< Isaïe 19 >

1 Malheur accablant de l’Egypte. Voici que le Seigneur montera sur un nuage léger, et qu’il entrera dans l’Egypte, et que seront ébranlés les simulacres de l’Egypte devant sa face, et le cœur de l’Egypte se fondra au milieu d’elle.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 Et je ferai courir des Egyptiens contre des Egyptiens; et un homme combattra contre son frère, et un homme contre un ami, une cité contre une cité, un royaume contre un royaume.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 Et l’esprit de l’Egypte sera déchiré dans ses entrailles, et je détruirai son conseil; et ils interrogeront leurs simulacres, et leurs devins, et les pythoniens et les magiciens.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 Et je livrerai l’Egypte à la main de maîtres cruels, et un roi puissant les dominera, dit le Seigneur Dieu des armées.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Et l’eau disparaîtra de la mer, et le fleuve sera détruit et desséché.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 Et les rivières tariront, et les ruisseaux, retenus par des digues, diminueront et seront desséchés. Le roseau et le jonc se flétriront;
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 Le lit du ruisseau sera mis à nu à sa source même, et l’eau dont on arrosait toute semence desséchera, deviendra aride, et ne sera plus.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Et les pêcheurs s’affligeront, et tous ceux qui jettent l’hameçon dans le fleuve pleureront, et ceux qui tendent le filet sur la surface des eaux dépériront.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Ils seront confondus, ceux qui travaillaient le lin, qui le cardaient et en faisaient de fins tissus.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Et ses lieux arrosés d’eau se dessécheront, de même tous ceux qui faisaient des fosses pour prendre des poissons.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Ils sont atteints de folie, les princes de Tanis, les sages conseillers de Pharaon ont donné un conseil insensé. Comment direz-vous à Pharaon: Je suis fils des sages, fils des anciens rois?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Où sont maintenant tes sages? Qu’ils t’annoncent, qu’ils apprennent ce qu’a résolu le Seigneur des armées, touchant l’Egypte.
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Ils sont devenus fous, les princes de Tanis; ils se sont amoindris, les princes de Memphis, ils ont séduit l’Egypte, soutien de ses peuples.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Le Seigneur a répandu au milieu d’elle un esprit de vertige, et ils ont fait errer l’Egypte dans toutes ses œuvres, comme erre l’homme ivre et qui vomit.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Et il n’y aura pour l’Egypte rien à faire à la tête et à la queue, à celui qui plie et à celui qui refrène.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 Et ce jour-là, les Egyptiens seront comme des femmes, et ils s’étonneront, et ils craindront à la vue de la commotion que la main du Seigneur des armées lui-même produira sur eux.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Et la terre de Juda sera à l’Égypte en effroi; quiconque s’en souviendra sera effrayé à la vue du dessein que le Seigneur des armées lui-même a formé contre elle.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 En ce jour-là, il y aura cinq cités dans la terre d’Égypte qui parleront la langue de Chanaan, et qui jureront par le Seigneur des armées; l’une sera appelée la cité du soleil.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 En ce jour-là, il y aura un autel du Seigneur au milieu de la terre d’Égypte, et un monument au Seigneur près de sa frontière.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 Ce sera en signe et en témoignage au Seigneur des armées dans la terre d’Égypte. Car ils crieront vers le Seigneur à la vue de l’oppresseur, et il leur enverra un sauveur et un défenseur, qui les délivrera.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 Et le Seigneur sera connu de l’Égypte, et les Égyptiens en ce jour-là connaîtront le Seigneur; et ils l’honoreront par des hosties et par des offrandes; et ils voueront des vœux et ils les acquitteront.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 Et le Seigneur frappera l’Égypte d’une plaie, et il la guérira; et il s’apaisera pour eux et il les guérira.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 En ce jour-là, il y aura une voie de l’Égypte chez les Assyriens, et l’Assyrien entrera dans l’Égypte, et l’Égyptien chez les Assyriens, et les Égyptiens serviront Assur.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 En ce jour-là, Israël sera réuni comme troisième à l’Égyptien et à l’Assyrien; la bénédiction sera au milieu de la terre,
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 Qu’a bénie le Seigneur des armées, disant: Béni soit mon peuple d’Égypte, et l’ouvrage de mes mains se fera par l’Assyrien, mais mon héritage est Israël.
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaïe 19 >