< Genèse 20 >

1 Parti de là pour la terre australe, Abraham habita entre Cadès et Sur, et demeura comme étranger à Gérara.
Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
2 Or il dit de Sara sa femme: C’est ma sœur. Abimélech, roi de Gérara, envoya donc vers lui et la fit enlever.
ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
3 Mais Dieu vint vers Abimélech dans un songe pendant la nuit, et lui dit: Voilà que tu mourras, à cause de la femme que tu as enlevée; car elle a un mari.
Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
4 Or Abimélech ne l’avait pas touchée, et il dit: Seigneur, perdrez-vous une nation qui est dans l’ignorance, et innocente?
Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
5 Lui-même ne m’a-t-il pas dit: C’est ma sœur? Et elle-même n’a-t-elle pas dit: C’est mon frère? C’est dans la simplicité de mon cœur et dans la pureté de mes mains que je l’ai fait.
Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
6 Et Dieu lui dit: Et moi aussi je sais que c’est avec un cœur simple que tu l’as fait; et c’est pour cela que je t’ai gardé, afin que tu ne péchasses pas contre moi, et que je n’ai pas permis que tu la touchasses.
Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
7 Maintenant donc rends à son mari cette femme; parce que c’est un prophète, et il priera pour toi, et tu vivras; mais si tu ne la rends pas, sache que tu mourras de mort, toi et tout ce qui est à toi.
Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
8 Aussitôt, se levant de nuit, Abimélech appela tous ses serviteurs, et fit entendre toutes ces paroles à leurs oreilles; et tous ces hommes furent saisis d une grande crainte.
Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
9 Puis Abimélech appela aussi Abraham et lui dit: Que nous as-tu fait? et en quoi t’avons-nous offensé, pour que tu aies attiré sur moi et sur mon royaume un si grand péché? ce que tu ne devais pas faire, tu nous l’as fait.
Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
10 Et de nouveau se plaignant, il dit: Qu’as-tu vu, pour agir ainsi?
Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
11 Abraham répondit: J’ai pensé en moi-même, disant: Peut-être n’y a-t-il point la crainte de Dieu en ce lieu-ci, et ils me feront mourir à cause de ma femme.
Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
12 D’ailleurs elle est vraiment aussi ma sœur, étant fille de mon père, quoiqu’elle ne soit pas fille de ma mère; et je l’ai prise pour femme.
Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
13 Or quand Dieu me fit sortir de la maison de mon père, je dis à Sara: Tu me feras cette grâce: dans tous les lieux où nous irons, tu diras que je suis ton frère.
Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
14 Abimélech prit donc des brebis, des bœufs, des serviteurs et des servantes, et il les donna à Abraham; et il lui rendit Sara sa femme.
Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
15 Et il dit: La terre est devant vous; partout où il te plaira, habites-y.
Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
16 Mais à Sara il dit: Voilà que j’ai donné à ton frère mille pièces d’argent, pour que tu aies un voile sur les yeux devant tous ceux qui seront avec toi, et en quelque lieu que tu ailles: et souviens-toi que tu as été enlevée.
Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
17 Mais Abraham ayant prié, Dieu guérit Abimélech, sa femme et ses servantes, et elles enfantèrent;
Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
18 Car le Seigneur avait frappé de stérilité toute la maison d’Abimélech, à cause de Sara femme d’Abraham.
Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.

< Genèse 20 >