< Isaïe 10 >
1 Malheur à ceux qui établissent des lois iniques, et qui écrivant, ont écrit l’injustice;
Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 Afin d’opprimer le pauvre dans le jugement, et de faire violence à la cause des faibles de mon peuple; afin que les veuves soient leur proie, et qu’ils pillent les orphelins!
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
3 Que ferez-vous au jour de la visite et de la calamité, venant de loin? De qui solliciterez-vous le secours, et où abandonnerez-vous votre gloire,
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 Pour n’être point courbés sous la chaîne, et ne point tomber avec les tués? Après toutes ces choses sa fureur n’a pas été détournée, mais sa main est encore étendue.
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
5 Malheur à Assur! la verge et le bâton de ma fureur, c’est lui; dans sa main est mon indignation.
“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
6 Je l’enverrai vers une nation trompeuse, je lui donnerai des ordres contre le peuple de ma fureur, afin qu’il emporte des dépouilles, et qu’il enlève du butin, et qu’il le foule aux pieds comme la boue des places publiques.
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
7 Mais lui-même ne pensera pas ainsi, et son cœur n’aura pas un pareil sentiment; mais son cœur sera porté à la destruction et à la ruine totale d’un grand nombre de nations.
Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9 Est-ce que mes princes ne sont pas autant de rois? Est-ce que Calano n’est pas comme Charcamis; et Emath comme Arphad? est-ce que Samarie n’est pas comme Damas?
‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 De même que ma main a atteint les royaumes des idoles, de même aussi j’atteindrai les simulacres de Jérusalem et de Samarie.
Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 Est-ce que comme j’ai fait à Samarie et à ses idoles, je ne ferai pas à Jérusalem et à ses simulacres?
nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
12 Et il arrivera que, lorsque le Seigneur aura accompli toutes ses œuvres sur la montagne de Sion et dans Jérusalem, je visiterai le fruit du cœur arrogant du roi d’Assur, et la fierté de ses yeux altiers.
Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
13 Car il a dit: Par la force de ma main j’ai fait, par ma sagesse j’ai compris; et j’ai arraché les limites des peuples, et j’ai spolié les princes, et comme puissant j’ai fait descendre ceux qui étaient assis sur un trône élevé.
Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Et ma main a atteint comme un nid la puissance des nations; et de même qu’on recueille des œufs qui ont été abandonnés, de même moi j’ai réuni toute la terre; et il ne s’est trouvé personne qui remuât l’aile et ouvrit la bouche, et fit entendre le moindre cri.
Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
15 Est-ce que la hache se glorifiera contre celui qui s’en sert pour fendre? ou la scie s’élèvera-t-elle contre celui par qui elle est mise en mouvement? C’est comme si la verge s’élevait contre celui qui la lève; et comme si le bâton se glorifiait, lui qui est absolument du bois.
Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 À cause de cela le dominateur. Seigneur des armées, enverra la maigreur au milieu de ses gras: et au-dessous de sa gloire s’allumera et s’enflammera comme un brasier ardent.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
17 Et la lumière d’Israël sera le feu, et son Saint la flamme; et les épines et les ronces d’Assur s’embraseront et seront dévorées dans un seul jour.
Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Et la gloire de sa forêt et de son Carmel, depuis l’âme jusqu’à la chair, sera {consumée; et Assur de frayeur s’enfuira.
Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
19 Et les restes des arbres de sa forêt, à cause de leur petit nombre, se compteront aisément, et un enfant pourra les enregistrer.
Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
20 Et il arrivera en ce jour-là que le reste d’Israël et ceux qui auront échappé de la maison de Jacob, ne s’appuieront plus sur celui qui les frappe, mais ils s’appuieront avec sincérité sur le Seigneur, le saint d’Israël.
Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
21 Les restes se convertiront (les restes de Jacob, dis-je) au Dieu fort.
Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Car lors-même que ton peuple, ô Israël, serait comme le sable de la mer, les restes seulement se convertiront; ces restes, réduits à un petit nombre, abonderont en justice.
Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Car le Seigneur Dieu des armées fera une destruction et un retranchement au milieu de toute la terre.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
24 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu des armées: Mon peuple, habitant de Sion, ne crains pas Assur; avec la verge il te frappera, et il lèvera son bâton sur toi, dans la voie de l’Egypte,
Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Car encore un peu, et un moment, et mon indignation et ma fureur seront à leur comble à cause de leur crime.
Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
26 Et le Seigneur des armées lèvera sur lui le fouet, comme il frappa Madian à la pierre d’Oreb, et sa verge sur la mer, et il la lèvera dans la voie de l’Egypte.
Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 Et il arrivera en ce jour-là, que le fardeau d’Assur sera ôté de ton épaule, et son joug de ton cou; et le joug pourrira à cause de l’huile.
Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
28 Il viendra à Aïath, il passera par Magron; à Machmas il déposera ses bagages.
Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Ils ont passé en courant Gaba, notre campement; Rama a été frappé de stupeur, Gabaath de Saül a pris la fuite.
Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Fais retentir la voix, fille de Gallim: sois attentive, Laïsa et toi aussi, pauvre Anathoth.
Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
31 Médéména a émigré: habitants de Gabim, rassurez-vous.
Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Il est encore jour pour s’arrêter à Nobé; il agitera sa main contre la montagne de la fille de Sion, et la colline de Jérusalem.
Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
33 Voici que le dominateur, Seigneur des armées, brisera la petite bouteille par la terreur; et les plus élevés par la taille seront coupés par le bas, et les grands seront humiliés.
Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Et les parties épaisses de la forêt seront abattues, et le Liban avec ses hauts cèdres tombera.
Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.