< Isaïe 15 >
1 Malheur accablant de Moab. Parce que pendant la nuit Ar a été dévastée, Moab s’est tu; parce que pendant la nuit a été détruit le mur, Moab s’est tu.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 La maison et Dibon sont montées sur les hauts lieux pour pleurer sur Nabo et sur Médaba; Moab a poussé des hurlements; sur toutes les têtes sera la calvitie, et toute barbe sera rasée.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 Dans ses rues ils ont été vêtus de sacs; sur ses toits tout hurlement est descendu dans le pleur.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 Hésébon et Eléalé crieront; jusqu’à Jasa leur voix a été entendue; à cause de cela les vaillant de Moab hurleront; et son âme hurlera pour elle-même.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Mon cœur pour Moab criera; ses verrous se feront entendre jusqu’à Ségor, génisse de trois ans; car par la montée de Luith ils monteront en pleurant, et dans la voix d’Oronaïm ils élèveront le cri d’une douleur déchirante.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 Car les eaux de Nemrim deviendront un désert, parce que l’herbe s’est desséchée, que le bourgeon a manqué et que toute verdure a péri.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Selon la grandeur de leurs œuvres, tel sera leur châtiment; au torrent des saules on les conduira.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Parce que le cri parcourra la frontière de Moab; jusqu’à Gallim ira son hurlement, jusqu’au Puits d’Elim son cri.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Parce que les eaux de Dibon ont été remplies de sang; car j’enverrai sur Dibon un surcroît de châtiment; à ceux qui fuiront de Moab et aux restes de cette terre, un lion.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.