< Hébreux 13 >

1 Que la charité fraternelle demeure en vous:
Pitirizani kukondana monga abale.
2 Et ne négligez pas l’hospitalité, car c’est par elle que quelques-uns ont donné, sans le savoir, l’hospitalité à des anges.
Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa.
3 Souvenez-vous de ceux qui sont dans les liens, comme si vous y étiez avec eux; et des affligés, comme demeurant vous-mêmes dans un corps.
Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.
4 Que le mariage soit honoré en toutes choses, et le lit nuptial sans souillure; car les fornicateurs et les adultères. Dieu les jugera.
Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga.
5 Que votre vie soit sans avarice, vous contentant de ce que vous avez; car lui-même a dit: Je ne t’abandonnerai ni ne te délaisserai.
Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati, “Sadzakusiyani, kapena kukutayani konse.”
6 Ainsi, disons avec confiance: Le Seigneur m’est aide; je ne craindrai point ce qu’un homme peut me faire.
Kotero ife tikunena molimba mtima kuti, “Ambuye ndiye mthandizi wanga; sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”
7 Souvenez-vous de vos préposés qui vous ont prêché la parole de Dieu; et considérant la fin de leur vie, imitez leur foi.
Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo.
8 Jésus-Christ était hier, il est aujourd’hui, et il sera le même dans tous les siècles. (aiōn g165)
Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn g165)
9 Ne vous laissez point emporter à des doctrines diverses et étrangères. Car il est bon d’affermir le cœur par la grâce, et non par des distinctions de viandes, lesquelles n’ont point servi à ceux qui s’y conformaient.
Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya.
10 Nous avons un autel dont n’ont pas le droit de manger ceux qui servent dans le tabernacle.
Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.
11 Car les corps des animaux dont le sang est porté par le pontife dans le sanctuaire sont brûlés hors du camp.
Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa.
12 C’est pourquoi Jésus lui-même, pour sanctifier le peuple par son sang, a souffert hors de la porte.
Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake.
13 Allons donc à lui hors du camp, portant son opprobre.
Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake.
14 Car nous n’avons point ici de cité permanente, mais nous cherchons la cité future.
Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.
15 Par lui donc offrons à Dieu une hostie de louange, c’est-à-dire le fruit de lèvres qui confessent son nom.
Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.
16 N’oubliez point non plus la charité et la communication de vos biens; car c’est par de telles hosties qu’on se concilie Dieu.
Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere.
17 Obéissez à vos préposés, et soyez-leur soumis (car ce sont eux qui veillent, comme devant rendre compte de vos âmes), afin qu’ils le fassent avec joie, et non en gémissant; cela ne vous serait pas avantageux.
Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.
18 Priez pour nous; car nous croyons avoir une bonne conscience, voulant en toutes choses nous bien conduire.
Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu.
19 Et je vous conjure, avec une nouvelle instance, de le faire, afin que je vous sois plus tôt rendu.
Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.
20 Que le Dieu de paix, qui, par le sang du testament éternel, a retiré d’entre les morts le grand pasteur des brebis, Notre-Seigneur Jésus-Christ, (aiōnios g166)
Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios g166)
21 Vous rende propres à tout bien, afin que vous fassiez sa volonté; lui-même faisant eu vous ce qui lui est agréable, par Jésus-Christ à qui est la gloire dans les siècle des siècles. Amen. (aiōn g165)
akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn g165)
22 Je vous prie, mes frères, d’agréer cette parole de consolation, car je ne vous ai écrit qu’en peu de mots.
Ndikukupemphani abale kuti mulandire mawu anga achilimbikitso, pakuti ndakulemberani mwachidule.
23 Sachez que notre frère Timothée est en liberté; c’est avec lui (s’il vient bientôt) que je vous verrai.
Ine ndikufuna kuti inu mudziwe kuti mʼbale wathu Timoteyo wamasulidwa. Ngati iye angafike msanga ndibwera naye kudzakuonani.
24 Saluez tous vos préposés et tous les saints. Les frères d’Italie vous saluent.
Mupereke moni kwa atsogoleri anu onse ndiponso kwa anthu onse a Mulungu. Abale ochokera ku Italiya akupereka moni.
25 Que la grâce soit avec vous tous. Amen.
Chisomo chikhale ndi inu nonse.

< Hébreux 13 >