< Ézéchiel 38 >
1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d’un homme, tourne ta face vers Gog, vers la terre de Magog, prince et chef de Mosoch et de Thubal, et prophétise sur lui,
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 Et tu lui diras: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voilà que je viens vers toi, Gog, prince et chef de Mosoch et de Thubal;
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Et je te ferai tourner de tous côtés, et je mettrai un frein dans tes mâchoires; et je te ferai sortir, toi et toute ton armée, tous tes chevaux, et tes cavaliers couverts de cuirasses, et la grande multitude de ceux qui ont pris la lance, le bouclier et le glaive.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Les Perses, les Ethiopiens, et les Libyens seront avec eux, tous armés de boucliers et coiffés d’un casque.
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer et tous ses bataillons, la maison de Thogorma, les côtés de l’aquilon, et toute sa force, et des peuples nombreux seront avec toi.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Prépare-toi et dispose-toi avec toute ta multitude qui s’est rassemblée auprès de toi; et prends le commandement sur eux.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 , Après de longs jours tu seras visité; et dans les dernières années tu viendras dans une terre qui a échappé au glaive, et a été rassemblée d’entre des peuples nombreux vers les montagnes d’Israël qui furent continuellement désertes; cette terre a été retirée d’entre les peuples, et ils y habiteront tous avec confiance.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Mais, montant comme une tempête et comme un nuage, tu viendras, afin que tu couvres la terre, toi, et tous tes bataillons, et des peuples nombreux avec toi.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: En ce jour-là, des projets monteront dans ton cœur et tu penseras une pensée très mauvaise;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Et tu diras: Je monterai dans une terre sans mur; je viendrai vers ceux qui demeurent en repos, et qui habitent en sécurité; tous ceux-là habitent sans mur; ils n’ont ni verrous ni portes;
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Afin que tu ravisses des dépouilles, et que tu saisisses une proie; que tu portes ta main sur ceux qui avaient été abandonnés et qui après cela ont été rétablis, et sur un peuple qui a été rassemblé d’entre des nations, et qui commençait à posséder, et à être habitant de l’éminence de la terre.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Saba et Dédan, et les marchands de Tharsis, et tous ses lions te diront: Est-ce que tu ne viens pas pour prendre des dépouilles? Voici que tu as rassemblé ta multitude pour saisir une proie, afin d’emporter de l’argent et de l’or, et d’enlever des meubles et des richesses, et d’emporter un butin immense.
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 À cause de cela, prophétise, fils d’un homme, et dis à Gog: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: N’est-ce pas qu’en ce jour-là, lorsque mon peuple Israël habitera avec confiance, tu le sauras?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 Et tu viendras de ton lieu, des côtés de l’aquilon, toi, et des peuples nombreux avec toi, tous montés sur des chevaux, grande assemblée et armée redoutable.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Et tu monteras contre mon peuple Israël comme un nuage, afin de couvrir la terre. Tu seras dans les derniers jours, et je t’amènerai sur ma terre, afin que les nations me connaissent, lorsque j’aurai été sanctifié en toi, à leurs yeux, ô Gog.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Toi donc tu es celui dont j’ai parlé dans les jours anciens par l’entremise de mes serviteurs les prophètes d’Israël, qui ont prophétisé dans les jours de ces temps-là que je t’amènerais contre eux.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Et il arrivera en ce jour-là, au jour de la venue de Gog sur la terre d’Israël, dit le Seigneur Dieu, mon indignation montera jusqu’à la fureur.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Et c’est dans mon zèle, dans le feu de ma colère, que j’ai parlé. Parce qu’en ce jour-là il y aura une grande commotion dans la terre d’Israël;
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Et ils seront violemment agités devant ma face, les poissons de la mer, et les oiseaux du ciel, et les bêtes de la campagne, et tout reptile qui se meut sur la terre, et tous les hommes qui sont sur la face de la terre; et les montagnes seront renversées, et les haies tomberont, et toute muraille s’écroulera sur le sol.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Et j’appellerai contre lui sur toutes mes montagnes le glaive, dit le Seigneur Dieu; et le glaive de chacun sera dirigé contre son frère.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 J’exercerai mes jugements sur lui par la peste, et par le sang, et par une pluie violente, et par des pierres énormes, et je ferai pleuvoir le feu et le soufre sur lui, et sur son armée, et sur les peuples nombreux qui sont avec lui.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Et je serai glorifié, et je serai sanctifié, et je serai connu aux yeux d’un grand nombre de nations; et ils sauront que je suis le Seigneur.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”