< Isaïe 50 >
1 Voici ce que dit le Seigneur: Quel est cet acte de répudiation donné à votre mère, par lequel je l’ai renvoyée? ou quel est mon créancier à qui je vous ai vendus? voilà que pour vos iniquités vous avez été vendus, et pour vos crimes, j’ai renvoyé votre mère.
Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Parce que je suis venu, et il n’y avait pas un homme: j’ai appelé, et il n’y avait personne qui entendit; est-ce que ma main s’est raccourcie, et est devenue toute petite, en sorte que je ne puisse vous racheter? ou bien n’y a-t-il pas en moi de force pour délivrer? Voici qu’à ma réprimande je ferai un désert de la mer; je mettrai les fleuves à sec; les poissons pourriront faute d’eau, et périront de soif.
Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
3 J’envelopperai les cieux de ténèbres, et je leur mettrai un sac pour couverture.
Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 Le Seigneur m’a donné une langue savante, afin que je sache soutenir par la parole celui qui est abattu; il prépare dès le matin, dès le matin il prépare mon oreille, afin que je l’écoute comme un maître.
Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 Le Seigneur Dieu m’a ouvert l’oreille, et moi je ne le contredis pas; je ne me suis pas retiré en arrière.
Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 J’ai abandonné mon corps à ceux qui me frappaient, mes joues à ceux qui arrachaient ma barbe; je n’ai pas détourné ma face à ceux qui me réprimandaient et qui crachaient sur moi.
Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 Le Seigneur Dieu est mon aide; c’est pour cela que je n’ai pas été confondu; c’est pour cela que j’ai présenté ma face comme une pierre très dure, et je sais que je ne serai pas confondu.
Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 Près de moi est celui qui me justifie, qui me contredira? présentons-nous ensemble, qui est mon adversaire? qu’il s’approche de moi.
Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
9 Voici que le Seigneur Dieu est mon aide, qui est-ce qui me condamnera? voici que tous seront mis en pièces comme un vêtement, la teigne les rongera.
Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
10 Qui de vous craint le Seigneur, écoute la voix de son serviteur? que celui qui a marché dans les ténèbres et en qui n’est pas la lumière, espère au nom du Seigneur, et qu’il s’appuie sur son Dieu.
Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
11 Voici que vous tous qui avez allumé un feu, qui êtes environnés de flammes, marchez à la lumière de votre feu. et dans les flammes que vous avez allumées; c’est par ma main que cela vous a été fait, vous dormirez au milieu des douleurs.
Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.