< Genèse 24 >

1 Or Abraham était vieux et plein de jours; et le Seigneur l’avait béni en toutes choses.
Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
2 Et il dit au serviteur le plus ancien de sa maison, qui présidait sur tout ce qu’il avait: Pose ta main sous ma cuisse,
Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
3 Afin que je t’adjure par le Seigneur Dieu du ciel et de la terre, que tu ne prendras pas de femme pour mon fils parmi les filles des Chananéens au milieu desquels j’habite;
Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
4 Mais que tu iras dans mon pays et dans ma parenté, et que c’est de là que tu prendras une femme pour mon fils Isaac.
koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
5 Le serviteur répondit: Si la femme ne veut pas venir avec moi dans ce pays-ci, dois-je remener votre fils dans le lieu d’où vous êtes sorti?
Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
6 Et Abraham dit: Garde-toi de jamais y remener mon fils
Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
7 Le Seigneur Dieu du ciel qui m’a tiré de la maison de mon père et du pays de ma naissance, qui m’a parlée et m’a juré, disant: C’est à ta postérité que je donnerai ce pays, enverra lui-même son ange devant toi, et tu prendras de là une femme pour mon fils.
Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
8 Que si la femme ne veut pas te suivre, tu ne seras pas engagé par le serment; seulement ne remène jamais là mon fils.
Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
9 Le serviteur donc posa la main sous la cuisse d’Abraham son maître, et il le lui jura.
Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
10 C’est pourquoi il prit dix chameaux du troupeau de son maître, et s’en alla portant avec lui de tous ses biens; et étant parti, il se dirigea en Mésopotamie, vers la ville de Nachor.
Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
11 Et lorsqu’il eut fait agenouiller ses chameaux hors de la ville, près du puits, sur le soir, temps où les jeunes filles ont coutume de sortir pour puiser de l’eau, il dit:
Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
12 Seigneur Dieu de mon maître Abraham, je vous supplie, venez-moi en aide aujourd’hui, et faites miséricorde à mon maître Abraham.
Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
13 Me voici près de la source d’eau, et les filles des habitants de cette ville sortiront pour puiser de l’eau.
Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
14 Que la jeune fille donc à qui je dirai: Incline ta cruche, afin que je boive, et qui répondra: Bois, et je donnerai aussi à boire à tes chameaux, soit celle que vous avez préparée à votre serviteur Isaac: et c’est à cela que je connaîtrai que vous aurez fait miséricorde à mon maître.
Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
15 Il n’avait pas encore achevé ces mots en lui-même, et voilà que sortit Rébecca, la fille de Bathuel, fils de Melcha, femme de Nachor, frère d’Abraham, laquelle portait une cruche sur son épaule;
Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
16 Jeune fille fort gracieuse, vierge très belle et inconnue à tout homme: or elle était déjà descendue à la fontaine, avait rempli sa cruche, et elle s’en retournait.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
17 Aussitôt le serviteur courut au-devant d’elle, et dit: Donne-moi un peu d’eau à boire de ta cruche.
Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
18 Elle répondit: Bois, mon seigneur; et elle posa promptement sa cruche sur son bras, et elle lui donna à boire.
Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
19 Et lorsqu’il eut bu, elle ajouta: Et même pour tes chameaux je puiserai de l’eau, jusqu’à ce que tous aient bu.
Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
20 Et versant sa cruche dans les canaux, elle courut au puits pour puiser de l’eau, et quand elle l’eut puisée, elle la donna à tous les chameaux.
Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
21 Cependant lui la contemplait en silence, voulant savoir si le Seigneur avait rendu son voyage heureux ou non.
Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
22 Or, après que les chameaux eurent bu, cet homme lui présenta des pendants d’oreilles d’or, pesant deux sicles, et autant de bracelets du poids de dix sicles.
Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
23 Puis il dit: De qui es-tu fille? dis-le moi: y a-t-il dans la maison de ton père un lieu pour y loger?
Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
24 Elle répondit: Je suis la fille de Bathuel, fils de Melcha et que lui a engendré Nachor.
Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
25 Et elle ajouta, disant: Il y a chez nous beaucoup de foin et de paille, et un lieu spacieux pour y loger.
Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
26 L’homme s’inclina, et adora le Seigneur,
Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
27 Disant: Béni le Seigneur Dieu de mon maître Abraham, qui ne lui a pas retiré sa miséricorde et sa fidélité, et qui m’a conduit par une voie droite dans la maison du frère de mon maître!
nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
28 C’est pourquoi la jeune fille courut et annonça à la maison de sa mère tout ce qu’elle avait entendu.
Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
29 Or Rébecca avait un frère du nom de Laban, qui sortit en grande hâte pour aller vers l’homme là où était la fontaine.
Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
30 Et, comme il avait vu les pendants d’oreilles et les bracelets aux mains de sa sœur, et qu’il avait entendu toutes ses paroles, lorsqu’elle disait: Ainsi m’a parlé cet homme, il vint vers l’homme, qui se tenait à côté de ses chameaux et près de la source d’eau.
Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
31 Et il lui dit: Entre, béni du Seigneur; pourquoi restes-tu dehors? J’ai préparé la maison et un lieu pour tes chameaux.
Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
32 Puis il le fit entrer dans le logis, dessangla les chameaux, leur donna de la paille et du foin, et à lui-même et à ceux qui étaient venus avec lui, de l’eau pour laver leurs pieds.
Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
33 On mit aussi du pain en sa présence. Il dit: Je ne mangerai pas que je ne vous aie énoncé mon message. Laban lui répondit: Parle.
Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
34 Alors lui: Je suis, dit-il, serviteur d’Abraham.
Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
35 Le Seigneur a béni beaucoup mon maître, et il est devenu grand; car il lui a donné des brebis et des bœufs, de l’argent et de l’or, des serviteurs et des servantes, des chameaux et des ânes.
Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
36 Et Sara la femme de mon maître lui a enfanté un fils dans sa vieillesse, et il lui a donné tout ce qu’il avait.
Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
37 Et mon maître m’a adjuré, disant: Tu ne prendras point de femme pour mon fils parmi les filles des Chananéens dans le pays desquels j’habite;
Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
38 Mais tu iras à la maison de mon père, et tu prendras dans ma parenté une femme pour mon fils.
koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
39 Et moi j’ai répondu à mon maître: Mais si la femme ne veut pas venir avec moi?
“Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
40 Le Seigneur, reprit-il, en présence de qui je marche, enverra son ange avec toi, et dirigera ta voie; et tu prendras une femme pour mon fils dans ma parenté et de la maison de mon père.
“Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
41 Tu seras exempt de ma malédiction, si tu vas vers mes parents et qu’ils te refusent.
Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
42 Je suis donc venu aujourd’hui près de la source d’eau, et j’ai dit: Seigneur Dieu de mon maître Abraham, si vous avez dirigé la voie dans laquelle je marche maintenant,
“Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
43 Me voici près de la source d’eau; que la vierge donc qui sortira pour puiser de l’eau, qui entendra de moi: Donne-moi un peu d’eau à boire de ta cruche,
taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
44 Et qui me répondra: Bois, toi; je puiserai ensuite de l’eau pour tes chameaux, soit la femme que le Seigneur a préparée au fils de mon maître.
ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
45 Pendant que sans rien dire, j’agitais ces pensées au-dedans de moi-même, parut Rébecca venant avec sa cruche qu’elle portait sur l’épaule: elle descendit à la fontaine et puisa de l’eau. Et je lui dis: Donne-moi un peu à boire.
“Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
46 Elle se hâtant, descendit sa cruche de dessus son épaule et me dit: Bois, toi; je donnerai ensuite à boire à tes chameaux. Je bus, et elle abreuva les chameaux.
“Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
47 Je l’interrogeai alors, et je dis: De qui es-tu fille? Elle répondit: Je suis fille de Bathuel, fils de Nachor, que lui a enfanté Melcha. Je lui ai donc mis les pendants d’oreilles pour orner son visage, et j’ai attaché les bracelets à ses bras.
“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
48 Et incliné, j’ai adoré le Seigneur, bénissant le Seigneur Dieu de mon maître Abraham, qui m’a conduit par une voie droite, afin de prendre la fille du frère de mon maître pour son fils.
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
49 C’est pourquoi, si vous agissez avec miséricorde et loyauté envers mon maître, dites-le-moi; mais si autre chose vous plaît, dites-le-moi encore; afin que j’aille à droite ou à gauche.
Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
50 Laban et Bathuel répondirent: C’est du Seigneur qu’est sortie cette parole; nous ne pouvons en dehors de sa volonté, te dire rien autre chose.
Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
51 Voici Rébecca devant toi: prends-la, pars, et qu’elle soit la femme du fils de ton maître, selon qu’a parlé le Seigneur.
Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
52 Ce qu’ayant entendu le serviteur d’Abraham, se prosternant en terre, il adora le Seigneur.
Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
53 Puis, tirant des vases d’or et d’argent, et des vêtements, il les donna à Rébecca en présent; et à ses frères et à sa mère, il offrit aussi des dons.
Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
54 Le repas commencé, mangeant ensemble et buvant, ils demeurèrent là. Mais se levant le matin, le serviteur dit: Laissez-moi partir, afin que j’aille vers mon maître.
Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
55 Les frères de Rébecca et sa mère répondirent: Que la jeune fille demeure au moins dix jours auprès de nous, et ensuite elle partira.
Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
56 Ne me retenez pas, reprit-il, puisque le Seigneur a dirigé ma voie: laissez-moi partir, afin que j’aille vers mon maître.
Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
57 Et ils dirent: Appelons la jeune fille, et demandons-lui ce qu’elle veut.
Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
58 Lorsque appelée, elle fut venue, ils lui demandèrent: Veux-tu aller avec cet homme? Elle dit: J’irai.
Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
59 Ils renvoyèrent donc, elle, sa nourrice, le serviteur d’Abraham et ses compagnons.
Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
60 Implorant des choses heureuses pour leur sœur, et disant: Tu es notre sœur; puisses-tu croître en mille et mille générations, et puisse ta postérité posséder les portes de ses ennemis!
Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
61 Ainsi Rébecca et ses servantes étant montées sur les chameaux, suivirent le serviteur qui en grande hâte retournait vers son maître.
Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
62 En ce même temps se promenait Isaac dans le chemin qui mène au puits dont le nom est puits Du vivant et voyant; car il habitait dans la terre australe.
Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
63 Et il était sorti pour méditer dans la campagne, le jour étant déjà sur son déclin: et comme il avait levé les yeux, il vit les chameaux venant de loin.
Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
64 Rébecca aussi, Isaac aperçu, descendit de son chameau,
Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
65 Et dit au serviteur: Quel est cet homme qui vient par la campagne, à notre rencontre? Et il lui dit: C’est mon maître. Et elle, prenant aussitôt son voile, se couvrit.
nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
66 Or le serviteur raconta tout ce qu’il avait fait, à Isaac,
Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
67 Qui conduisit Rébecca dans la tente de Sara sa mère, et la reçut pour femme: et il l’aima tellement, qu’il tempéra la douleur qu’il avait eue de la mort de sa mère.
Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.

< Genèse 24 >