< Isaïe 26 >
1 En ce jour-là sera chanté ce cantique dans la terre de Juda: Notre ville forte est Sion; le sauveur sera mis comme mur et avant-mur.
Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
2 Ouvrez les portes, et qu’il y entre une nation juste et observant la vérité.
Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
3 L’ancienne erreur a disparu; vous nous conserverez la paix, la paix, parce que nous avons espéré en vous.
Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
4 Vous avez espéré dans le Seigneur durant les siècles éternels, dans le Seigneur Dieu puissant à jamais.
Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
5 Parce qu’il abaissera ceux qui habitent dans les hauteurs, il humiliera la cité élevée. Il l’humiliera jusqu’à terre et il la renversera jusque dans la poussière.
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
6 Le pied la foulera, les pieds du pauvre, le pas de l’indigent.
Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
7 Le sentier du juste est droit, droit est le chemin où le juste doit marcher.
Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
8 Et dans le sentier de vos jugements. Seigneur, nous vous avons attendu patiemment; votre nom et votre souvenir sont dans le désir de l’âme.
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
9 Mon âme vous a désiré pendant la nuit; mais et par mon esprit et dans mon cœur, dès le matin je veillerai pour vous. Lorsque vous aurez exercé vos jugements sur la terre, les habitants du globe apprendront la justice.
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
10 Ayons pitié de l’impie, et il n’apprendra pas la justice; dans la terre des saints il a fait des choses iniques, et il ne verra pas la gloire du Seigneur.
Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
11 Seigneur, que votre main s’élève, et qu’ils ne voient pas; qu’ils voient et qu’ils soient confondus, ceux qui sont jaloux de votre peuple et qu’un feu dévore vos ennemis.
Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
12 Seigneur, vous nous donnerez la paix; car vous avez opéré toutes nos œuvres pour nous.
Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
13 Seigneur notre Dieu, des maîtres étrangers nous ont possédés sans vous, que seulement par vous nous nous souvenions de votre nom.
Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
14 Que les morts ne revivent point, que les géants ne ressuscitent point; à cause de cela vous les avez visités et brisés, et vous avez anéanti toute leur mémoire.
Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
15 Vous avez été indulgent envers cette nation, Seigneur, vous avez été indulgent envers cette nation; est-ce que vous n’avez pas été glorifié? Vous avez reculé les frontières de sa terre.
Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
16 Seigneur, dans l’angoisse ils vous ont recherché, dans la tribulation du murmure votre enseignement était avec eux.
Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
17 Comme celle qui a conçu, lorsqu’elle approche de l’enfantement, souffre et crie dans ses douleurs; ainsi nous sommes devenus à votre face, Seigneur.
Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
18 Nous avons conçu, nous avons été comme en travail, nous avons enfanté du vent; nous n’avons pas fait des œuvres de salut sur la terre; c’est pour cela que ne sont pas tombés les habitants de la terre.
Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
19 Ils vivront, vos morts; ceux qui m’ont été tués ressusciteront; réveillez-vous, et chantez des louanges, vous qui habitez dans la poussière; parce que votre rosée, Seigneur, est une rosée de lumière, et que vous réduirez la terre des géants en ruine.
Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
20 Va, mon peuple, entre dans tes chambres; ferme les portes sur toi; cache-toi un peu pour un moment jusqu’à ce que soit passée l’indignation.
Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
21 Car voici que le Seigneur sortira de son lieu, afin de visiter l’iniquité de l’habitant de la terre; et la terre révélera le sang qu’elle a reçu, et elle ne couvrira plus ceux qui avaient été tués sur elle.
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.