< Isaïe 39 >

1 En ce temps-là Mérodach Baladan, fils de Baladan, roi de Babylone, envoya des livres et des présents à Ezéchias; car il avait appris qu’il avait été malade, et qu’il était guéri.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Ezéchias se réjouit à l’arrivée des députés, et leur montra le lieu où étaient conservés les aromates, l’argent et l’or, les parfums, et les essences les meilleures, tous les endroits où étaient les meubles, et tout ce qui se trouva dans ses trésors. Il n’y eut chose que ne leur montrât Ezéchias de ce qui était en sa maison et toute sa puissance.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Or Isaïe, le prophète, entra auprès du roi Ezéchias, et lui dit: Qu’ont dit ces hommes, et d’où sont-ils venus vers vous? Et dit Ezéchias: C’est d’une terre lointaine qu’ils sont venus vers moi, de Babylone.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Et le prophète dit: Qu’ont-ils vu dans votre maison? Et Ezéchias dit: Tout ce qu’il y a dans ma maison, ils l’ont vu; il n’est chose que je ne leur aie montrée dans mes trésors.
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Et Isaïe dit à Ezéchias: Ecoute la parole du Seigneur des armées.
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Voilà que des jours viendront, et que sera emporté à Babylone tout ce qui est dans ta maison, et ce qu’ont amassé tes pères jusqu’à ce pour; rien ne sera laissé, dit le Seigneur;
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Et on prendra de tes fils qui sortiront de toi, et que tu auras engendrés, et ils seront eunuques dans le palais du roi de Babylone.
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Et Ezéchias dit à Isaïe: Bonne est la parole du Seigneur que tu as dite. Puis il dit: Qu’il y ait paix seulement et vérité durant mes jours.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

< Isaïe 39 >