< Isaïe 21 >
1 Malheur accablant du désert de la mer. Comme des tourbillons viennent de l’Africus, il vient du désert, d’une terre affreuse.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Une vision pénible m’a été annoncée; celui qui est incrédule agit infidèlement; et celui qui dépeuple, dévaste. Monte, Elam; Mède, assiège; j’ai fait cesser tous ses gémissements.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 À cause de cela mes reins sont remplis de douleur; l’angoisse s’est emparée de moi comme l’angoisse d’une femme en travail; je suis tombé, lorsque j’ai entendu; j’ai été tout troublé, lorsque j’ai vu.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Mon cœur s’est flétri; des ténèbres m’ont frappé de stupeur; Babylone que je chérissais m’est devenue un sujet d’étonnement.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Dresse la table; contemple dans une guérite ceux qui mangent et qui boivent: levez-vous, princes, saisissez le bouclier.
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Car voici ce que m’a dit le Seigneur: Va, et place une sentinelle; et tout ce qu’elle aura vu, qu’elle l’annonce.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Et elle vit un chariot conduit par deux cavaliers, l’un qui montait un âne, et l’autre qui montait un chameau; et elle considéra soigneusement d’un œil très attentif.
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Et elle cria comme un lion: Je suis dans la guérite du Seigneur, m’y tenant continuellement pendant le jour, et je fais ma garde, m’y tenant les nuits entières.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Voici que vient cet homme qui monte le chariot aux deux montures des cavaliers; et il répondit et dit: Elle est tombée, elle est tombée, Babylone, et toutes les images de ses dieux, taillées au ciseau, ont été brisées contre terre.
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 Mon battage, et vous, fils de mon aire, ce que j’ai ouï du Seigneur des armées. Dieu d’Israël, je vous l’ai annoncé.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Malheur accablant de Duma. Il me crie de Séir: Garde, qu’annonces-tu de la nuit? garde, qu’annonces-tu de la nuit?
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Le garde dit: Le matin est venu, et la nuit; si vous cherchez, cherchez; convertissez-vous, venez.
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Malheur accablant dans l’Arabie. Dans le bois, le soir, vous dormirez, dans les sentiers de Dédanim.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 Venant au-devant de celui qui a soif, portez de l’eau, vous qui habitez la terre du midi, avec des pains venez au-devant de celui qui fuit.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Car à la face des glaives ils ont fui, à la face du glaive suspendu, à la face de l’arc bandé, à la face d’un grave combat:
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Parce que voici ce que me dit le Seigneur: Encore une année comptée comme l’année d’un mercenaire, et toute gloire de Cédar sera enlevée.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Et le reste du nombre des forts archers de Cédar seront diminués; car le Seigneur Dieu d’Israël a parlé.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.