< Isaïe 4 >
1 Et sept femmes prendront un seul homme en ce jour-là, disant: Nous mangerons notre pain, et nous serons couvertes de nos vêtements; seulement que votre nom soit invoqué sur nous, enlevez notre opprobre.
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 En ce jour-là, le germe du Seigneur sera dans la magnificence et la gloire; et le fruit de la terre s’élèvera, et l’exultation sera pour ceux d’Israël qui auront été sauvés.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 Et voici ce qui arrivera: Quiconque aura été laissé dans Sion, et sera resté dans Jérusalem, sera appelé saint; quiconque aura été écrit comme vivant dans Jérusalem;
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 Quand le Seigneur aura purifié les souillures des filles de Sion, et qu’il aura lavé le sang de Jérusalem, lequel est au milieu d’elle, par un esprit de justice et par un esprit d’ardeur.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 Et le Seigneur créera sur toute la montagne de Sion, et sur le lieu où il aura été invoqué, un nuage et une fumée pendant le jour, et l’éclat d’un feu flamboyant pendant la nuit; car sur toute gloire sera sa protection.
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 Et il y aura un tabernacle pour ombrage dans le jour contre la chaleur, et pour mettre en sûreté et à couvert de la tempête et de la pluie.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.