< Ézéchiel 31 >
1 Et il arriva en la onzième année, au troisième mois, au premier jour du mois, que la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils d’un homme, dis à Pharaon, roi d’Egypte, et à son peuple: À qui es-tu devenu semblable dans ta grandeur?
“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti, “‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?
3 Voilà qu’Assur était comme un cèdre sur le Liban, beau en ses branches, abondant en feuillage, et d’une hauteur très élevée, et entre des rameaux touffus montait sa cime.
Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni, wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango. Unali wautali, msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.
4 Des eaux l’ont nourri; l’abîme l’a fait pousser en haut; ses fleuves coulaient autour de ses racines, et il a envoyé ses ruisseaux vers tous les arbres de la campagne.
Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo, akasupe ozama ankawutalikitsa. Mitsinje yake inkayenda mozungulira malo amene unaliwo ndipo ngalande zake zinkafika ku mitengo yonse ya mʼmunda.
5 À cause de cela, sa hauteur s’est élevée au-dessus de tous les arbres de la contrée, et ses branches se sont multipliées; et ses rameaux se sont élevés, arrosés par les grandes eaux.
Choncho unatalika kwambiri kupambana mitengo yonse ya mʼmunda. Nthambi zake zinachuluka ndi kutalika kwambiri, chifukwa inkalandira madzi ambiri.
6 Et, lorsqu’il eut étendu son ombre, tous les volatiles du ciel firent leur nid sur ses rameaux, et sous son feuillage toutes les bêtes des forêts déposèrent leurs petits, et sous son ombrage habitait une troupe de nations très nombreuses.
Mbalame zonse zamlengalenga zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo. Nyama zakuthengo zonse zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake. Mitundu yotchuka ya anthu inkakhala mu mthunzi wake.
7 Et il était très beau dans sa grandeur et dans l’étendue de ses branches, car sa racine était près des grandes eaux.
Unali wokongola kwambiri, wa nthambi zake zotambalala, chifukwa mizu yake inazama pansi kumene kunali madzi ochuluka.
8 Les cèdres n’étaient pas plus élevés dans le paradis de Dieu, les sapins n’égalaient pas sa cime, et les platanes ne lui étaient pas égaux en feuillage; aucun arbre du paradis de Dieu ne fut comparable à lui et à sa beauté.
Mʼmunda wa Mulungu munalibe mkungudza wofanana nawo, kapena mitengo ya payini ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake. Munalibenso mtengo wa mkuyu nthambi zofanafana ndi zake. Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse wofanana ndi iwo kukongola kwake.
9 Parce que je le fis si beau, et avec des feuilles si nombreuses et si épaisses, tous les arbres de délices, qui étaient dans le paradis de Dieu, lui ont porté envie.
Ine ndinawupanga wokongola wa nthambi zochuluka. Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa Mulungu inawuchitira nsanje.
10 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu: Parce qu’il s’est élevé en hauteur, et qu’il a poussé sa cime verdoyante et touffue, et que son cœur s’est enorgueilli dans sa grandeur,
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake,
11 Je l’ai livré à la main de l’homme le plus fort des nations, qui agira comme il voudra; selon son impiété je l’ai rejeté.
ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake.
12 Et des étrangers, et les hommes les plus cruels des nations le couperont par le pied, et le jetteront sur les montagnes; et dans toutes les vallées tomberont ses rameaux, et ses branches seront brisées sur tous les rochers de la terre; et tous les peuples de la terre se retireront de son ombrage et l’abandonneront.
Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya.
13 Dans ses ruines ont habité tous les volatiles du ciel, et dans ses rameaux ont demeuré toutes les bêtes de la contrée.
Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake.
14 C’est pour cette raison qu’aucun arbre planté sur les eaux ne s’élèvera dans sa hauteur, et il ne portera pas son sommet au milieu de rameaux touffus et feuillus, et aucun de ceux qui sont arrosés par les eaux ne se soutiendra dans son élévation, parce que tous ont été livrés à la mort, précipités au fond de la terre, au milieu des fils des hommes, avec ceux qui descendent dans la fosse.
Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.
15 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Au jour qu’il est descendu aux enfers, j’ai fait faire un deuil, je l’ai couvert de l’abîme; et j’ai arrêté ses fleuves, et retenu les grandes eaux: le Liban a été attristé sur lui, et tous les arbres des champs ont été ébranlés. (Sheol )
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol )
16 Par le bruit de sa ruine, j’ai agité des nations, lorsque je le conduisais dans l’enfer avec ceux qui descendent dans la fosse; et ils se sont consolés au fond de la terre, tous les arbres de délices, beaux et magnifiques du Liban, tous ceux qui étaient arrosés par les eaux. (Sheol )
Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol )
17 Car eux-mêmes aussi descendront avec lui dans l’enfer parmi les tués par le glaive; et le bras de chacun d’eux restera immobile sous son ombrage au milieu des nations. (Sheol )
Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol )
18 À qui as-tu été assimilé, ô illustre et sublime entre les arbres de délices? Voilà que tu as été précipité au plus profond de la terre avec les arbres de délices, tu dormiras au milieu des incirconcis, avec ceux qui ont été tués par le glaive; c’est là Pharaon lui-même et toute sa multitude, dit le Seigneur Dieu.
“‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo. “‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’”