< Ézéchiel 35 >
1 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d’un homme, tourne ton visage contre le mont de Séir; prophétise sur lui, et tu lui diras:
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voilà que je viens vers toi, mont de Séir, et j’étendrai ma main sur toi, et je te rendrai désolé et désert.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Tes villes, je les détruirai et tu seras désert; et tu sauras que je suis le Seigneur.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Parce que tu as été un ennemi éternel, et que tu as renfermé les fils d’Israël dans la main du glaive au temps de leur affliction au temps de leur iniquité extrême;
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 À cause de cela, je vis, moi, dit le Seigneur Dieu; je te livrerai au sang, et le sang te poursuivra; et puisque tu as haï le sang, le sang te poursuivra.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Et je rendrai le mont de Séir désolé et désert; et j’en retrancherai l’allant et le revenant.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 Et je remplirai ses montagnes de ses morts; sur tes collines, dans tes vallées, et le long de tes torrents, les tués sous le glaive tomberont.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Je te réduirai en solitudes éternelles; et tes cités ne seront pas habitées; et vous saurez que je suis le Seigneur Dieu.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Parce que tu as dit: Deux nations et deux terres seront à moi, et je les posséderai en héritage, quoique le Seigneur y fût;
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 À cause de cela, je vis, moi, dit le Seigneur Dieu, j’agirai selon ta colère et selon ta jalousie que tu as exercées, parce que tu les haïssais; et je me ferai connaître par eux, lorsque je t’aurai jugé.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Tu sauras que moi, le Seigneur, j’ai entendu toutes les paroles outrageantes que tu as proférées contre les montagnes d’Israël, en disant: Ce sont des déserts; ils nous ont été donnés pour être dévorés.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Et vous vous êtes élevés contre moi par votre bouche, et vous avez prononcé dédaigneusement contre moi vos paroles; moi j’ai entendu.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Lorsque toute la terre se réjouira, je te réduirai en une solitude.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 Comme tu t’es réjoui sur l’héritage de la maison d’Israël, de ce qu’elle avait été dévastée, ainsi je te ferai; tu seras dévasté, mont de Séir, et toute l’Idumée; et ils sauront que je suis le Seigneur Dieu.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”