.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Voilà que tu appelleras une nation que tu ne connaissais pas; et des nations qui ne t’ont pas connu vers toi accourront, à cause du Seigneur ton Dieu, et du saint d’Israël qui t’a glorifié.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Cherchez le Seigneur, tandis qu’on peut le trouver, invoquez-le tandis qu’il est proche.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Que l’impie abandonne sa voie, et l’homme inique ses pensées, et qu’il retourne au Seigneur, et il aura pitié de lui; et à notre Dieu, parce qu’il pardonne beaucoup.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 Car mes pensées ne sont pas vos pensées, ni vos voies mes voies, dit le Seigneur.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 Parce qu’autant les cieux sont élevés au-dessus de la terre, autant sont élevées mes voies au-dessus de vos voies, et mes pensées au-dessus de vos pensées.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Et de même que la pluie et la neige descendent du ciel et n’y retournent plus, mais qu’elles abreuvent la terre, la pénètrent, la font germer, et qu’elle donnent la semence au semeur, et le pain à celui qui le mange;
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ainsi sera ma parole qui sortira de ma bouche; elle ne reviendra pas à moi sans effet; mais elle fera tout ce que j’ai voulu, et elle réussira dans toutes les choses pour lesquelles je l’aurai envoyée.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Parce que dans la joie vous sortirez, et dans la paix vous serez ramenés; les montagnes et les collines chanteront devant vous des louanges, et tous les arbres du pays battront des mains.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Au lieu du nard sauvage s’élèvera le sapin, et au lieu de l’ortie croîtra le myrte; et le nom du Seigneur deviendra un signe éternel, qui ne sera pas enlevé.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”