< Osée 6 >
1 Dans leur tribulation, ils se lèveront dès le matin pour venir vers moi: Venez, et retournons au Seigneur.
“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
2 Parce que c’est lui qui nous a pris et qui nous sauvera; il nous frappera et il nous guérira;
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 Il nous rendra la vie après deux jours; au troisième jour, il nous ressuscitera, et nous vivrons en sa présence. Nous connaîtrons, et nous chercherons à connaître, le Seigneur; comme le point du jour a été préparée sa sortie, et il viendra pour nous comme la pluie de la première et de l’arrière-saison.
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 Que ferai-je pour toi, Ephraïm? Que ferai-je pour toi, Juda? Votre miséricorde est comme la nuée du matin et comme la rosée qui se dissipe.
Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 À cause de cela, je les ai traités durement par les prophètes, je les ai tués par les paroles de ma bouche; et tes jugements éclateront comme la lumière.
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 Parce que c’est la miséricorde que je veux et non le sacrifice, et la science de Dieu plus que les holocaustes.
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
7 Mais eux comme Adam, ils ont prévariqué contre moi.
Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
8 Galaad est une cité de fabricateurs d’idoles, renversée par le sang.
Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
9 Et elle est comme le gosier des voleurs altéré de carnage, alliée aux prêtres qui sur la voie tuent ceux qui viennent de Sichem; parce qu’ils sont livrés au crime.
Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
10 Dans la maison d’Israël j’ai vu une chose horrible; là sont les fornications d’Ephraïm; Israël s’est souillé.
Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
11 Mais toi aussi, Juda, prépare-toi une moisson, lorsque je ramènerai de la captivité mon peuple.
“Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”